Hoseya 13 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 13:1-16

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

1Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;

anali wolemekezeka mu Israeli.

Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.

2Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;

akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,

zifanizo zopangidwa mwaluso,

zonsezo zopangidwa ndi amisiri.

Amanena za anthu awa kuti,

“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe

ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”

3Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,

ngati mame amene amakamuka msanga,

ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,

ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.

4Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mu Igupto.

Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,

palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.

5Ndinakusamalira mʼchipululu,

mʼdziko lotentha kwambiri.

6Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;

iwo atakhuta anayamba kunyada;

ndipo anandiyiwala Ine.

7Motero ndidzawalumphira ngati mkango,

ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.

8Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,

ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.

Ndidzawapwepweta ngati mkango;

chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.

9“Iwe Israeli, wawonongedwa,

chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.

10Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?

Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,

amene iwe unanena za iwo kuti,

‘Patseni mfumu ndi akalonga?’

11Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,

ndipo ndinayichotsa mwaukali.

12Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,

machimo ake alembedwa mʼbuku.

13Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,

koma iye ndi mwana wopanda nzeru,

pamene nthawi yake yobadwa yafika

iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.

14“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;

ndidzawawombola ku imfa.

Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?

Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?

“Sindidzachitanso chifundo,

15ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,

mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,

ikuwomba kuchokera ku chipululu.

Kasupe wake adzaphwa

ndipo chitsime chake chidzawuma.

Chuma chake chonse chamtengowapatali

chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.

16Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,

chifukwa anawukira Mulungu wawo.

Adzaphedwa ndi lupanga;

ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,

akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

King James Version

Hosea 13:1-16

1When Ephraim spake trembling, he exalted himself in Israel; but when he offended in Baal, he died. 2And now they sin more and more, and have made them molten images of their silver, and idols according to their own understanding, all of it the work of the craftsmen: they say of them, Let the men that sacrifice kiss the calves.13.2 they sin…: Heb. they add to sin13.2 the men…: or, the sacrificers of men 3Therefore they shall be as the morning cloud, and as the early dew that passeth away, as the chaff that is driven with the whirlwind out of the floor, and as the smoke out of the chimney. 4Yet I am the LORD thy God from the land of Egypt, and thou shalt know no god but me: for there is no saviour beside me.

5¶ I did know thee in the wilderness, in the land of great drought.13.5 great…: Heb. droughts 6According to their pasture, so were they filled; they were filled, and their heart was exalted; therefore have they forgotten me. 7Therefore I will be unto them as a lion: as a leopard by the way will I observe them: 8I will meet them as a bear that is bereaved of her whelps, and will rend the caul of their heart, and there will I devour them like a lion: the wild beast shall tear them.13.8 wild…: Heb. beast of the field

9¶ O Israel, thou hast destroyed thyself; but in me is thine help.13.9 is…: Heb. in thy help 10I will be thy king: where is any other that may save thee in all thy cities? and thy judges of whom thou saidst, Give me a king and princes?13.10 I will…: rather, Where is thy king? 11I gave thee a king in mine anger, and took him away in my wrath. 12The iniquity of Ephraim is bound up; his sin is hid. 13The sorrows of a travailing woman shall come upon him: he is an unwise son; for he should not stay long in the place of the breaking forth of children.13.13 long: Heb. a time 14I will ransom them from the power of the grave; I will redeem them from death: O death, I will be thy plagues; O grave, I will be thy destruction: repentance shall be hid from mine eyes.13.14 power: Heb. hand

15¶ Though he be fruitful among his brethren, an east wind shall come, the wind of the LORD shall come up from the wilderness, and his spring shall become dry, and his fountain shall be dried up: he shall spoil the treasure of all pleasant vessels.13.15 pleasant…: Heb. vessels of desire 16Samaria shall become desolate; for she hath rebelled against her God: they shall fall by the sword: their infants shall be dashed in pieces, and their women with child shall be ripped up.