Hagai 2 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 2:1-23

Ulemerero wa Nyumba Yatsopano ya Yehova

1Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti: 2“Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti, 3‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu? 4Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 5‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’

6“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda. 7Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 8‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. 9‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

Madalitso kwa Anthu Oyipitsidwa

10Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti: 11“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena: 12Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’ ”

Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”

13Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?”

Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”

14Pamenepo Hagai anati, “ ‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.

15“ ‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova. 16Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha. 17Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova 18‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino. 19Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso.

“ ‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’ ”

Zerubabeli Mphete Yolamulira ya Yehova

20Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti: 21“Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi. 22Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.

23“ ‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

New Serbian Translation

Књига пророка Агеја 2:1-23

Обећање славе новог Дома

1Двадесетог дана седмог месеца, реч Господња је дошла преко пророка Агеја. Поручила је: 2„Кажи управитељу Јуде Зоровавељу, Салатиловом сину, и Првосвештенику Исусу, Јоседековом сину, и свем преосталом народу: 3’Ко је међу вама преосталима видео овај Дом у његовој пређашњој слави? А како вам сада изгледа? Зар сад није као ништа? 4Зато сада, Зоровавељу, буди јак – говори Господ. Буди јак, првосвештениче Исусе, сине Јоседеков! Буди јак, сав народе земље – говори Господ. Градите, јер ја сам са вама – говори Господ над војскама. 5Ово је обећање које сам вам дао када сте изашли из Египта: мој ће Дух бити међу вама. Не плашите се!’

6Јер овако каже Господ над војскама: ’Још једном ћу, и то ускоро, уздрмати небеса и земљу, море и копно! 7Уздрмаћу све народе па ће доћи Чежња2,7 Христос. свих народа. Испунићу овај Дом славом – каже Господ над војскама. 8Моје је сребро, а и злато је моје – говори Господ над војскама. 9Слава овог другог Дома ће бити већа од славе претходног – каже Господ над војскама. Даћу мир месту овом – говори Господ над војскама.’“

Благослов за онечишћени народ

10Двадесет четвртог дана деветог месеца, друге године Даријеве, реч Господња је дошла пророку Агеју и поручила: 11„Овако каже Господ над војскама: ’Питај свештенике за Закон и реци: 12Ево, ако неко носи жртву у скуту својих хаљина, и скутом својим дотакне хлеб, вариво, вино, уље и осталу храну, хоће ли се она посветити?’“

А свештеници су одговорили: „Неће.“

13Агеј је узвратио: „Ако се особа онечишћена мртвим телом дотакне свих тих ствари, хоће ли се оне онечистити?“

А свештеници су одговорили: „Онечистиће се.“

14А Агеј је узвратио: „Такав је овај народ и такви су ови људи преда мном – говори Господ – такав је сав труд њихових руку. Нечисто је све што ми тамо приносе.

15Сада вас молим да срцем размислите од данас па уназад, од када је полаган камен за каменом у Дом Господњи. 16Од тог времена када би неко на гомили очекивао двадесет мера, било би их десет. А када би неко очекивао да из винске каце заграби педесет нацеђених мерица, било би их двадесет. 17Ударао сам вас и сва дела ваших руку медљиком, кукољем и градом. И ниједан од вас ми се није вратио – говори Господ. 18Срцем својим размислите од данас па уназад, од двадесет четвртог дана деветог месеца до дана када је основан Господњи Дом. Размислите срцем својим! 19Наиме, да ли је зрно у амбару? Па ни лоза, смоква, нар и маслина не рађају плодом.

А од овога дана ја ћу да благословим!“

Зоровавељ је Господњи печатни прстен

20Господња реч је дошла и други пут Агеју двадесет четвртог дана тог месеца: 21„Реци Зоровавељу, управитељу Јуде: ’Ја ћу уздрмати небеса и земљу! 22Претурићу престо царствима и уништићу снагу царствима народа. Преврнућу бојна кола и њихове возаче па ће попадати коњи и њихови коњаници, и то сви до једног од мача свог брата.

23Тога ћу дана – говори Господ над војскама – да те узмем, о, Зоровавељу, Салатилов сине, слуго мој! Говори Господ: учинићу те печатним прстеном јер сам те изабрао – говори Господ над војскама.’“