Genesis 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 3:1-24

Kuchimwa kwa Munthu

1Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’ ”

2Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu, 3koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’ ”

4“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo. 5“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”

6Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso. 7Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.

8Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo. 9Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”

10Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”

11Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”

12Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”

13Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?”

Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”

14Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi,

“Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse

ndi nyama zakuthengo zonse.

Udzayenda chafufumimba

ndipo udzadya fumbi

masiku onse a moyo wako.

15Ndipo ndidzayika chidani

pakati pa iwe ndi mkaziyo,

pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake;

Iye adzaphwanya mutu wako

ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”

16Kwa mkaziyo Iye anati,

“Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati;

ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana.

Udzakhumba mwamuna wako,

ndipo adzakulamulira.”

17Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’

“Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe,

movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo

masiku onse a moyo wako.

18Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula

ndipo udzadya zomera zakuthengo.

19Kuti upeze chakudya udzayenera

kukhetsa thukuta,

mpaka utabwerera ku nthaka

pakuti unachokera kumeneko;

pakuti ndiwe fumbi

ku fumbi komweko udzabwerera.”

20Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.

21Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka. 22Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.” 23Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera. 24Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 3:1-24

始祖犯罪

1在耶和华上帝所造的田野的各种动物中,蛇最狡猾。蛇对女人说:“上帝真的说过不许你们吃园中所有树上的果子吗?” 2女人回答说:“我们可以吃园中树上的果子, 3只是不可以吃园子中间那棵树的果子。上帝曾经吩咐说,‘你们不可吃那果子,也不可摸,否则你们就会死。’” 4蛇对女人说:“你们一定不会死! 5上帝那样说是因为祂知道你们吃了那树的果子以后,眼睛就会明亮,像上帝一样懂得分辨善恶。” 6女人见那棵树上的果子可口,赏心悦目,可以使人有智慧,就摘下来吃了。她也把果子给跟她在一起的丈夫,他也吃了。 7二人的眼睛果然明亮起来,这才发觉自己原来赤身露体,便把无花果树的叶子编起来遮体。

8傍晚天凉时,夫妇二人听见耶和华上帝在园中行走的声音,就藏在园子的树丛中,想躲开耶和华上帝。 9耶和华上帝呼唤那人说:“你在哪里?” 10那人说:“我听见你在园中行走的声音,就害怕得躲了起来,因为我赤身露体!” 11耶和华上帝问:“谁说你赤身露体?难道你吃了我吩咐你不可吃的果子吗?” 12那人说:“你赐给我作伴的女人摘了那树上的果子给我,我就吃了。” 13耶和华上帝对女人说:“你这做的是什么事?”女人说:“是蛇诱骗我,我才吃的。”

上帝的审判

14耶和华上帝对蛇说:

“你既然做了这事,

你要比一切的牲畜和野兽受更重的咒诅,

你要用肚子爬行,

一生都要吃尘土。

15我要使你和女人结仇,

你的后代和女人的后代也要彼此为仇,

女人的后代必伤你的头,

你必伤他的脚跟。”

16耶和华上帝对女人说:

“我必大大加重你怀孕的痛苦,

你分娩时必受痛苦。

你必恋慕3:16 恋慕”或译“想控制”。自己的丈夫,

你的丈夫必管辖你。”

17耶和华上帝又对亚当说:

“因为你听从妻子的话,

吃了我吩咐你不可吃的果子,

地必因你而受咒诅。

你必终生艰辛劳苦,

才能吃到地里出产的食物。

18地必给你长出荆棘和蒺藜,

你要吃田间长出来的菜蔬。

19你必汗流满面,才有饭吃,

一直到你归回尘土。

因为你是尘土造的,

也必归回尘土。”

20亚当给他的妻子取名叫夏娃,因为她是众生之母。 21耶和华上帝做了皮衣给他们夫妇穿。 22耶和华上帝说:“看啊,那人已经与我们相似,能分辨善恶。现在,恐怕他会伸手去摘生命树的果子吃,那样他就会永远活着。” 23因此,耶和华上帝就把亚当赶出伊甸园,让他去开垦土地——他的本源。 24上帝赶走了亚当以后,就派遣基路伯天使驻守在伊甸园东边,又用一把旋转的火剑守护在通往生命树的路上。