Ezekieli 40 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 40:1-49

Malo Atsopano a Nyumba ya Mulungu

1Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu. 2Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda. 3Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera. 4Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”

Chipata Chakummawa

5Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.

6Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu. 7Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.

8Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu. 9Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.

10Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana. 11Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka. 12Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu. 13Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka. 14Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo. 15Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27. 16Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.

Bwalo la Kunja

17Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo. 18Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi. 19Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipata Chakumpoto

20Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja. 21Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13. 22Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde. 23Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Chipata Chakummwera

24Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija. 25Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13. 26Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma. 27Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.

Zipata Zolowera ku Bwalo la Mʼkati

28Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija. 29Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13. 30(Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake). 31Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.

32Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija. 33Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13. 34Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.

35Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija. 36Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13. 37Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.

Zipinda Zokonzeramo Nsembe

38Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza. 39Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula. 40Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero. 41Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza. 42Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina. 43Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.

Zipinda za Ansembe

44Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto. 45Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu, 46ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”

47Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.

Nyumba ya Mulungu

48Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse. 49Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.

New International Version – UK

Ezekiel 40:1-49

The temple area restored

1In the twenty-fifth year of our exile, at the beginning of the year, on the tenth of the month, in the fourteenth year after the fall of the city – on that very day the hand of the Lord was on me and he took me there. 2In visions of God he took me to the land of Israel and set me on a very high mountain, on whose south side were some buildings that looked like a city. 3He took me there, and I saw a man whose appearance was like bronze; he was standing in the gateway with a linen cord and a measuring rod in his hand. 4The man said to me, ‘Son of man, look carefully and listen closely and pay attention to everything I am going to show you, for that is why you have been brought here. Tell the people of Israel everything you see.’

The east gate to the outer court

5I saw a wall completely surrounding the temple area. The length of the measuring rod in the man’s hand was six long cubits,40:5 That is, about 3.2 metres; also in verse 12. The long cubit of about 53 centimetres is the basic unit of measurement of length throughout chapters 40–48. each of which was a cubit and a handbreadth. He measured the wall; it was one measuring rod thick and one rod high.

6Then he went to the east gate. He climbed its steps and measured the threshold of the gate; it was one rod deep. 7The alcoves for the guards were one rod long and one rod wide, and the projecting walls between the alcoves were five cubits40:7 That is, about 2.7 metres; also in verse 48 thick. And the threshold of the gate next to the portico facing the temple was one rod deep.

8Then he measured the portico of the gateway; 9it40:8,9 Many Hebrew manuscripts, Septuagint, Vulgate and Syriac; most Hebrew manuscripts gateway facing the temple; it was one rod deep. 9 Then he measured the portico of the gateway; it was eight cubits40:9 That is, about 4.2 metres deep and its jambs were two cubits40:9 That is, about 1 metre thick. The portico of the gateway faced the temple.

10Inside the east gate were three alcoves on each side; the three had the same measurements, and the faces of the projecting walls on each side had the same measurements. 11Then he measured the width of the entrance of the gateway; it was ten cubits and its length was thirteen cubits.40:11 That is, about 5.3 metres wide and 6.9 metres long 12In front of each alcove was a wall one cubit high, and the alcoves were six cubits square. 13Then he measured the gateway from the top of the rear wall of one alcove to the top of the opposite one; the distance was twenty-five cubits40:13 That is, about 13 metres; also in verses 21, 25, 29, 30, 33 and 36 from one parapet opening to the opposite one. 14He measured along the faces of the projecting walls all around the inside of the gateway – sixty cubits.40:14 That is, about 32 metres The measurement was up to the portico40:14 Septuagint; Hebrew projecting wall facing the courtyard.40:14 The meaning of the Hebrew for this verse is uncertain. 15The distance from the entrance of the gateway to the far end of its portico was fifty cubits.40:15 That is, about 27 metres; also in verses 21, 25, 29, 33 and 36 16The alcoves and the projecting walls inside the gateway were surmounted by narrow parapet openings all round, as was the portico; the openings all round faced inward. The faces of the projecting walls were decorated with palm trees.

The outer court

17Then he brought me into the outer court. There I saw some rooms and a pavement that had been constructed all round the court; there were thirty rooms along the pavement. 18It abutted the sides of the gateways and was as wide as they were long; this was the lower pavement. 19Then he measured the distance from the inside of the lower gateway to the outside of the inner court; it was a hundred cubits40:19 That is, about 53 metres; also in verses 23, 27 and 47 on the east side as well as on the north.

