Genesis 39 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 39:1-23

Yosefe ndi Mkazi wa Potifara

1Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.

2Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto. 3Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino. 4Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake. 5Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda. 6Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya.

Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola. 7Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”

8Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga. 9Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?” 10Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.

11Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo. 12Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.

13Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba, 14iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri. 15Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”

16Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba. 17Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane. 18Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”

19Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri. 20Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu.

Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo 21koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe. 22Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo. 23Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

Swedish Contemporary Bible

1 Moseboken 39:1-23

Josef kastas i fängelse

1Josef hade nu förts ner till Egypten. Potifar, faraos hovman och befälhavare för livgardet, en egypter, köpte honom av ismaeliterna som hade fört honom dit. 2Herren var med Josef, allt han gjorde lyckades väl. Han var i sin egyptiske husbondes hus, 3och denne förstod att Herren var med Josef och gav honom framgång i allt han företog sig. 4Han såg med välvilja på Josef och gjorde honom till sin närmaste man. Josef fick ansvar för hela hushållet och över allt som Potifar ägde. 5Från den dagen han gav Josef ansvaret för sitt hus och sin egendom, välsignade Herren egypterns hus på grund av Josef. Herren välsignade allt Potifar hade, såväl hemma som ute på markerna. 6Josef fick ansvaret för allt hans husbonde ägde. Det enda Potifar själv behövde bry sig om var vad han skulle äta.

Josef var välbyggd och såg bra ut. 7Efter en tid började Potifars hustru göra närmanden mot honom och föreslog att han skulle ligga med henne.

8Josef vägrade och svarade: ”Min husbonde bekymrar sig inte för någonting i sitt hus utan har lämnat allt han äger i min vård. 9Själv har han inte mer makt här än vad jag har. Han har inte undanhållit mig annat än dig, eftersom du är hans hustru. Hur skulle jag kunna göra något så ont som detta och synda mot Gud?”

10Men hon fortsatte med sina förslag dag efter dag. Josef vägrade dock att lyssna till henne och ville varken ligga med henne eller ens vara nära henne.

11En dag när han gick in i huset för att sköta sina sysslor, var ingen annan inne. 12Då kom hon och grep tag i hans kläder och krävde att han skulle ligga med henne. Men han lämnade sin mantel i hennes hand och flydde ut. 13När hon såg att han lämnade sin mantel och flydde, 14ropade hon på husfolket och sa till dem:

”Se här! Han har tagit hit den där hebreiske slaven som bara vill roa sig med oss. Han kom och ville ligga med mig, men jag skrek högt, 15och när han hörde mitt skrik, lämnade han sin mantel och sprang ut.”

16Hon behöll hans mantel och när hans husbonde kom hem på kvällen, 17berättade hon samma sak också för honom: ”Den där hebreiske slaven, som du har tagit hit, kom och ville roa sig med mig, 18men jag ropade och skrek. Då lämnade han sin mantel och flydde.”

19När husbonden hörde hustruns berättelse om hur hans slav hade uppfört sig mot henne, blev han rasande. 20Husbonden grep Josef och spärrade in honom i det fängelse där kungen hade sina fångar. Så satt alltså Josef nu i fängelse. 21Men Herren var med Josef också där och var god emot honom. Han gjorde fängelsechefen så välvilligt inställd mot Josef 22att han gav Josef ansvaret för alla de andra fångarna liksom ansvaret för allt som gjordes där.

23Fängelsechefen behövde inte bekymra sig över något av det som Josef tog hand om, för Herren var med honom och allt han gjorde lyckades väl.