Genesis 14 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 14:1-24

Abramu Apulumutsa Loti

1Pa nthawi imeneyi Amarafeli mfumu ya Sinara, Arioki mfumu ya Elasara, Kedorilaomere mfumu ya Elamu ndi Tidala mfumu ya Goimu 2anathira nkhondo Bera mfumu ya ku Sodomu, Birisa mfumu ya Gomora, Sinabi mfumu ya Adima, Semeberi mfumu ya Ziboimu ndi mfumu ya Bela (kumeneko ndi ku Zowari). 3Mafumu onse anathiridwa nkhondowa anagwirizana pamodzi kupita ku Chigwa cha Sidimu (Nyanja ya Mchere). 4Kwa zaka khumi ndi ziwiri anali pansi pa ulamuliro wa Kedorilaomere, koma mʼchaka cha khumi ndi chitatu anamuwukira.

5Mʼchaka cha khumi ndi chinayi, Kedorilaomere mogwirizana ndi mafumu ena aja anapita kukagonjetsa Arefaiwa ku Asiteroti-karanaimu, Zuzimu wa ku Hamu, Aemi wa ku Savekiriataimu 6amene ankakhala ku Ahori, ku dziko la mapiri la Seiri mpaka ku Eli Parani kufupi ndi chipululu. 7Kenaka anabwerera napita ku Eni-Misipati (ku Kadesi), ndipo anagonjetsa dera lonse la Aamaleki, kuphatikizanso Aamori amene ankakhala ku Hazazoni Tamara.

8Tsono mafumu a ku Sodomu, Gomora, Adima, Zeboimu ndi ku Bela (ku Zowari) anapita ku Chigwa cha Sidimu kukakonzekera kuthira nkhondo 9Kedorilaomere mfumu ya Elamu, Tidala mfumu ya Goimu, Amarafeli mfumu ya Sinara ndi Arioki mfumu ya Elasara. Mafumu anayi analimbana ndi mafumu asanu. 10Koma Chigwa cha Sidimu chinali chodzaza ndi maenje aphula. Choncho pamene mafumu a ku Sodomu ndi Gomora amathawa, ankhondo ena anagweramo ndipo ena anathawira ku mapiri. 11Mafumu anayi aja anatenga katundu yense ndi chakudya chonse cha ku Sodomu ndi Gomora napita nazo. 12Anatenganso Loti, mwana wa mʼbale wake wa Abramu pamodzi ndi katundu wake popeza ankakhala mu Sodomu.

13Koma munthu wina amene anathawa, anabwera kudzamufotokozera Abramu Mhebri. Tsono Abramu ankakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya Mamre wa fuko la Aamori, mʼbale wake wa Esikolo ndi Aneri. Onsewa anali pa mgwirizano ndi Abramu. 14Abramu atamva kuti Loti wagwidwa pa nkhondo, anasonkhanitsa asilikali 318 obadwira mʼbanja lake lomwelo nalondola mpaka ku Dani. 15Pa nthawi ya usiku Abramu anawagawa asilikali ake kuti athire nkhondo mafumu aja, ndipo anawakantha nawapirikitsa mpaka ku Hoba, cha kumpoto kwa Damasiko. 16Ndipo anawalanda katundu wawo yense nabwera naye Loti, katundu wake yense, pamodzi ndi akazi ndi anthu ena.

17Abramu atabwerera kuchokera kogonjetsa Kedorilaomere ndi mafumu amene anali nawo pa mgwirizano, mfumu ya ku Sodomu inabwera kudzakumana naye ku Chigwa cha Save (chimenechi ndicho Chigwa cha Mfumu).

18Ndipo Melikizedeki mfumu ya ku Salemu anabweretsa buledi ndi vinyo. Iyeyu anali wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba, 19ndipo anadalitsa Abramu nati,

“Mulungu Wammwambamwamba,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, akudalitse iwe Abramu.

20Ndipo adalitsike Mulungu Wammwambamwamba

amene anapereka adani ako mʼdzanja lako.”

Ndipo Abramu anamupatsa iye chakhumi cha zonse anali nazo.

21Mfumu ya Sodomu inati kwa Abramu, “Ine undipatse anthu okhawo, koma katundu akhale wako.”

