Genesis 13 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 13:1-18

Abramu Asiyana ndi Loti

1Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo. 2Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.

3Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba, 4ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.

5Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti. 6Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi. 7Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.

8Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale. 9Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”

10Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora). 11Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana. 12Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu. 13Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.

14Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo. 15Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya. 16Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako. 17Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”

18Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.

Thai New Contemporary Bible

ปฐมกาล 13:1-18

อับรามแยกทางกับโลท

1อับรามจึงอพยพจากอียิปต์ขึ้นไปเนเกบพร้อมด้วยภรรยาและทุกสิ่งที่เขามี โลทก็ไปด้วย 2อับรามกลายเป็นคนร่ำรวยมาก มีทั้งฝูงสัตว์และเงินทองมากมาย

3เขาเดินทางรอนแรมจากเนเกบต่อไปถึงเบธเอล จนมาถึงสถานบูชาระหว่างเมืองเบธเอลกับเมืองอัย ซึ่งเขาเคยตั้งเต็นท์ 4และได้สร้างแท่นบูชาเป็นครั้งแรก อับรามนมัสการร้องออกพระนามพระยาห์เวห์ที่นั่น

5ฝ่ายโลทซึ่งมากับอับรามก็มีฝูงแพะแกะ ฝูงวัว และเต็นท์ด้วย 6แต่ที่ดินนั้นไม่เพียงพอให้อับรามกับโลทอยู่ร่วมกัน เพราะต่างก็มีทรัพย์สินมากมาย 7คนเลี้ยงสัตว์ของอับรามกับคนเลี้ยงสัตว์ของโลทก็ทะเลาะกัน เวลานั้นชาวคานาอันและชาวเปริสซียังอาศัยอยู่ในดินแดนนั้นด้วย

8อับรามจึงกล่าวกับโลทว่า “อย่าให้เรากับเจ้าหรือคนของเรากับคนของเจ้าทะเลาะกันเลย เพราะเราเป็นญาติพี่น้องกัน 9ที่ดินทั้งหมดอยู่ตรงหน้าเจ้าไม่ใช่หรือ? เราแยกทางกันเถอะ ถ้าเจ้าไปทางซ้าย เราก็จะไปทางขวา ถ้าเจ้าไปทางขวา เราก็จะไปทางซ้าย”

10โลทเงยหน้าขึ้นมองดูรอบๆ และเห็นว่าที่ราบลุ่มแม่น้ำจอร์แดนทั้งหมดตามทิศที่จะไปยังเมืองโศอาร์นั้นมีน้ำท่าอุดมสมบูรณ์ดี ดั่งสวนขององค์พระผู้เป็นเจ้าดั่งแผ่นดินอียิปต์ (ขณะนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้ายังไม่ได้ทรงทำลายเมืองโสโดมและเมืองโกโมราห์) 11โลทจึงเลือกเอาบริเวณที่ราบลุ่มแม่น้ำจอร์แดนทั้งหมดเป็นของตนและรอนแรมไปทางตะวันออก เขาทั้งสองจึงแยกทางกัน 12อับรามอาศัยอยู่ในดินแดนคานาอัน ส่วนโลทไปอาศัยอยู่ตามเมืองต่างๆ ในที่ราบจอร์แดน และตั้งเต็นท์ของเขาใกล้เมืองโสโดม 13ชาวโสโดมนั้นชั่วร้ายและทำบาปมหันต์ต่อองค์พระผู้เป็นเจ้า

14เมื่อโลทแยกทางไปแล้ว องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับอับรามว่า “จงเงยหน้าขึ้นมองดูรอบๆ มองไปทางทิศเหนือและทิศใต้ ทิศตะวันออกและทิศตะวันตก 15เราจะมอบดินแดนทั้งหมดที่เจ้ามองเห็นให้แก่เจ้าและเชื้อสาย13:15 หรือเมล็ดพันธุ์เช่นเดียวกับข้อ 16ของเจ้าตลอดไป 16เราจะให้เชื้อสายของเจ้ามีจำนวนมากมายนับไม่ถ้วนดุจผงธุลีบนแผ่นดินโลก ถ้าใครสามารถนับผงธุลีได้ก็จะสามารถนับเชื้อสายของเจ้าได้ 17ไปเถิด เดินไปให้ตลอดความกว้างความยาวของดินแดนนี้ เพราะเราจะยกให้เจ้า”

18ดังนั้นอับรามจึงย้ายเต็นท์ไปอยู่ใกล้หมู่ต้นไม้ใหญ่ของมัมเรที่เมืองเฮโบรน และได้สร้างแท่นบูชาแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าที่นั่น