Genesis 4 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 4:1-26

Kaini ndi Abele

1Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.” 2Kenaka anabereka mʼbale wake Abele.

Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi. 3Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe. 4Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake. 5Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.

6Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa? 7Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”

8Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.

9Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?”

Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”

10Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka. 11Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa. 12Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”

13Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga. 14Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”

15Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe. 16Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.

Banja la Kaini

17Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki. 18Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.

19Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila. 20Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto. 21Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro. 22Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.

23Lameki anawuza akazi akewo kuti,

“Ada ndi Zila, ndimvereni;

inu akazi anga imvani mawu anga.

Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka.

Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.

24Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri,

ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”

25Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.” 26Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi.

Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

O Livro

Génesis 4:1-26

Caim e Abel

1Então Adão juntou-se à sua mulher; ela concebeu e teve um filho, a que chamou Caim (alcançar), porque disse: “Com a ajuda do Senhor alcancei um homem!” 2Depois teve outro filho, Abel.

Abel tornou-se pastor de gado, enquanto Caim trabalhava na terra. 3Quando chegou o tempo da colheita, Caim trouxe ao Senhor uma oferta feita de produtos da terra. 4Abel fez o mesmo, mas com os primogénitos e melhores do seu gado. E o Senhor agradou-se de Abel e da sua oferta; 5mas não de Caim nem da sua oferta. Este, em consequência, ficou muito dececionado e irritado. O seu aspeto alterou-se, por causa do ódio que sentia. 6“Porque é que estás furioso?”, perguntou-lhe o Senhor. “Porque estás assim alterado? 7Se fizeres o bem, serás bem aceite e serás feliz. Se agires mal e não obedeceres, toma atenção, porque o pecado está à espera para poder atacar-te, e o seu desejo é destruir-te. No entanto, está na tua mão poder dominá-lo.”

8Um dia, Caim veio ter com o irmão e sugeriu-lhe que fossem andar pelos campos. Quando iam juntos, Caim atacou-o e matou-o.

9O Senhor perguntou-lhe: “Onde é que está o teu irmão?”

“Não sei”, respondeu Caim. “Será que sou o guarda dele?”

10O Senhor insistiu: “Que foi que lhe fizeste? Porque o sangue do teu irmão clama por mim desde a terra em que foi derramado! 11Por isso, agora viverás como um banido nessa terra manchada com o sangue dele. 12Quando a cultivares, não dará mais o fruto resultante do teu esforço. Daqui em diante andarás sempre errante e fugido.”

13Caim replicou: “É um castigo demasiado pesado para suportar. 14Se me expulsas desta terra que tenho cultivado, fazes de mim um fugitivo e um vagabundo. E qualquer que me encontrar há de querer matar-me!”

15“Não”, respondeu-lhe o Senhor. “Não te matarão. Porque quem o fizesse haveria de ser castigado sete vezes mais do que tu.” E pôs em Caim um sinal identificador, para o impedir de ser morto por quem o encontrasse. 16Assim, Caim se afastou da presença do Senhor, indo estabelecer-se na terra de Node, a oriente do Éden.

17Entretanto, a mulher de Caim concebeu e teve uma criança chamada Enoque. Caim construiu então uma cidade e deu-lhe o nome do seu filho.

18Enoque veio a ser pai de Irade, o qual teve por filho Meujael; este gerou Metusael, que foi pai de Lameque.

19Lameque casou com duas mulheres: Ada e Zila. 20Ada teve um filho por nome Jabal que foi pai de todos os criadores de gado e de todos os nómadas que vivem em tendas. 21O seu irmão chamava-se Jubal, o primeiro músico; o inventor da harpa e da flauta. 22Zila, a outra mulher de Lameque, foi mãe de Tubal-Caim, o primeiro a trabalhar com metal fundido, fazendo obras em bronze e em ferro. Este tinha ainda uma irmã: Naamá.

23Um dia, Lameque disse às suas mulheres:

“Ada e Sila, ouçam-me com atenção!

Ó mulheres de Lameque,

prestem atenção ao que vou dizer!

Eu estou pronto a matar um homem,

um jovem, por me atacar ou ferir.

24Na verdade, quem matar Caim

será castigado sete vezes mais do que ele foi

e quem me matar a mim, para se vingar,

será setenta e sete vezes mais castigado.”

25Adão teve de novo relações com sua mulher e ela teve outro filho a quem chamou Sete. E ela disse: “Deus me deu outro filho em lugar de Abel que Caim havia assassinado.” 26Sete teve um filho a quem chamou Enos.

E foi a partir de então, durante a vida deste, que se começou a invocar o nome do Senhor.