Chimaliziro Chafika
1Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:
“Chimaliziro! Chimaliziro chafika
ku ngodya zinayi za dziko.
3Chimaliziro chili pa iwe tsopano.
Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.
Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.
4Ine sindidzakumvera chisoni
kapena kukuleka.
Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa
komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.
Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
5“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:
“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!
Taona chikubwera!
6Chimaliziro chafika!
Chimaliziro chafika!
Chiwonongeko chakugwera.
Taona chafika!
7Inu anthu okhala mʼdziko,
chiwonongeko chakugwerani.
Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.
8Ine ndili pafupi kukukwiyirani,
ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;
Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako
ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.
9Ine sindidzakumvera chisoni
kapena kukuleka.
Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako
ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.
‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’
10“Taona, tsikulo!
Taona, lafika!
Chiwonongeko chako chabwera.
Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.
Kudzitama kwaphuka.
11Chiwawa chasanduka ndodo
yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.
Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.
Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.
Palibiretu ndipo sipadzapezeka
munthu wowalira maliro.
12Nthawi yafika!
Tsiku layandikira!
Munthu wogula asakondwere
ndipo wogulitsa asamve chisoni,
popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.
13Wogulitsa sadzazipezanso zinthu
zimene anagulitsa kwa wina
chinkana onse awiri akanali ndi moyo,
pakuti chilango chidzagwera onsewo
ndipo sichingasinthike.
Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense
amene adzapulumutsa moyo wake.
14“Lipenga lalira,
ndipo zonse zakonzeka.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,
pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.
15Ku bwalo kuli kumenyana
ndipo mʼkati muli mliri ndi njala.
Anthu okhala ku midzi
adzafa ndi nkhondo.
Iwo okhala ku mizinda
adzafa ndi mliri ndi njala.
16Onse amene adzapulumuka
ndi kumakakhala ku mapiri,
azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.
Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.
17Dzanja lililonse lidzalefuka,
ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.
18Iwo adzavala ziguduli
ndipo adzagwidwa ndi mantha.
Adzakhala ndi nkhope zamanyazi
ndipo mitu yawo adzameta mpala.
19“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu
ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.
Siliva ndi golide wawo
sizidzatha kuwapulumutsa
pa tsiku la ukali wa Yehova.
Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,
kapena kukhala okhuta,
pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.
20Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka
ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.
Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa
kukhala zowanyansa.
21Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.
Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda
ndi kudziyipitsa.
22Ine ndidzawalekerera anthuwo
ndipo adzayipitsa malo anga apamtima.
Adzalowamo ngati mbala
ndi kuyipitsamo.
23“Konzani maunyolo,
chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo
ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.
24Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa
kuti idzalande nyumba zawo.
Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu
pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.
25Nkhawa ikadzawafikira
adzafunafuna mtendere koma osawupeza.
26Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,
ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.
Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.
Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,
ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.
27Mfumu idzalira,
kalonga adzagwidwa ndi mantha.
Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.
Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,
ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.
Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Le jour de la fin arrive
1L’Eternel m’adressa la parole et me dit :
2O toi, fils d’homme, ╵voici ce que déclare ╵le Seigneur, l’Eternel,
au pays d’Israël : ╵La fin est arrivée !
Aux quatre extrémités ╵du pays, c’est la fin !
3Oui, maintenant, ╵c’en est fini de toi,
car je vais déchaîner ╵contre toi ma colère
et je vais te juger ╵pour ta conduite :
je te ferai payer ╵toutes tes abominations.
4Je n’aurai pas pour toi ╵un regard de pitié,
je serai sans merci,
je te rétribuerai ╵pour ta conduite,
et, de tes abominations, ╵tu resteras coupable ;
et vous reconnaîtrez ╵que je suis l’Eternel.
5Voici ce que vous dit ╵le Seigneur, l’Eternel :
Un malheur, oui un malheur sans pareil
va survenir !
6La fin arrive. ╵C’est vrai, elle arrive la fin,
c’en est fini de toi,
la voilà qui arrive.
7La ruine vient pour toi, ╵habitant du pays !
Oui, le moment arrive,
le jour est proche7.7 Voir 13.5 ; 22.21-22 ; Es 2.12 ; Jl 1.15 ; 2.1 ; 4.14 ; Am 5.18 ; Ab 15 ; So 1.7..
Voici : sur les montagnes, ╵c’est la consternation ╵au lieu des cris de joie.
8Maintenant, sans tarder, ╵moi, je vais déverser ╵ma colère sur toi,
et j’irai jusqu’au bout ╵de tout mon courroux contre toi.
