Genesis 20 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 20:1-18

Abrahamu ndi Mfumu Abimeleki

1Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi, 2ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.

3Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”

4Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama? 5Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”

6Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze. 7Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”

8Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri. 9Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.” 10Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”

11Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga. 12Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga. 13Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’ ”

14Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake. 15Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”

16Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”

17Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana. 18Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.

Священное Писание

Начало 20:1-18

Ибрахим и Сарра у Ави-Малика

1Оттуда Ибрахим перебрался в область Негев и поселился между Кадешем и Суром. Он жил пришельцем в Гераре, 2и там сказал о своей жене Сарре: «Она моя сестра». Ави-Малик, царь Герара, послал за Саррой и взял её к себе.

3Но Всевышний явился к Ави-Малику ночью во сне и сказал ему:

– Тебе грозит смерть за женщину, которую ты взял к себе: она замужем.

4Но Ави-Малик не прикасался к ней, и поэтому он сказал:

– Владыка, неужели Ты уничтожишь невинный народ? 5Ведь он мне сказал: «Она моя сестра», и она сказала: «Он мой брат». В этом деле совесть моя чиста и руки невинны.

6Всевышний сказал ему во сне:

– Да, Я знаю, что совесть твоя чиста: это Я удержал тебя от греха против Меня, поэтому и не позволил тебе прикоснуться к ней. 7Теперь верни жену мужу, потому что он – пророк, он помолится за тебя, и ты останешься жив. Но если ты не вернёшь её, знай, что тебе и твоим близким не избежать смерти.

8На другой день рано утром Ави-Малик собрал всех своих приближённых и рассказал им, что случилось; и они сильно испугались. 9Потом Ави-Малик вызвал Ибрахима и сказал:

– Что ты с нами сделал? Какое зло я тебе причинил, что ты навёл такую тяжкую вину на меня и моё царство? Ты поступил со мной так, как нельзя поступать.

10И Ави-Малик спросил Ибрахима:

– Что было у тебя на уме, когда ты сделал такое?

11Ибрахим ответил:

– Я подумал: «В этом месте, конечно, не боятся Всевышнего, и они убьют меня за мою жену». 12Кроме того, она действительно моя сестра – дочь моего отца, хотя и не от моей матери; и она стала моей женой. 13Когда Всевышний отправил меня странствовать из дома моего отца, я сказал ей: «Окажи мне такую услугу: куда бы мы ни пришли, говори обо мне, что я твой брат».

14Тогда Ави-Малик привёл мелкий и крупный скот, рабов и рабынь и дал их Ибрахиму; и вернул ему его жену Сарру.

15Ави-Малик сказал:

– Моя земля перед тобой: живи, где хочешь.

16Сарре он сказал:

– Я даю твоему брату двенадцать килограммов20:16 Букв.: «тысячу шекелей». серебра, чтобы покрыть твою обиду в глазах всего твоего дома; честь твоя восстановлена.

17Ибрахим помолился Всевышнему, и Всевышний исцелил Ави-Малика, и его жену, и рабынь, чтобы они снова могли иметь детей, 18потому что Вечный сделал бесплодными всех женщин в доме Ави-Малика из-за жены Ибрахима Сарры.