Ezekieli 7 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 7:1-27

Chimaliziro Chafika

1Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuwuza dziko la Israeli kuti:

“Chimaliziro! Chimaliziro chafika

ku ngodya zinayi za dziko.

3Chimaliziro chili pa iwe tsopano.

Mkwiyo wanga ndidzawuthira pa iwe.

Ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako

ndi kukulanga chifukwa cha zonyansa zako.

4Ine sindidzakumvera chisoni

kapena kukuleka.

Ndidzakulanga ndithu chifukwa cha ntchito zako zoyipa

komanso chifukwa cha miyambo yako yonyansa imene ili pakati pako.

Pamenepo udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

5“Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi:

“Chiwonongeko! Chiwonongeko chimene sichinamvekepo!

Taona chikubwera!

6Chimaliziro chafika!

Chimaliziro chafika!

Chiwonongeko chakugwera.

Taona chafika!

7Inu anthu okhala mʼdziko,

chiwonongeko chakugwerani.

Nthawi yafika, tsiku layandikira; tsiku la chisokonezo osati la chimwemwe pa mapiri.

8Ine ndili pafupi kukukwiyirani,

ndipo ukali wanga udzathera pa iwe;

Ine ndidzakuweruza molingana ndi machitidwe ako

ndiponso ndidzakulanga chifukwa cha miyambo yako yonyansa.

9Ine sindidzakumvera chisoni

kapena kukuleka.

Ndidzakulanga malingana ndi ntchito zako

ndiponso chifukwa cha miyambo yako yonyansa pakati pako.

‘Pamenepo udzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndimakantha.’

10“Taona, tsikulo!

Taona, lafika!

Chiwonongeko chako chabwera.

Ndodo yaphuka mphundu za maluwa.

Kudzitama kwaphuka.

11Chiwawa chasanduka ndodo

yowakwapulira chifukwa cha kuyipa kwawo.

Palibe mwa anthu amenewo amene adzatsale.

Palibe ndi mmodzi yemwe mwa unyinji wawo.

Palibiretu ndipo sipadzapezeka

munthu wowalira maliro.

12Nthawi yafika!

Tsiku layandikira!

Munthu wogula asakondwere

ndipo wogulitsa asamve chisoni,

popeza ukali wanga uli pa gulu lonse.

13Wogulitsa sadzazipezanso zinthu

zimene anagulitsa kwa wina

chinkana onse awiri akanali ndi moyo,

pakuti chilango chidzagwera onsewo

ndipo sichingasinthike.

Chifukwa cha machimo awo, palibe aliyense

amene adzapulumutsa moyo wake.

14“Lipenga lalira,

ndipo zonse zakonzeka.

Koma palibe ndi mmodzi yemwe amene akupita ku nkhondo,

pakuti mkwiyo wanga uli pa gulu lonse.

15Ku bwalo kuli kumenyana

ndipo mʼkati muli mliri ndi njala.

Anthu okhala ku midzi

adzafa ndi nkhondo.

Iwo okhala ku mizinda

adzafa ndi mliri ndi njala.

16Onse amene adzapulumuka

ndi kumakakhala ku mapiri,

azidzalira ngati nkhunda za ku zigwa.

Aliyense azidzabuwula chifukwa cha machimo ake.

17Dzanja lililonse lidzalefuka,

ndipo bondo lililonse lidzalobodoka ngati madzi.

18Iwo adzavala ziguduli

ndipo adzagwidwa ndi mantha.

Adzakhala ndi nkhope zamanyazi

ndipo mitu yawo adzameta mpala.

19“Iwo adzataya siliva wawo mʼmisewu

ndipo golide wawo adzakhala chinthu chonyansa.

Siliva ndi golide wawo

sizidzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Chuma chawochi sichidzawathandiza kuthetsa njala,

kapena kukhala okhuta,

pakuti ndicho chinawagwetsa mʼmachimo.

