Ezekieli 41 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 41:1-26

1Ndipo munthuyo anapita nane mʼchipinda chopatulika cha Nyumba ya Mulungu ndipo anayeza khonde lake; mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu mbali iliyonse kutalika kwake. 2Mulifupi mwa khomo munali motalika mamita asanu. Makoma a mbali zonse anali a mamita awiri ndi theka mulifupi mwake. Anayezanso kutalika kwa chipinda chopatulika chija ndipo mulitali mwake munali motalika mamita makumi awiri ndi mulifupi mwake munali mamita khumi.

3Kenaka munthuyo anakalowa mʼkati ndipo anayeza khonde la pa khomo; khondelo linali mita imodzi mulifupi mwake. Mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu. 4Ndiponso anayeza kutalika kwa chipinda chopatulika chenichenicho. Mulitali mwake munali mamita khumi, ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi. Munthuyo anandiwuza kuti, “Ichi ndicho chipinda chopatulika kwambiri.”

5Tsono munthuyo anayeza khoma la Nyumba ya Mulungu; kuchindikira kwake kunali mamita atatu. Panalinso zipinda zina kuzungulira Nyumba ya Mulungu ndipo chilichonse chinali cha mamita awiri mulifupi wake. 6Zipindazo zinali zitatu zosanjikizana. Chigawo chilichonse chinali ndi zipinda makumi atatu. Pa makoma a Nyumba ya Mulungu panali zochirikiza zipindazo kuti zisatsamire khoma la Nyumba ya Mulungu. 7Zipinda za mʼmbalizo zinkapita zikulirakulira pomakwera chipinda ndi chipinda potsata kukulirakulira kwa zochirikiza za zipinda zija. Pambali pa Nyumba ya Mulungu panali makwerero okwerera pamwamba, kuchokera chigawo chapansi kudzera chapakati, mpaka kukafika pamwamba.

8Ndinaona chiwundo kuzungulira Nyumba ya Mulungu. Chinapanga maziko a zipindazo ndipo chinali cha mamita atatu. 9Khoma lakunja la zipindazo linali la mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake. Pakati pa chiwundocho 10ndi zipinda za Nyumba ya Mulungu panali bwalo limeneli la mamita khumi kupingasa kwake kuzungulira Nyumba yonse ya Mulungu. 11Zitseko za zipinda zamʼmbalizo zinali zotsekulira ku chiwundo. Chitseko chimodzi chinkayangʼana kumpoto ndipo china chinkayangʼana kummwera. Chiwundo chosamangapo kanthu chinali mamita awiri ndi theka kukula kwake kuzungulira ponseponse.

12Nyumba imene inali chakummwera moyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu inali mamita 35 mulifupi mwake. Khoma la nyumbayo linali mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake kuzungulira ponseponse, ndipo mulitali mwake linali mamita 45.

13Ndipo munthuyo anayeza Nyumba ya Mulungu ndipo mulitali mwake inali mamita makumi asanu. Nyumbayo ndi makoma ake, zonse zinali za mamita makumi asanu. 14Kumaso kwa Nyumba ya Mulungu chakummawa kwa bwalolo mulifupi mwake munali mamita makumi asanu.

15Kenaka anayeza kutalika kwa nyumba yoyangʼanana ndi bwalo chakumadzulo kwa Nyumba ya Mulungu, kuphatikizapo njira zamʼkati ku mbali iliyonse. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, chimene chili chamʼkati, khonde lamʼkati loyangʼanana ndi bwalo, 16mazenera ndi maferemu ake, zonsezi zinali zokutidwa ndi matabwa. Pamwamba moyangʼanana ndi chiwundo, Nyumba ya Mulungu inakutidwa ndi matabwa kuyambira pansi mpaka ku mazenera, (mazenerawo anali okutidwa), 17pamwamba pa khomo lolowera ku malo opatulika amʼkati komanso kuzungulira makoma onse kunja ndi mʼkati, 18anajambulapo zithunzi za kerubi mmodzi atakhala pakati pa kanjedza muwiri. Kerubi aliyense anali ndi nkhope ziwiri: 19imodzi inali nkhope ya munthu yoyangʼana kanjedza mbali imodzi, ndi ina inali nkhope ya mkango yoyangʼana kanjedza mbali ina. Zinajambulidwa kuzungulira Nyumba ya Mulungu yonse. 20Motero kuyambira pansi mpaka pamwamba pa khomo komanso pa makoma onse a chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, anajambula zithunzi za akerubi ndi kanjedza pa makoma onse a malo opatulika.

