Genesis 9 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 9:1-29

Pangano la Mulungu ndi Nowa

1Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi. 2Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire. 3Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.

4“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda. 5Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.

6“Aliyense wopha munthu,

adzaphedwanso ndi munthu;

pakuti Mulungu analenga munthu

mʼchifanizo chake.

7Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”

8Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti, 9“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo, 10pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe. 11Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”

12Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo. 13Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi. 14Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka, 15ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi. 16Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”

17Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”

Ana Aamuna a Nowa

18Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani. 19Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.

20Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa. 21Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche. 22Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja. 23Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.

24Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira, 25anati,

“Atembereredwe Kanaani!

Adzakhala kapolo

wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”

26Anatinso,

“Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu!

Kanaani akhale kapolo wa Semu.

27Mulungu akulitse dziko la Yafeti;

Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu,

ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”

28Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350. 29Anamwalira ali ndi zaka 950.

Japanese Contemporary Bible

創世記 9:1-29

9

神の祝福と契約

1神は、ノアと息子たちを祝福しました。そして、子どもがたくさん生まれ、全地に増え広がるようにと命じたのです。 2-3「野の獣と鳥と魚はみな、あなたたちを恐れるようになるだろう。あなたたちは動物を治めなさい。穀物と野菜のほかに動物も食用として与えよう。 4しかし、いのちの源である血をすっかり抜き取ったあとでなければ、食べてはならない。 5-6人のいのちを奪うことは禁じる。人を殺した動物は生かしておいてはならない。人のいのちを奪う者には、同じくいのちが求められる。人殺しは、神に似せて造られた者を殺すことになるからだ。 7子どもをたくさん産みなさい。どんどん増え広がって、世界を治めなさい。」

8それから神は、ノアと息子たちに約束しました。 9-11「あなたたちとあなたたちの子孫、生き残った鳥、家畜、野生の動物すべてに、わたしはおごそかに誓う。もう二度と洪水で世界を滅ぼしたりはしない。 12その約束のしるしに、 13雲の中に虹をかけよう。この約束は、あなたたちと全世界に対し、この世の終わりまで効力を持つ。 14雲が大地を覆う時、虹が雲の中に輝くだろう。 15その時わたしは、いのちあるものを二度と洪水で滅ぼさないと、堅く約束したことを思い出そう。 16-17雲間にかかる虹が、地上のすべての生き物に対する永遠の約束を思い出させるからだ。」

ノアの息子たち

18ノアの三人の息子はセム、ハム、ヤペテで、このうちハムがカナン人の先祖に当たります。 19この三人から世界のあらゆる国民が出たのです。

20-21さて、ノアは農夫となり、ぶどうを栽培してぶどう酒を作るようになりました。ある日、彼はぶどう酒に酔って前後不覚になり、裸のままテントの中で寝入ってしまいました。 22その醜態を見たハムはあわてて外に飛び出し、二人の兄に、父親が裸で寝ていることを話しました。 23話を聞いたセムとヤペテは父の服を取りに行き、その服を自分たちの肩にかけ、二人並んでうしろ向きのままそろそろとテントに入りました。そして、父親の裸を見ないように注意しながら、服を肩から落として、父の体にかけたのです。 24-25ノアは酔いがさめて起き上がると、とっさに何があったのか悟りました。末の息子ハムがしたことを知った時、彼はこう言いました。

「カナン人〔ハムの子カナンから出た民族〕はのろわれよ。

セムとヤペテの奴隷となって仕えよ。」

26-27また、こう言いました。

「神がセムを祝福なさるように。

カナンは彼の奴隷となれ。

神がヤペテを祝福し、

セムの繁栄にあずかる者としてくださるように。

カナンは彼の奴隷となれ。」

28-29ノアは洪水のあとさらに三百五十年生き、九百五十歳で死にました。