Genesis 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 3:1-24

Kuchimwa kwa Munthu

1Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’ ”

2Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu, 3koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’ ”

4“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo. 5“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”

6Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso. 7Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.

8Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo. 9Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”

10Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”

11Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”

12Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”

13Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?”

Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”

14Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi,

“Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse

ndi nyama zakuthengo zonse.

Udzayenda chafufumimba

ndipo udzadya fumbi

masiku onse a moyo wako.

15Ndipo ndidzayika chidani

pakati pa iwe ndi mkaziyo,

pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake;

Iye adzaphwanya mutu wako

ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”

16Kwa mkaziyo Iye anati,

“Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati;

ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana.

Udzakhumba mwamuna wako,

ndipo adzakulamulira.”

17Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’

“Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,

movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo

masiku onse a moyo wako.

18Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula

ndipo udzadya zomera zakuthengo.

19Kuti upeze chakudya udzayenera

kukhetsa thukuta,

mpaka utabwerera ku nthaka

pakuti unachokera kumeneko;

pakuti ndiwe fumbi

ku fumbi komweko udzabwerera.”

20Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.

21Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka. 22Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.” 23Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera. 24Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

New Russian Translation

Бытие 3:1-24

Начало греха

1Из всех диких зверей, которых создал Господь Бог, самым хитрым был змей. Он спросил женщину:

– Правда ли Бог сказал: «Не ешьте ни с какого дерева в саду»?

2Женщина ответила змею:

– Мы можем есть плоды с деревьев сада, 3но Бог сказал: «Не ешьте плодов с дерева, которое посередине сада, и не трогайте их, иначе вы умрете».

4– Нет, вы не умрете, – сказал змей женщине. 5– Просто Бог знает, что когда вы съедите их, ваши глаза откроются, и вы станете как Бог3:5 Или: «как боги»., познав добро и зло3:5 Или: «узнав все», также в ст. 3:22..

6Тогда женщина увидела, что плод дерева был хорош в пищу и приятен на вид, и что дерево было желанно, как источник мудрости; и она взяла один из плодов и съела. Она дала плод и мужу, который был с ней, и он ел его. 7Их глаза открылись, и они поняли, что наги; тогда они сшили себе повязки из листьев инжира.

8Подул ветерок3:8 Букв.: «В ветре дня». Это выражение указывает на вечернюю прохладу. Однако слово, стоящее в тексте оригинала, переводится и как ветер, и как дух, и потому оно здесь также говорит о приближении Бога., и они услышали, как Господь Бог ходит3:8 Они услышали, как Господь Бог ходит – или: «Они услышали голос Господа Бога, ходящего, … ». по саду. Адам и его жена спрятались от Господа Бога среди деревьев сада, 9но Господь Бог воззвал к Адаму:

– Где ты?

10Адам ответил:

– Я услышал Тебя3:10 Я услышал Тебя – или: «Я услышал Твой голос». в саду и испугался, потому что я наг, вот я и спрятался.

11Он спросил:

– Кто сказал тебе, что ты наг? Ты ел плоды дерева, с которого Я запретил тебе есть?

12Адам ответил:

– Женщина, которую Ты дал мне, чтобы она была со мной, – это она дала мне плод с того дерева, и я съел его.

13Тогда Господь Бог сказал женщине:

– Что же ты сделала?

Женщина ответила:

– Змей обманул меня, вот я и ела.

14Тогда Господь Бог сказал змею:

– За то, что ты сделал это,

проклят ты больше любого скота

и всех диких зверей!

Ты будешь ползать на брюхе,

ты будешь есть прах

во все дни твоей жизни.

15Я положу вражду

между тобой и женщиной

и между твоим потомком и ее потомком3:15 Еврейский термин «семя» – ключевой термин в Ветхом Завете. Он имеет форму единственного числа, но может указывать как на одного потомка человека, так и на все его потомство в целом. Весьма вероятно, что в большинстве случаев эта двусмысленность применялась намеренно. В данном переводе этот термин либо переводится буквально как «семя», либо как «потомок», «потомки» или «потомство» в зависимости от текстуального и богословского контекста.:

он будет поражать тебя в голову,

а ты будешь жалить его в пяту3:15 Эти слова служат пророчеством об Иисусе Христе (см. Гал. 4:4; 1 Ин. 3:8)..

16А женщине Он сказал:

– Я мучительной сделаю беременность твою:

в страдании ты будешь рожать детей.

Ты будешь желать мужа,

и он будет властвовать над тобою.

17Адаму же Он сказал:

– Так как ты послушался жены и съел плод с дерева,

о котором Я велел тебе: «Не ешь от него»,

проклята из-за тебя земля:

в тяжком труде ты будешь питаться от нее

во все дни твоей жизни.

18Она произрастит тебе колючки и сорняки,

ты будешь питаться полевыми злаками.

19В поте лица своего ты будешь есть свой хлеб,

пока не вернешься в землю,

из которой был взят;

потому что ты – прах,

и в прах ты вернешься.

20Адам назвал свою жену Ева3:20 Возможное значение этого имени (евр.: «Хавва»): «жизнь»., потому что она стала матерью всех живущих.

21Господь Бог сделал одежды из кожи и одел в них Адама и его жену. 22Потом Господь Бог сказал:

– Познав добро и зло, человек стал теперь как один из Нас. Нельзя, чтобы он протянул руку, и, сорвав плод также и с дерева жизни, съел его и стал жить вечно.

23И Господь Бог изгнал его из сада Эдем, чтобы он трудился на земле, из которой был взят. 24Изгнав человека, Он поставил на востоке от сада3:24 Или: «перед садом». Эдем херувимов3:24 Херувим – один из высших ангельских чинов. и вращающийся пламенный меч, чтобы охранять путь к дереву жизни.