20Iwo ankanyadira zodzikongoletsera zawo zamakaka

ndipo ankazigwiritsa ntchito kupanga mafano awo onyansa ndi zonyansa zawo zina.

Nʼchifukwa chake Ine ndidzazisandutsa

kukhala zowanyansa.

21Ndidzazipereka kwa alendo kuti azifunkhe.

Anthu oyipa a dziko lapansi adzazilanda

ndi kudziyipitsa.

22Ine ndidzawalekerera anthuwo

ndipo adzayipitsa malo anga apamtima.

Adzalowamo ngati mbala

ndi kuyipitsamo.

23“Konzani maunyolo,

chifukwa dziko ladzaza ndi anthu opha anzawo

ndipo mzinda wadzaza ndi chiwawa.

24Ndidzabweretsa mitundu ya anthu oyipitsitsa

kuti idzalande nyumba zawo.

Ndidzathetsa kunyada kwa anthu amphamvu

pamene anthu akunja adzalowa mʼmalo awo achipembedzo ndi kuyipitsamo.

25Nkhawa ikadzawafikira

adzafunafuna mtendere koma osawupeza.

26Tsoka lidzatsatana ndi tsoka linzake,

ndipo mphekesera idzatsatana ndi mphekesera inzake.

Iwo adzayesa kufuna masomphenya kuchokera kwa mneneri.

Adzasowa ansembe owaphunzitsa malamulo,

ndipo anthu akuluakulu sadzakhalanso ndi uphungu.

27Mfumu idzalira,

kalonga adzagwidwa ndi mantha.

Manja a anthu a mʼdzikomo azidzangonjenjemera ndi mantha.

Ine ndidzawalanga molingana ndi machitidwe awo,

ndipo ndidzawaweruza molingana ndi momwe anaweruzira anzawo.

Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 7:1-27

Le jour de la fin arrive

1L’Eternel m’adressa la parole et me dit :

2O toi, fils d’homme, ╵voici ce que déclare ╵le Seigneur, l’Eternel,

au pays d’Israël : ╵La fin est arrivée !

Aux quatre extrémités ╵du pays, c’est la fin !

3Oui, maintenant, ╵c’en est fini de toi,

car je vais déchaîner ╵contre toi ma colère

et je vais te juger ╵pour ta conduite :

je te ferai payer ╵toutes tes abominations.

4Je n’aurai pas pour toi ╵un regard de pitié,

je serai sans merci,

je te rétribuerai ╵pour ta conduite,

et, de tes abominations, ╵tu resteras coupable ;

et vous reconnaîtrez ╵que je suis l’Eternel.

5Voici ce que vous dit ╵le Seigneur, l’Eternel :

Un malheur, oui un malheur sans pareil

va survenir !

6La fin arrive. ╵C’est vrai, elle arrive la fin,

c’en est fini de toi,

la voilà qui arrive.

7La ruine vient pour toi, ╵habitant du pays !

Oui, le moment arrive,

le jour est proche7.7 Voir 13.5 ; 22.21-22 ; Es 2.12 ; Jl 1.15 ; 2.1 ; 4.14 ; Am 5.18 ; Ab 15 ; So 1.7..

Voici : sur les montagnes, ╵c’est la consternation ╵au lieu des cris de joie.

8Maintenant, sans tarder, ╵moi, je vais déverser ╵ma colère sur toi,

et j’irai jusqu’au bout ╵de tout mon courroux contre toi.

Oui, je te jugerai ╵pour ta conduite,

je te ferai payer ╵toutes tes abominations.

9Je n’aurai pas pour toi ╵un regard de pitié,

je serai sans merci,

je te rétribuerai ╵pour ta conduite

et, de tes abominations, ╵tu resteras coupable,

et vous reconnaîtrez ╵que c’est moi, l’Eternel, ╵qui vous aurai frappés.

La ruine se prépare

10Voici le jour ! ╵Elle arrive la ruine !

