Hoseya 4 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 4:1-19

Yehova Ayimba Mlandu Israeli

1Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,

chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu

amene mumakhala mʼdzikoli:

“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi

mulibe kulabadira za Mulungu.

2Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.

Kuba ndi kuchita chigololo;

machimo achita kunyanya

ndipo akungokhalira kuphana.

3Chifukwa chake dziko likulira

ndipo onse amene amakhalamo akuvutika;

zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga

ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.

4“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,

wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,

pakuti anthu ako ali ngati anthu

amene amayimba mlandu wansembe.

5Mumapunthwa usana ndi usiku

ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi.

Choncho ndidzawononga amayi anu.

6Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa.

“Pakuti mwakana kudziwa,

Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;

chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,

Inenso ndidzayiwala ana anu.

7Ansembe ankati akachuluka

iwo ankandichimwiranso kwambiri;

iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.

8Amalemererapo pa machimo a anthu anga

ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.

9Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.

Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,

ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.

10“Iwo azidzadya koma sadzakhuta;

azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,

chifukwa anasiya Yehova

kuti adzipereke 11ku zachiwerewere,

ku vinyo wakale ndi watsopano,

zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu

12za anthu anga.

Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo

ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.

Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;

iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.

13Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri

ndi kufukiza lubani pa zitunda,

pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,

pamene pali mthunzi wabwino.

Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere

ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.

14“Ine sindidzalanga ana anu aakazi

pamene iwo adzachita zachiwerewere,

kapena akazi a ana anu

pamene adzachita zigololo.

Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,

ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.

Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!

15“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,

Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.

“Usapite ku Giligala.

Usapite ku Beti-Aveni.

Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’

16Aisraeli ndi nkhutukumve,

ngosamva ngati ana angʼombe.

Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji

ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?

17Efereimu waphathana ndi mafano;

mulekeni!

18Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha,

amapitiriza kuchita zachiwerewere;

atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.

19Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu

ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

King James Version

Hosea 4:1-19

1Hear the word of the LORD, ye children of Israel: for the LORD hath a controversy with the inhabitants of the land, because there is no truth, nor mercy, nor knowledge of God in the land. 2By swearing, and lying, and killing, and stealing, and committing adultery, they break out, and blood toucheth blood.4.2 blood: Heb. bloods 3Therefore shall the land mourn, and every one that dwelleth therein shall languish, with the beasts of the field, and with the fowls of heaven; yea, the fishes of the sea also shall be taken away. 4Yet let no man strive, nor reprove another: for thy people are as they that strive with the priest. 5Therefore shalt thou fall in the day, and the prophet also shall fall with thee in the night, and I will destroy thy mother.4.5 destroy: Heb. cut off

6¶ My people are destroyed for lack of knowledge: because thou hast rejected knowledge, I will also reject thee, that thou shalt be no priest to me: seeing thou hast forgotten the law of thy God, I will also forget thy children.4.6 destroyed: Heb. cut off 7As they were increased, so they sinned against me: therefore will I change their glory into shame. 8They eat up the sin of my people, and they set their heart on their iniquity.4.8 set…: Heb. lift up their soul to 9And there shall be, like people, like priest: and I will punish them for their ways, and reward them their doings.4.9 punish: Heb. visit upon4.9 reward: Heb. cause to return 10For they shall eat, and not have enough: they shall commit whoredom, and shall not increase: because they have left off to take heed to the LORD. 11Whoredom and wine and new wine take away the heart.

12¶ My people ask counsel at their stocks, and their staff declareth unto them: for the spirit of whoredoms hath caused them to err, and they have gone a whoring from under their God. 13They sacrifice upon the tops of the mountains, and burn incense upon the hills, under oaks and poplars and elms, because the shadow thereof is good: therefore your daughters shall commit whoredom, and your spouses shall commit adultery. 14I will not punish your daughters when they commit whoredom, nor your spouses when they commit adultery: for themselves are separated with whores, and they sacrifice with harlots: therefore the people that doth not understand shall fall.4.14 I will not: or, Shall I not4.14 fall: or, be punished

15¶ Though thou, Israel, play the harlot, yet let not Judah offend; and come not ye unto Gilgal, neither go ye up to Beth-aven, nor swear, The LORD liveth. 16For Israel slideth back as a backsliding heifer: now the LORD will feed them as a lamb in a large place. 17Ephraim is joined to idols: let him alone. 18Their drink is sour: they have committed whoredom continually: her rulers with shame do love, Give ye.4.18 sour: Heb. gone4.18 rulers: Heb. shields 19The wind hath bound her up in her wings, and they shall be ashamed because of their sacrifices.