21Mphuthu za chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu kutalika kwake mbali zonse kunali kofanana. Ndipo kumaso kwa malo opatulika kunali chinthu china chooneka ngati 22guwa lansembe la matabwa. Msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka, mulitali mwake munali mita imodzi, mulifupi mwake munalinso mita imodzi. Mphuthu zake, tsinde lake ndi mbali zonse zinali za matabwa. Munthuyo anandiwuza kuti, “Tebulo limeneli ndilo limakhala pamaso pa Yehova.” 23Chipinda chachikulu chija chinali ndi zitseko ziwiri. Malo opatulika aja analinso ndi zitseko ziwiri. 24Chitseko chilichonse chinali ndi zigawo ziwiri zopatukana. 25Ndipo pa zitsekopo anajambulipo zithunzi za akerubi ndi kanjedza monga zomwe anajambulapo pa makoma. Kunja kwake kunali ngati denga lamatabwa pamwamba pa khonde lamʼkati. 26Pa mbali zonse za khonde lamʼkatilo panali mazenera, ndipo pa makoma ake onse anajambulapo zithunzi za kanjedza.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 41:1-26

1那人帶我進入殿堂,量兩邊的牆柱,各三米寬。 2殿的入口寬五米,兩邊的牆各寬二點五米。殿堂面積長二十米,寬十米。 3他到內殿的入口,量兩邊的牆柱,各一米寬,門寬三米,兩邊的牆各寬三點五米。 4他量了內殿,長寬各十米。他對我說:「這是至聖所。」

5他又量殿牆,厚三米,殿的週邊有廂房,每間寬二米。 6廂房是一層疊一層的,共有三層,每層有三十個房間。殿牆週邊有支撐廂房梁木的牆坎,以免梁木插入殿牆中。 7這些廂房的設計是階梯形的;因此,廂房越往上層越寬,有樓梯自下層經過中層到上層。 8殿的周圍有突出的平臺,高一竿,構成廂房的根基。 9-10廂房外牆厚二點五米,廂房與祭司房之間的空地寬十米。 11有兩個門從空地通往廂房,一南一北。廂房周圍與空地相連的平臺寬二點五米。

12在殿前空地向西的地方有一棟建築物,寬三十五米,長四十五米,牆厚二點五米。

13他量了殿,長五十米。殿的院子,那棟建築物和牆共長五十米。 14殿東邊的空地寬五十米。

15他量了殿後面、空地對面的那棟建築物及其兩邊走廊的長度,共長五十米。

16聖所、至聖所、院子對面的門廊及它們周圍的門檻、格子窗和走廊從地面到窗沿都鑲有木板。 17殿的入口和裡外四周的牆也按尺寸鑲著木板。 18木板上刻著基路伯天使和棕樹,兩者彼此相間排列。基路伯天使有兩個面孔: 19一個是人的臉,面向一邊的棕樹;一個是獅子的臉,面向另一邊的棕樹。 20從地板到門以上殿內牆壁上都刻著基路伯天使和棕樹。

21聖所的門框是方形的,至聖所前的門框也一樣。 22裡面有一座木頭做的祭壇,高一點五米,寬一米,壇的四角、底及四面都是木造的。他對我說:「這是耶和華面前的桌子。」

23聖所和至聖所各有一道雙扇的門, 24每扇都是可以折疊的雙頁門, 25上面也刻有基路伯天使和棕樹,與殿內牆上所刻的一樣。門廊上有木造的廊簷。 26聖殿門廊的牆壁上有格子窗和棕樹雕刻,廂房都有房檐。