Ezekieli 5 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 5:1-17

Chizindikiro cha Chiweruzo

1Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu. 2Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga. 3Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako. 4Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”

5Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira. 6Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.

7“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.

8“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona. 9Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo. 10Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi. 11Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni. 12Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.

13“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.

14“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo 15Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula. 16Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku. 17Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

Thai New Contemporary Bible

เอเสเคียล 5:1-17

1“บัดนี้บุตรมนุษย์เอ๋ย จงเอาดาบคมกริบมาเล่มหนึ่งและใช้มันเป็นเหมือนมีดโกนของช่างตัดผม จงโกนผมและเคราของเจ้า แล้วเอาตาชั่งมาชั่ง แบ่งผมออกเป็นส่วนๆ 2เมื่อสิ้นสุดวันกำหนดให้ล้อมกรุงแล้ว จงเผาผมหนึ่งในสามส่วนในกรุงนั้น ผมอีกหนึ่งในสามใช้ดาบฟันกระจายรอบเมือง อีกหนึ่งในสามที่เหลือโปรยปลิวไปกับลมเพราะเราจะชักดาบออกมารุกไล่พวกเขา 3แต่จงเอาผมกระจุกหนึ่งมาขมวดไว้ในทบของเสื้อคลุม 4แล้วเอาสองสามเส้นออกมาโยนลงในไฟและเผาให้หมด ไฟกองหนึ่งจะลามจากที่นั่นมายังพงศ์พันธุ์อิสราเอลทั้งหมด

5“พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่า นี่คือเยรูซาเล็มซึ่งเราตั้งไว้ใจกลางชนชาติต่างๆ มีนานาประเทศล้อมรอบ 6แต่โดยความชั่วร้าย เยรูซาเล็มได้กบฏต่อบทบัญญัติและกฎหมายของเรามากยิ่งกว่าชนชาติและประเทศต่างๆ โดยรอบ เยรูซาเล็มได้ละทิ้งบทบัญญัติของเราและไม่ปฏิบัติตามกฎหมายของเรา

7“ดังนั้นพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตจึงตรัสดังนี้ว่า เจ้าดื้อด้านยิ่งกว่าชนชาติต่างๆ โดยรอบ และไม่ได้ปฏิบัติตามกฎหมายของเราหรือรักษาบทบัญญัติของเรา มิหนำซ้ำยังชั่วร้ายยิ่งกว่าชนชาติเพื่อนบ้านเสียอีก5:7 สำเนาต้นฉบับภาษาฮีบรูและฉบับ Syr. ว่าบทบัญญัติของเรา เจ้าได้ประพฤติตามมาตรฐานของชนชาติเพื่อนบ้าน

8“ดังนั้น พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตจึงตรัสดังนี้ว่า เยรูซาเล็มเอ๋ย เราเองจะเป็นศัตรูกับเจ้า และจะลงโทษเจ้าต่อหน้าประชาชาติทั้งหลาย 9เนื่องจากรูปเคารพอันน่าชิงชังทั้งปวงของเจ้า เราจะทำกับเจ้าอย่างที่เราไม่เคยทำมาก่อนและจะไม่ทำอีกเลย 10ดังนั้นในหมู่พวกเจ้า พ่อจะกินลูกของตนเองและลูกจะกินพ่อ เราจะลงโทษเจ้าและจะทำให้ผู้ที่รอดชีวิตอยู่ทั้งหมดกระจัดกระจายไปตามลม 11ดังนั้นพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตจึงประกาศดังนี้ว่า เราดำรงชีวิตอยู่แน่ฉันใด เนื่องจากเจ้าทำให้สถานนมัสการของเราเป็นมลทินด้วยรูปเคารพอันชั่วช้าสามานย์และพิธีกรรมอันน่าชิงชังทั้งสิ้นของเจ้า เราเองจะเลิกโปรดปรานเจ้า เราจะไม่เหลียวแลเจ้าด้วยความสงสารหรือไว้ชีวิตเจ้าฉันนั้น 12หนึ่งในสามของพวกเจ้าจะตายด้วยโรคระบาดหรือการกันดารอาหารในกรุง อีกหนึ่งในสามล้มตายด้วยสงครามนอกกำแพง และเราจะชักดาบออกไล่ล่าอีกหนึ่งในสามของพวกเจ้าให้กระจัดกระจายไปตามลม

13“แล้วความโกรธของเราจะมอดลง โทสะของเราจะสงบลง และเราจะหายแค้น และเมื่อเราได้ระบายโทสะเหนือพวกเขา พวกเขาจะรู้ว่าเราผู้เป็นพระยาห์เวห์ได้ลั่นวาจาไว้ด้วยความกระตือรือร้น

14“เราจะทำให้เจ้าเป็นซากปรักหักพัง และเป็นที่ตำหนิติเตียนในหมู่ประชาชาติรอบตัวเจ้า ต่อหน้าผู้คนที่ผ่านไปมา 15เจ้าจะเป็นที่ตำหนิติเตียนและเป็นที่เปรียบเปรยเย้ยหยัน เป็นคำเตือนและเป็นเป้าของความสยดสยองแก่บรรดาประชาชาติโดยรอบ เมื่อเราลงโทษเจ้าด้วยความโกรธ ด้วยโทสะ และด้วยการกำราบอันเจ็บแสบ เราผู้เป็นพระยาห์เวห์ได้ลั่นวาจาไว้ 16เมื่อเรายิงเจ้าด้วยลูกศรแห่งการกันดารอาหารที่เข่นฆ่าและทำลายล้าง เราจะยิงลูกศรเพื่อทำลายเจ้า เราจะนำการกันดารอาหารที่รุนแรงขึ้นเรื่อยๆ มายังเจ้า และตัดแหล่งเสบียงอาหารของเจ้า 17เราจะส่งการกันดารอาหารและสัตว์ป่ามาเล่นงานเจ้า และคร่าชีวิตลูกๆ ของเจ้า โรคระบาดและการนองเลือดจะแพร่ไปทั่วดินแดนของเจ้า และเราจะนำดาบมาฟาดฟันเจ้า เราผู้เป็นพระยาห์เวห์ได้ลั่นวาจาไว้”