The north gate

20Then he measured the length and width of the north gate, leading into the outer court. 21Its alcoves – three on each side – its projecting walls and its portico had the same measurements as those of the first gateway. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 22Its openings, its portico and its palm tree decorations had the same measurements as those of the gate facing east. Seven steps led up to it, with its portico opposite them. 23There was a gate to the inner court facing the north gate, just as there was on the east. He measured from one gate to the opposite one; it was a hundred cubits.

The south gate

24Then he led me to the south side and I saw the south gate. He measured its jambs and its portico, and they had the same measurements as the others. 25The gateway and its portico had narrow openings all round, like the openings of the others. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 26Seven steps led up to it, with its portico opposite them; it had palm tree decorations on the faces of the projecting walls on each side. 27The inner court also had a gate facing south, and he measured from this gate to the outer gate on the south side; it was a hundred cubits.

The gates to the inner court

28Then he brought me into the inner court through the south gate, and he measured the south gate; it had the same measurements as the others. 29Its alcoves, its projecting walls and its portico had the same measurements as the others. The gateway and its portico had openings all round. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 30(The porticoes of the gateways around the inner court were twenty-five cubits wide and five cubits deep.) 31Its portico faced the outer court; palm trees decorated its jambs, and eight steps led up to it.

32Then he brought me to the inner court on the east side, and he measured the gateway; it had the same measurements as the others. 33Its alcoves, its projecting walls and its portico had the same measurements as the others. The gateway and its portico had openings all round. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 34Its portico faced the outer court; palm trees decorated the jambs on either side, and eight steps led up to it.

35Then he brought me to the north gate and measured it. It had the same measurements as the others, 36as did its alcoves, its projecting walls and its portico, and it had openings all round. It was fifty cubits long and twenty-five cubits wide. 37Its portico40:37 Septuagint (see also verses 31 and 34); Hebrew jambs faced the outer court; palm trees decorated the jambs on either side, and eight steps led up to it.

The rooms for preparing sacrifices

38A room with a doorway was by the portico in each of the inner gateways, where the burnt offerings were washed. 39In the portico of the gateway were two tables on each side, on which the burnt offerings, sin offerings40:39 Or purification offerings and guilt offerings were slaughtered. 40By the outside wall of the portico of the gateway, near the steps at the entrance of the north gateway were two tables, and on the other side of the steps were two tables. 41So there were four tables on one side of the gateway and four on the other – eight tables in all – on which the sacrifices were slaughtered. 42There were also four tables of dressed stone for the burnt offerings, each a cubit and a half long, a cubit and a half wide and a cubit high.40:42 That is, about 80 centimetres long and wide and 53 centimetres high On them were placed the utensils for slaughtering the burnt offerings and the other sacrifices. 43And double-pronged hooks, each a handbreadth40:43 That is, about 9 centimetres long, were attached to the wall all round. The tables were for the flesh of the offerings.

The rooms for the priests

44Outside the inner gate, within the inner court, were two rooms, one40:44 Septuagint; Hebrew were rooms for singers, which were at the side of the north gate and facing south, and another at the side of the south40:44 Septuagint; Hebrew east gate and facing north. 45He said to me, ‘The room facing south is for the priests who guard the temple, 46and the room facing north is for the priests who guard the altar. These are the sons of Zadok, who are the only Levites who may draw near to the Lord to minister before him.’

47Then he measured the court: it was square – a hundred cubits long and a hundred cubits wide. And the altar was in front of the temple.

The new temple

48He brought me to the portico of the temple and measured the jambs of the portico; they were five cubits wide on either side. The width of the entrance was fourteen cubits40:48 That is, about 7.4 metres and its projecting walls were40:48 Septuagint; Hebrew entrance was three cubits40:48 That is, about 1.6 metres wide on either side. 49The portico was twenty cubits40:49 That is, about 11 metres wide, and twelve40:49 Septuagint; Hebrew eleven cubits40:49 That is, about 6.4 metres from front to back. It was reached by a flight of stairs,40:49 Hebrew; Septuagint Ten steps led up to it and there were pillars on each side of the jambs.