Ezekieli 43 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 43:1-27

Ulemerero Ubwerera Mʼnyumba ya Mulungu

1Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa, 2ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake. 3Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba. 4Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa. 5Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.

6Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu. 7Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo. 8Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya. 9Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.

10“Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo, 11akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.

12“Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.

Guwa la Nsembe

13“Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25. 14Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu. 15Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi. 16Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi. 17Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”

18Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo. 19Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 20Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula. 21Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.

22“Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija. 23Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema. 24Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.

25“Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema. 26Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo. 27Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 43:1-27

耶和華的榮光充滿聖殿

1後來,那人帶我來到東門, 2只見以色列上帝的榮光從東方而來,祂的聲音如澎湃的洪濤,大地也因祂的榮耀而發出光芒。 3這異象如同我從前在祂毀滅耶路撒冷時看見的異象,也像我在迦巴魯河邊看見的異象,我便俯伏在地。 4耶和華的榮光從東門進入聖殿。 5上帝的靈把我舉起,帶我進入內院,耶和華的榮光充滿聖殿。

6那人仍然站在我身旁,我聽見有一位從殿中對我說: 7「人子啊,這裡是我的寶座,是我踏腳的地方,我要與以色列人永遠同住。以色列的君民必不再因不忠貞或在高處為他們死去的君王立碑而玷污我的聖名。 8他們不再在我聖殿旁邊建廟宇,使它們的門檻和門柱緊挨著我的門檻和門柱,以致我與它們只有一牆之隔。他們曾經行可憎的事,玷污我的聖名,所以我發怒消滅他們。 9現在,他們要停止祭拜偶像和他們死去的君王,我就永遠住在他們當中。

10「人子啊,你要向以色列人描述所看見的聖殿,讓他們思考聖殿的設計,使他們為自己的罪惡而羞愧。 11他們若為自己的行為感到羞愧,你就把殿的構造、出入口等整個設計,以及殿中的一切律例和法則告訴他們,並且當著他們的面寫下來,讓他們忠於設計,遵守律例。 12殿所在的山頂周圍都是至聖之地,這是有關殿的法則。

13「以下是祭壇的尺寸,底槽深五十釐米,與四邊的寬度相等,周圍環繞著一條二十二釐米高的邊框, 14從底座到下層臺座高一米,邊寬五十釐米,下層臺座到上一層高二米,邊寬五十釐米。 15最高一層是祭台,高二米,祭台上的四角向上突起。 16祭台是方形的,長寬各六米, 17下面的臺座是方形的,長寬各七米,周圍環繞著一條二十五釐米高的邊框。底座四圍的邊寬五十釐米,上祭台的石階在東面。」

18祂對我說:「人子啊,主耶和華這樣說,『祭壇建成後,要按以下的規矩在上面獻燔祭和灑血。 19你要將一頭公牛犢作為贖罪祭給撒督後裔中做祭司的利未人,他們可以前來事奉我。這是主耶和華說的。 20取些公牛犢的血抹在祭壇的四角、臺座的四角和四邊,使祭壇潔淨,為祭壇贖罪, 21並把贖罪用的公牛犢拿到聖所外指定的地方焚燒。 22第二天,你要獻上一頭毫無殘疾的公山羊作贖罪祭,就像獻公牛一樣,使祭壇潔淨。 23祭壇潔淨後,你要取來一頭毫無殘疾的公牛犢和一隻毫無殘疾的公綿羊, 24祭司要把鹽撒在祭牲上,作為燔祭獻在耶和華面前。 25一連七天,每天都要獻上一隻公山羊、一頭公牛犢和一隻公綿羊作贖罪祭,都不可有殘疾。 26在這七天之內,他們要為祭壇贖罪,使壇潔淨,成為聖壇。 27從第八天開始,祭司要在祭壇上獻你們的燔祭和平安祭,我必悅納你們。這是主耶和華說的。』」