Habakuku 1 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 1:1-17

1Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.

Dandawulo la Habakuku

2Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani,

koma wosayankha?

Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!”

koma wosatipulumutsa?

3Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa?

Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa?

Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa;

pali ndewu ndi kukangana kwambiri.

4Kotero malamulo anu atha mphamvu,

ndipo chilungamo sichikugwira ntchito.

Anthu oyipa aposa olungama,

kotero apotoza chilungamo.

Yankho la Yehova

5“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani,

ndipo muthedwe nazo nzeru.

Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu

zimene inu simudzazikhulupirira,

ngakhale wina atakufotokozerani.

6Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni,

anthu ankhanza ndiponso amphamvu,

amene amapita pa dziko lonse lapansi

kukalanda malo amene si awo.

7Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa;

amadzipangira okha malamulo

ndi kudzipezera okha ulemu.

8Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku

ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo.

Okwerapo awo akuthamanga molunjika;

a pa akavalo awo ndi ochokera kutali,

akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;

9onse akubwera atakonzekera zachiwawa.

Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu

ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.

10Akunyoza mafumu

ndiponso kuchitira chipongwe olamulira.

Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa;

akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.

11Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe,

anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”

Dandawulo Lachiwiri la Habakuku

12Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire?

Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa.

Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo;

Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.

13Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa;

Inu simulekerera cholakwa.

Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa?

Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa

akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?

14Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,

ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.

15Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza,

amawakola mu ukonde wake,

amawasonkhanitsa mu khoka lake;

kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.

16Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake

ndiponso kufukizira lubani khoka lake,

popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba

ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.

17Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo,

kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

New International Version – UK

Habakkuk 1:1-17

1The prophecy that Habakkuk the prophet received.

Habakkuk’s complaint

2How long, Lord, must I call for help,

but you do not listen?

Or cry out to you, ‘Violence!’

but you do not save?

3Why do you make me look at injustice?

Why do you tolerate wrongdoing?

Destruction and violence are before me;

there is strife, and conflict abounds.

4Therefore the law is paralysed,

and justice never prevails.

The wicked hem in the righteous,

so that justice is perverted.

The Lord’s answer

5‘Look at the nations and watch –

and be utterly amazed.

For I am going to do something in your days

that you would not believe,

even if you were told.

6I am raising up the Babylonians,1:6 Or Chaldeans

that ruthless and impetuous people,

who sweep across the whole earth

to seize dwellings not their own.

7They are a feared and dreaded people;

they are a law to themselves

and promote their own honour.

8Their horses are swifter than leopards,

fiercer than wolves at dusk.

Their cavalry gallops headlong;

their horsemen come from afar.

They fly like an eagle swooping to devour;

9they all come intent on violence.

Their hordes1:9 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain. advance like a desert wind

and gather prisoners like sand.

10They mock kings

and scoff at rulers.

They laugh at all fortified cities;

by building earthen ramps they capture them.

11Then they sweep past like the wind and go on –

guilty people, whose own strength is their god.’

Habakkuk’s second complaint

12Lord, are you not from everlasting?

My God, my Holy One, you1:12 An ancient Hebrew scribal tradition; Masoretic Text we will never die.

You, Lord, have appointed them to execute judgment;

you, my Rock, have ordained them to punish.

13Your eyes are too pure to look on evil;

you cannot tolerate wrongdoing.

Why then do you tolerate the treacherous?

Why are you silent while the wicked

swallow up those more righteous than themselves?

14You have made people like the fish in the sea,

like the sea creatures that have no ruler.

15The wicked foe pulls all of them up with hooks,

he catches them in his net,

he gathers them up in his drag-net;

and so he rejoices and is glad.

16Therefore he sacrifices to his net

and burns incense to his drag-net,

for by his net he lives in luxury

and enjoys the choicest food.

17Is he to keep on emptying his net,

destroying nations without mercy?