Genesis 30 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 30:1-43

1Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”

2Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”

3Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”

4Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha, 5ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna. 6Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.

7Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 8Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.

9Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye. 10Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna. 11Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.

12Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 13Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.

14Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”

15Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.”

Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”

16Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.

17Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu. 18Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.

19Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi. 20Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.

21Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.

22Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana. 23Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.” 24Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”

Nkhosa za Yakobo Zichuluka

25Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu. 26Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”

27Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.” 28Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”

29Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira. 30Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”

31Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?”

Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira: 32Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga. 33Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”

34Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.” 35Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta. 36Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.

37Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera. 38Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana. 39Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho. 40Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani. 41Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija. 42Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo. 43Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 30:1-43

1拉结见自己没有给雅各生孩子,就嫉妒姐姐。她对雅各说:“你给我孩子,不然我还不如死了!” 2雅各气愤地说:“使你不能生育的是上帝,难道我能代替上帝吗?” 3拉结说:“你去跟我的婢女辟拉同房吧,这样她可以为我生孩子,我也可以留下后代。” 4于是拉结把婢女辟拉给丈夫做妾,雅各辟拉同房。 5辟拉怀了孕,为雅各生下一个儿子。 6拉结说:“上帝为我申了冤,也听了我的恳求,赐给我一个儿子。”拉结就给孩子取名叫30:6 ”意思是“申冤”。7拉结的婢女辟拉又怀孕,为雅各生了第二个儿子。 8拉结说:“我跟姐姐相争,我得胜了。”她就给这孩子取名叫拿弗他利30:8 拿弗他利”意思是“相争”。

9利亚见自己不再生育,就把婢女悉帕雅各做妾。 10悉帕雅各生了一个儿子。 11利亚说:“真幸运!”她便给孩子取名叫迦得30:11 迦得”意思是“幸运”。12悉帕又给雅各生了第二个儿子, 13利亚说:“我真有福啊!妇女们会说我有福!”她就为孩子取名亚设30:13 亚设”意思是“有福”。

14在收麦子的季节,吕便在田间找到一些风茄,拿回家给母亲利亚拉结知道后,对利亚说:“请给我一些你儿子找到的风茄。” 15利亚说:“你抢了我丈夫还不够吗?现在还要抢我儿子的风茄吗?”拉结回答说:“你给我风茄,今夜雅各就跟你同房。” 16那天晚上,雅各从田间回来,利亚就出来迎接他说:“你要来跟我同房,因为我已经用儿子的风茄把你雇下来了。”于是,那天晚上雅各便跟利亚同房。 17上帝答应利亚的祈求,使她怀孕,为雅各生了第五个儿子。 18利亚说:“我把婢女送给丈夫做妾,现在上帝给我报酬了。”因此,她就为孩子取名叫以萨迦30:18 以萨迦”意思是“报酬”。

19后来,利亚又怀孕,给雅各生下第六个儿子。 20她说:“上帝赐给我珍贵的礼物,现在我丈夫会尊重我,因为我给他生了六个儿子。”于是,她就给这个儿子取名叫西布伦30:20 西布伦”意思是“尊重”。21后来,利亚又生了一个女儿,给她取名叫底娜

22上帝眷顾拉结,听了她的祷告,使她可以生育。 23她就怀孕,生了一个儿子,说:“上帝除去了我的羞辱。” 24她给孩子取名叫约瑟30:24 约瑟”意思是“增添”。,又说:“愿上帝再给我添一个儿子!”

雅各与拉班的协议

25拉结约瑟以后,雅各拉班说:“请让我走吧!我想回故乡, 26请你让我和妻儿一同回去吧!她们都是我替你工作得来的,你知道我怎样努力为你工作。”

27拉班却挽留他,说:“如果你肯赏光,请你留下来!因为我占卜得知上帝为了你的缘故才赐福给我。 28你要多少酬劳,只管说出来,我一定会给你。”

29雅各回答说:“你知道我怎样努力地服侍你,照顾你的牲畜。 30我来以前,你的财产很少。上帝因为我的到来而赐福给你,使你财产大增。但我自己什么时候才能兴家立业呢?”

31拉班问:“我该给你什么呢?”雅各说:“你不用给我什么,只要你答应一件事,我就继续照料你的羊群。 32今天让我从你的羊群中挑出黑色或有斑点的绵羊,以及有斑点的山羊作为我的薪酬。 33以后,如果你在给我作薪酬的羊群中发现白色的绵羊或没有斑点的山羊,就算是我偷的。这样你可以知道我是否诚实。”

34拉班说:“好,就照你的话做!” 35当天,拉班把有条纹或斑点的公山羊以及有斑点或夹杂白纹的母山羊,连同黑色的绵羊都挑出来,交给自己的儿子们看管。 36然后,他离开雅各,彼此相隔三天的路程。雅各继续为他照料其余的羊。

37雅各折下一些杨树、杏树和枫树的嫩枝,削掉部分树皮,露出白色的条纹, 38然后把这些嫩枝插在羊喝水的水槽和水沟里。羊群来喝水时互相交配。 39它们对着这些树枝交配,就生下有条纹和有斑点的羊羔。 40雅各把这些羊羔分出来,使它们与拉班的羊各在一处。他把自己的羊安置在一处,不与拉班的羊搀杂在一起。 41每当肥壮的羊交配时,雅各就把有条纹的枝子插在水沟里,使羊对着树枝交配。 42但如果交配的羊是瘦弱的,他就不插枝子。这样,瘦弱的羊归拉班,肥壮的羊归雅各43因此,雅各变得极其富有,拥有很多羊、骆驼、驴和仆婢。