22Koma Abramu anawuza mfumu ya Sodomu kuti, “Ndakweza manja anga kwa Yehova, Mulungu Wammwambamwamba, Mlengi wakumwamba ndi dziko lapansi, kulumbira 23kuti sindidzalandira kanthu kalikonse kako, ngakhale utakhala ulusi chabe kapena chingwe cha nsapato, kuopa kuti ungamanene kuti, ‘Ndamulemeretsa Abramu.’ 24Sindidzalandira kanthu kalikonse kupatula zokhazo zimene anthu anga adya ndi gawo la katundu la anthu amene ndinapita nawo monga Aneri, Esikolo ndi Mamre. Iwowa atenge gawo lawo.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Начало 14:1-24

Ибрам освобождает Лута

1В то время Амрафел, царь Вавилонии14:1 Букв.: «Шинара»; также в ст. 9., Ариох, царь Элласара, Кедорлаомер, царь Елама, и Тидал, царь Гоима, 2вместе пошли войной на Беру, царя Содома, Биршу, царя Гоморры, Шинава, царя Адмы, Шемевера, царя Цевоима, и на царя Белы (то есть Цоара). 3Эти цари объединили силы в долине Сиддим (где теперь Мёртвое море14:3 Букв.: «Солёное море».). 4Уже двенадцать лет они были под властью Кедорлаомера, но на тринадцатый год восстали. 5В четырнадцатый год Кедорлаомер и союзные с ним цари вышли и разбили рефаитов в Аштерот-Карнаиме, зузитов в Гаме, емитов в Шав-Кириатаиме 6и хорреев в нагорьях Сеира, по дороге в Ел-Паран, на краю пустыни. 7Оттуда они повернули назад и пришли к Ен-Мишпат (то есть Кадешу), и завоевали всю землю амаликитян, а также аморреев, которые жили в Хацацон-Тамаре.

8Против них выступили царь Содома, царь Гоморры, царь Адмы, царь Цевоима и царь Белы (то есть Цоара). В долине Сиддим они вступили в битву 9против Кедорлаомера, царя Елама, Тидала, царя Гоима, Амрафела, царя Вавилонии, и Ариоха, царя Элласара, – четыре царя против пяти. 10В долине Сиддим было много смоляных ям; когда цари Содома и Гоморры обратились в бегство, многие упали в них, а остальные бежали в горы. 11Четыре царя захватили всё имущество Содома и Гоморры и все их запасы и ушли. 12Они забрали также племянника Ибрама Лута, который жил в Содоме, и всё его имущество.

13Один из тех, кто спасся, пришёл и рассказал об этом еврею Ибраму. Ибрам жил неподалёку от великих деревьев, принадлежавших аморрею Мамре, брату14:13 Брат – здесь это слово может означать «родственник» или «союзник». Эшкола и Анера – все они были союзниками Ибрама. 14Когда Ибрам услышал, что его родственник в плену, он созвал триста восемнадцать способных к бою мужчин, рождённых в его доме, погнался за четырьмя царями, и преследовал их до Дана. 15Ночью Ибрам разделил свой отряд, напал на них и обратил в бегство, преследуя их до Ховы, к северу от Дамаска. 16Он возвратил всё добро и своего родственника Лута со всем имуществом, и женщинами, и людьми.

Ибрам встречает Малик-Цедека

17Когда Ибрам возвращался после победы над Кедорлаомером и союзными с ним царями, царь Содома вышел встречать его в долину Шаве (то есть Царскую долину); 18и Малик-Цедек, царь Салима14:18 Малик-Цедек означает: «царь праведности», а титул «царь Салима» означает: «царь мира (покоя)»., вынес лепёшки и вино. Он был священнослужителем Бога Высочайшего, 19и он благословил Ибрама, сказав:

– Благословен будь Ибрам от Бога Высочайшего, Творца14:19 Или: «Владыки»; так же в ст. 22. неба и земли! 20И славен будь Бог Высочайший, отдавший твоих врагов в руки твои.

Ибрам дал ему от всего десятую часть.

21Царь Содома сказал Ибраму:

– Отдай мне моих людей, а добро оставь себе.

22Но Ибрам сказал царю Содома:

– Я поднял руку мою к Вечному, Богу Высочайшему, Творцу неба и земли, и дал клятву, 23что не приму от тебя даже нитки или ремешка от сандалий, не возьму ничего твоего, чтобы ты не мог сказать: «Я обогатил Ибрама». 24Я возьму только то, что съели мои люди, а кто пошёл со мной – Анер, Эшкол и Мамре – пусть возьмут свою долю.