Mkwiyo wa Yehova pa Israeli
1Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;
anali wolemekezeka mu Israeli.
Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;
akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,
zifanizo zopangidwa mwaluso,
zonsezo zopangidwa ndi amisiri.
Amanena za anthu awa kuti,
“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe
ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,
ngati mame amene amakamuka msanga,
ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,
ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
amene ndinakutulutsani mu Igupto.
Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,
palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5Ndinakusamalira mʼchipululu,
mʼdziko lotentha kwambiri.
6Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;
iwo atakhuta anayamba kunyada;
ndipo anandiyiwala Ine.
7Motero ndidzawalumphira ngati mkango,
ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,
ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.
Ndidzawapwepweta ngati mkango;
chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9“Iwe Israeli, wawonongedwa,
chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?
Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,
amene iwe unanena za iwo kuti,
‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,
ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,
machimo ake alembedwa mʼbuku.
13Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,
koma iye ndi mwana wopanda nzeru,
pamene nthawi yake yobadwa yafika
iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;
ndidzawawombola ku imfa.
Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?
Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?
“Sindidzachitanso chifundo,
15ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,
mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,
ikuwomba kuchokera ku chipululu.
Kasupe wake adzaphwa
ndipo chitsime chake chidzawuma.
Chuma chake chonse chamtengowapatali
chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,
chifukwa anawukira Mulungu wawo.
Adzaphedwa ndi lupanga;
ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,
akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
La ira del Señor contra Israel
1Cuando Efraín hablaba, la gente temía;
él tenía la preeminencia sobre Israel.
Pero rindió culto a Baal y por ese pecado murió.
2Sin embargo, siguen pecando,
pues se fabrican, según su ingenio,
imágenes de fundición e ídolos de plata
que no son más que obra de artesanos.
De ellos se dice:
«Ofrecen sacrificios humanos
y besan ídolos en forma de becerros».13:2 De ellos … becerros. Alt. Dicen a la gente: «Quien ofrezca sacrificios, que bese a los becerros».
3Por eso serán como nube matutina,
como rocío que temprano se evapora,
como paja que se lleva el viento,
como humo que se escapa por la chimenea.
4«Pero yo soy el Señor tu Dios
desde que estabas en Egipto.
No conocerás13:4 No conocerás. Alt. No deberías haber conocido. a otro dios fuera de mí
ni hay otro salvador que no sea yo.
5Porque yo cuidé de ti en el desierto,
en esa tierra de terrible aridez.
6Les di de comer y quedaron saciados;
una vez satisfechos, se volvieron arrogantes
y se olvidaron de mí.
7Por eso, yo seré para ellos como un león;
los acecharé junto al camino como un leopardo.
8Los atacaré y desgarraré su pecho
como una osa a quien le quitan sus cachorros.
¡Los devoraré como un león!
¡Los despedazaré como fiera del campo!
9»Voy a destruirte, Israel,
porque estás contra quien te ayuda.
10¿Dónde está tu rey,
para que te salve en todas tus ciudades?
¿Dónde están tus líderes, de los que decías:
“Dame rey y príncipes”?
11En mi ira te di rey
y en mi enojo te lo quité.
12La maldad de Efraín fue anotada;
se ha registrado su pecado.
13Llegan los dolores de parto,
pero él es una criatura necia:
cuando llega la hora del parto,
no se acomoda para salir.
14»Yo los libraré del poder del sepulcro
y los rescataré de la muerte.13:14 de la muerte. Lit. del Seol.
¿Dónde están, oh muerte, tus plagas?
¿Dónde está, oh sepulcro, tu destrucción?
»¡No les tendré compasión!
15Aunque Efraín prospere entre sus hermanos,
vendrá el viento del Señor,
el viento del este que se levanta del desierto
y se agotarán sus fuentes y manantiales.
¡Serán saqueados sus tesoros
y todos sus objetos preciosos!
16El pueblo de Samaria cargará con su culpa
por haberse rebelado contra su Dios.
Caerán a filo de espada;
a los niños los lanzarán contra el suelo
y a las embarazadas les abrirán el vientre».