Hagai 1 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 1:1-15

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

1Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

3Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, 4“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

5Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. 6Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. 8Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. 9“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

Swedish Contemporary Bible

Haggaj 1:1-14

Uppdraget att återuppbygga templet

1I kung Dareios andra regeringsår, på första dagen i sjätte månaden1:1 Den 29. aug. 520 f.Kr. Dareios regerade i Persien 522-486 f.Kr., kom Herrens ord genom profeten Haggaj till Serubbabel, Shealtiels son, ståthållare i Juda, och till översteprästen Josua, Josadaks son:

2Så säger härskarornas Herre: ”Detta folk säger att det ännu inte är dags att bygga upp Herrens hus igen.” 3Så kom Herrens ord genom profeten Haggaj: 4”Är det då dags för er själva att bo i panelade hus, när detta hus ligger i ruiner?”

5Så säger nu härskarornas Herre: ”Tänk efter hur ni har det! 6Ni sår mycket men skördar lite. Ni äter men blir inte mätta. Ni dricker men blir inte druckna. Ni klär er men blir inte varma. Den som får någon inkomst stoppar sin lön i en börs med hål.”

7Så säger härskarornas Herre: ”Tänk efter hur ni har det! 8Gå upp i bergen och hämta ner timmer, bygg upp mitt hus! Jag ska se på det med välvilja och visa min härlighet, säger Herren. 9Ni har hoppats på mycket men fått lite. Och när ni fört hem det har jag blåst bort det. Varför? säger härskarornas Herre. Därför att mitt hus ligger i ruiner, medan ni jäktar var och en med sitt eget hus. 10Därför har himlen hållit tillbaka sin dagg och jorden sin skörd. 11Jag har kallat fram en torka över landet och över bergen, över säd, vin och olja, över det som marken producerar, över människor och djur och över era händers arbete.”

12Serubbabel, Shealtiels son, och översteprästen Josua, Josadaks son, och hela den rest av folket som fanns kvar lyssnade då till Herren, sin Gud, och till profeten Haggajs budskap som Herren, deras Gud, hade sänt, och folket fruktade Herren.

13Då förmedlade Haggaj, Herrens sändebud, detta budskap från Herren till folket: ”Jag är med er, säger Herren.” 14Och Herren inspirerade Serubbabel, Shealtiels son och ståthållare i Juda, och översteprästen Josua, Josadaks son, och hela den rest av folket som fanns kvar, så att de kom och började bygga upp härskarornas Herres, sin Guds, tempel.