Hoseya 13 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 13:1-16

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

1Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;

anali wolemekezeka mu Israeli.

Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.

2Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;

akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,

zifanizo zopangidwa mwaluso,

zonsezo zopangidwa ndi amisiri.

Amanena za anthu awa kuti,

“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe

ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”

3Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,

ngati mame amene amakamuka msanga,

ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,

ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.

4Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mu Igupto.

Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,

palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.

5Ndinakusamalira mʼchipululu,

mʼdziko lotentha kwambiri.

6Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;

iwo atakhuta anayamba kunyada;

ndipo anandiyiwala Ine.

7Motero ndidzawalumphira ngati mkango,

ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.

8Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,

ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.

Ndidzawapwepweta ngati mkango;

chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.

9“Iwe Israeli, wawonongedwa,

chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.

10Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?

Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,

amene iwe unanena za iwo kuti,

‘Patseni mfumu ndi akalonga?’

11Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,

ndipo ndinayichotsa mwaukali.

12Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,

machimo ake alembedwa mʼbuku.

13Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,

koma iye ndi mwana wopanda nzeru,

pamene nthawi yake yobadwa yafika

iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.

14“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;

ndidzawawombola ku imfa.

Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?

Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?

“Sindidzachitanso chifundo,

15ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,

mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,

ikuwomba kuchokera ku chipululu.

Kasupe wake adzaphwa

ndipo chitsime chake chidzawuma.

Chuma chake chonse chamtengowapatali

chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.

16Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,

chifukwa anawukira Mulungu wawo.

Adzaphedwa ndi lupanga;

ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,

akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

Nova Versão Internacional

Oseias 13:1-16

A Ira do Senhor contra Israel

1Quando Efraim falava, os homens tremiam;

ele era exaltado em Israel.

Mas tornou-se culpado da adoração a Baal

e começou a morrer.

2Agora eles pecam cada vez mais;

com sua prata fazem ídolos de metal para si,

imagens modeladas com muita inteligência,

todas elas obras de artesãos.

Dizem desse povo:

“Eles oferecem sacrifício humano

e beijam13.2 Ou “Homens que sacrificam beijam os ídolos feitos em forma de bezerro”.

3Por isso serão como a neblina da manhã,

como o orvalho que bem cedo evapora,

como palha que num redemoinho vai-se de uma eira,

como a fumaça que sai pela chaminé.

4“Mas eu sou o Senhor, o seu Deus,

desde a terra do Egito.

Vocês não reconhecerão nenhum outro Deus além de mim,

nenhum outro Salvador.

5Eu cuidei de vocês no deserto,

naquela terra de calor ardente.

6Quando eu os alimentava,

ficavam satisfeitos;

quando ficavam satisfeitos,

eles se orgulhavam,

e então me esqueciam.

7Por isso virei sobre eles como leão,

como leopardo, ficarei à espreita junto ao caminho.

8Como uma ursa de quem roubaram os filhotes,

eu os atacarei e os rasgarei.

Como leão eu os devorarei;

um animal selvagem os despedaçará.

9“Você foi destruído, ó Israel,

porque está contra mim, contra o seu ajudador.

10E agora? Onde está o seu rei

que havia de salvá-lo em todas as suas cidades?

E os oficiais que você pediu, dizendo:

‘Dá-me um rei e líderes’?

11Dei a você um rei na minha ira,

e o tirei na minha indignação.

12A culpa de Efraim foi anotada;

seus pecados são mantidos em registro.

13Chegam-lhe dores como as da mulher em trabalho de parto,

mas é uma criança insensata;

quando chega a hora,

não sai do ventre que a abrigou.

14“Eu os redimirei do poder da sepultura13.14 Hebraico: Sheol. Essa palavra também pode ser traduzida por profundezas, ou morte.;

eu os resgatarei da morte.

Onde estão, ó morte, as suas pragas?

Onde está, ó sepultura, a sua destruição?

“Não terei compaixão alguma,

15embora Efraim floresça entre os seus irmãos.

Um vento oriental virá da parte do Senhor,

soprando desde o deserto;

sua fonte falhará, e seu poço secará.

Todos os seus tesouros serão saqueados dos seus depósitos.

16O povo de Samaria carregará sua culpa,

porque se rebelou contra o seu Deus.

Eles serão mortos à espada;

seus pequeninos serão pisados e despedaçados,

suas mulheres grávidas

terão rasgados os seus ventres.”