Genesis 6 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 6:1-22

Kuyipa kwa Mtundu wa Anthu

1Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi, 2ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha. 3Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”

4Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.

5Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha, 6Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima. 7Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.” 8Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.

Nowa ndi Chigumula

9Mbiri ya Nowa inali yotere:

Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu. 10Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.

11Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu. 12Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi. 13Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko. 14Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja. 15Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake. 16Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba. 17Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa. 18Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho. 19Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe. 20Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo. 21Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”

22Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.

Persian Contemporary Bible

پيدايش 6:1‏-22

طوفان نوح

1‏-2در اين زمان كه تعداد انسانها روی زمين زياد می‌شد، پسران خدا6‏:1‏و2 منظور از «پسران خدا» ممکن است نسل خداپرست شيث باشد، زيرا لفظ پسران خدا به مردم خداپرست نيز اطلاق می‌شد. در اين صورت می‌توان آيات مزبور را چنين تفسير کرد که پسران نسل شيث با دختران نسل قائن ازدواج کردند و فرزندانی به وجود آوردند که به شرارت روی آوردند. ولی برخی از مفسرين معتقدند که منظور از پسران خدا، فرشتگانی می‌باشند که از فرمان خدا سرپيچی نمودند.‏ مجذوب دختران زيباروی انسانها شدند و هر كدام را كه پسنديدند، برای خود به زنی گرفتند. 3آنگاه خداوند فرمود: «روح من هميشه در انسان باقی نخواهد ماند، زيرا او موجودی است فانی و نفسانی. پس صد و بيست سال به او فرصت می‌دهم تا خود را اصلاح كند.»

4پس از آنكه پسران خدا و دختران انسانها با هم وصلت نمودند، مردانی غول‌آسا از آنان به وجود آمدند. اينان دلاوران معروف دوران قديم هستند. 5‏-6هنگامی كه خداوند ديد مردم غرق در گناهند و دائماً به سوی زشتی‌ها و پليدی‌ها می‌روند، از آفرينش انسان متأسف و محزون شد.

7پس خداوند فرمود: «من انسانی را كه آفريده‌ام از روی زمين محو می‌كنم. حتی حيوانات و خزندگان و پرندگان را نيز از بين می‌برم، زيرا از آفريدن آنها متأسف شدم.»

8اما در اين ميان نوح مورد لطف خداوند قرار گرفت. 9‏-10اين است سرگذشت او:

نوح سه پسر داشت به نامهای سام، حام و يافث. او تنها مرد درستكار و خداترس زمان خودش بود و هميشه می‌كوشيد مطابق خواست خدا زندگی كند.

11در اين زمان، افزونی گناه و ظلم در نظر خدا به منتها درجهٔ خود رسيده و دنيا به کلی فاسد شده بود.

12‏-13وقتی خدا فساد و شرارت بشر را مشاهده كرد، به نوح فرمود: «تصميم گرفته‌ام تمام اين مردم را هلاک كنم، زيرا زمين را از شرارت پُر ساخته‌اند. من آنها را همراه زمين از بين می‌برم.

14«اما تو، ای نوح، با چوب درخت سرو يک كشتی بساز و در آن اتاقهايی درست كن. درزها و شكافهای كشتی را با قير بپوشان. 15آن را طوری بساز كه طولش ۳۰۰ ذراع،6‏:15 فاصله بين سرانگشتان تا آرنج را يک ذراع می‌گفتند. هر ذراع تقريباً نيم متر است.‏ عرضش ۵۰ ذراع و ارتفاع آن ۳۰ ذراع باشد. 16يک ذراع پايينتر از سقف، پنجره‌ای برای روشنايی كشتی بساز. در داخل آن سه طبقه بنا كن و در ورودی كشتی را در پهلوی آن بگذار.

17«بزودی من سراسر زمين را با آب خواهم پوشانيد تا هر موجود زنده‌ای كه در آن هست، هلاک گردد. 18اما با تو عهد می‌بندم كه تو را با همسر و پسران و عروسانت در كشتی سلامت نگاه دارم. 19‏-20از تمام حيوانات، خزندگان و پرندگان يک جفت نر و ماده با خود به داخل كشتی ببر، تا از خطر اين طوفان در امان باشند. 21همچنين خوراک كافی برای خود و برای تمام موجودات در كشتی ذخيره كن.» 22نوح تمام اوامر خدا را انجام داد.