Oui, je te jugerai ╵pour ta conduite,
je te ferai payer ╵toutes tes abominations.
9Je n’aurai pas pour toi ╵un regard de pitié,
je serai sans merci,
je te rétribuerai ╵pour ta conduite
et, de tes abominations, ╵tu resteras coupable,
et vous reconnaîtrez ╵que c’est moi, l’Eternel, ╵qui vous aurai frappés.
La ruine se prépare
10Voici le jour ! ╵Elle arrive la ruine !
Oui, elle se prépare,
et le bâton qui va frapper fleurit,
l’arrogance s’épanouit,
11la violence se dresse
pour servir de bâton ╵à la méchanceté.
Il ne restera rien ╵ni de ce peuple,
de ces multitudes bruyantes,
ni de tout son tumulte7.11 tumulte: sens incertain.,
ni de sa gloire.
12Le temps arrive,
le jour approche :
que celui qui achète ╵ne se réjouisse pas,
et que celui qui vend ╵ne se désole pas,
car la colère plane
sur toute cette multitude,
13parce que le vendeur ╵ne retrouvera pas ╵ce qu’il avait vendu,
même s’il demeurait ╵au nombre des vivants.
En effet, la révélation ╵concernant cette multitude ╵ne sera jamais révoquée :
à cause de ses fautes, ╵aucun d’eux ne pourra ╵sauver sa vie.
14On sonnera du cor, ╵et l’on se tiendra prêt,
mais aucun n’ira au combat
car ma colère plane ╵sur toute cette multitude.
Pas d’échappatoire
15Au dehors de la ville, ╵c’est l’épée qui sévit,
au dedans, c’est la peste ╵et la famine.
Celui qui est aux champs
périra par l’épée,
et celui qui est dans la ville,
la peste et la famine ╵le feront succomber.
16Si quelque rescapé ╵parvient à s’échapper,
il s’enfuira vers les montagnes
tout comme les colombes des vallées.
Et ils gémiront tous7.16 L’ancienne version grecque a : et je les ferai mourir.,
chacun pour son péché.
17Leurs mains pendront sans force
et leurs genoux flageoleront.
18Ils porteront ╵des habits de toile de sac
et la frayeur les saisira,
la honte se lira ╵sur chacun des visages,
toutes les têtes ╵seront rasées7.18 Marques de deuil et de tristesse..
19Ils jetteront ╵leur argent dans les rues,
et considéreront ╵leur or comme souillé,
car ni l’argent ni l’or ╵ne pourront les sauver
au jour de la colère ╵de l’Eternel,
ni apaiser leur faim ;
ils ne satisferont ╵aucun de leurs désirs,
car c’est l’argent et l’or ╵qui les ont fait tomber
dans le péché.
20Ils ont mis leur orgueil ╵dans leurs parures magnifiques
et ils s’en sont servis ╵pour fabriquer ╵des idoles abominables ╵et exécrables.
C’est pourquoi tout cela ╵je le rendrai souillé pour eux :
21je le livrerai à des étrangers ╵pour qu’ils le pillent,
comme butin ╵aux méchants de la terre
qui viendront souiller tout cela.
22Je détournerai d’eux ma face
et l’on profanera ╵le lieu que je chéris.
Des brigands y pénétreront ╵et le profaneront.
23Fabriquez-vous des chaînes,
car les crimes font loi ╵dans ce pays,
et la ville est remplie de violence.
24J’amènerai ici ╵les pires des peuples païens
afin qu’ils prennent possession ╵de leurs maisons.
J’abattrai l’orgueil des puissants,
leurs sanctuaires7.24 leurs sanctuaires: selon l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel a : ceux qui les sanctifient. seront profanés.
25Voici : la ruine vient,
ils chercheront la paix ╵sans pouvoir la trouver.
26Désastre sur désastre ╵viendront les submerger,
il y aura un afflux incessant ╵de mauvaises nouvelles.
Ils solliciteront ╵en vain quelque révélation ╵de la part du prophète,
la loi fera défaut au prêtre
et les responsables du peuple ╵seront dépourvus de conseil.
27Le roi prendra le deuil,
et le prince sera vêtu ╵des habits des temps de malheur,
le peuple du pays ╵aura les mains tremblantes.
C’est d’après leur conduite ╵que je les traiterai
et je les jugerai ╵selon leurs propres règles,
et ils reconnaîtront ╵que je suis l’Eternel.