Oui, elle se prépare,

et le bâton qui va frapper fleurit,

l’arrogance s’épanouit,

11la violence se dresse

pour servir de bâton ╵à la méchanceté.

Il ne restera rien ╵ni de ce peuple,

de ces multitudes bruyantes,

ni de tout son tumulte7.11 tumulte: sens incertain.,

ni de sa gloire.

12Le temps arrive,

le jour approche :

que celui qui achète ╵ne se réjouisse pas,

et que celui qui vend ╵ne se désole pas,

car la colère plane

sur toute cette multitude,

13parce que le vendeur ╵ne retrouvera pas ╵ce qu’il avait vendu,

même s’il demeurait ╵au nombre des vivants.

En effet, la révélation ╵concernant cette multitude ╵ne sera jamais révoquée :

à cause de ses fautes, ╵aucun d’eux ne pourra ╵sauver sa vie.

14On sonnera du cor, ╵et l’on se tiendra prêt,

mais aucun n’ira au combat

car ma colère plane ╵sur toute cette multitude.

Pas d’échappatoire

15Au dehors de la ville, ╵c’est l’épée qui sévit,

au dedans, c’est la peste ╵et la famine.

Celui qui est aux champs

périra par l’épée,

et celui qui est dans la ville,

la peste et la famine ╵le feront succomber.

16Si quelque rescapé ╵parvient à s’échapper,

il s’enfuira vers les montagnes

tout comme les colombes des vallées.

Et ils gémiront tous7.16 L’ancienne version grecque a : et je les ferai mourir.,

chacun pour son péché.

17Leurs mains pendront sans force

et leurs genoux flageoleront.

18Ils porteront ╵des habits de toile de sac

et la frayeur les saisira,

la honte se lira ╵sur chacun des visages,

toutes les têtes ╵seront rasées7.18 Marques de deuil et de tristesse..

19Ils jetteront ╵leur argent dans les rues,

et considéreront ╵leur or comme souillé,

car ni l’argent ni l’or ╵ne pourront les sauver

au jour de la colère ╵de l’Eternel,

ni apaiser leur faim ;

ils ne satisferont ╵aucun de leurs désirs,

car c’est l’argent et l’or ╵qui les ont fait tomber

dans le péché.

20Ils ont mis leur orgueil ╵dans leurs parures magnifiques

et ils s’en sont servis ╵pour fabriquer ╵des idoles abominables ╵et exécrables.

C’est pourquoi tout cela ╵je le rendrai souillé pour eux :

21je le livrerai à des étrangers ╵pour qu’ils le pillent,

comme butin ╵aux méchants de la terre

qui viendront souiller tout cela.

22Je détournerai d’eux ma face

et l’on profanera ╵le lieu que je chéris.

Des brigands y pénétreront ╵et le profaneront.

23Fabriquez-vous des chaînes,

car les crimes font loi ╵dans ce pays,

et la ville est remplie de violence.

24J’amènerai ici ╵les pires des peuples païens

afin qu’ils prennent possession ╵de leurs maisons.

J’abattrai l’orgueil des puissants,

leurs sanctuaires7.24 leurs sanctuaires: selon l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel a : ceux qui les sanctifient. seront profanés.

25Voici : la ruine vient,

ils chercheront la paix ╵sans pouvoir la trouver.

26Désastre sur désastre ╵viendront les submerger,

il y aura un afflux incessant ╵de mauvaises nouvelles.

Ils solliciteront ╵en vain quelque révélation ╵de la part du prophète,

la loi fera défaut au prêtre

et les responsables du peuple ╵seront dépourvus de conseil.

27Le roi prendra le deuil,

et le prince sera vêtu ╵des habits des temps de malheur,

le peuple du pays ╵aura les mains tremblantes.

C’est d’après leur conduite ╵que je les traiterai

et je les jugerai ╵selon leurs propres règles,

et ils reconnaîtront ╵que je suis l’Eternel.