Ezekieli 39 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 39:1-29

1“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala. 2Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli. 3Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja. 4Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo. 5Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 6Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’

7“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli. 8Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.

9“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri. 10Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.

11“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.

12“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko. 13Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

14“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo. 15Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi. 16(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.

17“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi. 18Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani. 19Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera. 20Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.

21“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo. 22Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo. 23Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo. 24Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.

25“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera. 26Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine. 27Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera. 28Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo. 29Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 39:1-29

預言歌革被滅

1「人子啊,你要發預言斥責歌革,告訴他,主耶和華這樣說,『米設土巴的首領歌革啊,我要與你為敵。 2我要把你調轉過來,使你從遙遠的北方來到以色列的山中。 3我要打掉你左手的弓,擊落你右手的箭。 4你和你的軍隊以及與你同來的各國聯軍都要倒斃在以色列的山嶺上,我要把你們的屍體給各種猛禽野獸作食物。 5你必倒斃在田野之間,因為我已經宣告。這是主耶和華說的。 6我要火燒安居在瑪各和海島的人,他們就知道我是耶和華。

7「『我要讓我的以色列子民知道我的聖名,不再讓我的聖名被褻瀆。這樣列國就知道我是耶和華——以色列的聖者。 8我所說的日子將要來臨,一切必然實現。這是主耶和華說的。

9「『以色列各城邑的居民都要出去撿兵器當柴燒,其中包括大小的盾牌、弓箭、矛槍等,足夠用七年。 10他們不必到田間拾柴,或到林中伐木,因為有兵器當燃料。他們要搶奪那些搶奪過他們的人,擄掠那些擄掠過他們的人。這是主耶和華說的。

11「『那一天我要把以色列境內、通往鹽海東邊的旅客之谷作為歌革的墳地,埋葬他和他的軍隊。這墳地將截斷行人的去路,因此人稱那地方為哈們·歌革谷。 12以色列人要用七個月來埋葬他們,使那地方潔淨。 13以色列人都來埋葬他們。我彰顯榮耀的那天將是以色列人揚眉吐氣的日子。這是主耶和華說的。 14七個月後,他們會派人不斷巡視那裡,埋葬遺留在地面上的屍體,使那裡潔淨。 15如果巡視的人發現了骸骨,便在旁邊立一個標記,好叫負責埋葬的人將骸骨埋葬在哈們·歌革谷。 16他們要這樣使那地方潔淨。那裡有一座城叫哈摩那39·16 哈摩那」意思是「大群」。。』

17「人子啊,主耶和華說,『你要召喚各類飛鳥和野獸,讓牠們聚集起來,從四面八方來赴我為牠們預備的祭宴,就是以色列山嶺上的大祭宴,在那裡吃肉飲血。 18牠們將吃到勇士的肉,喝到君王的血,好像吃公綿羊、羊羔、公山羊、公牛這些巴珊的肥畜。 19牠們要在我為牠們設的祭宴中任意吃肉飲血,直到吃飽喝醉為止。 20牠們在我的宴席上要飽餐戰馬、車夫、勇士和軍人的肉。這是主耶和華說的。

21「『我要在各國中彰顯我的榮耀,使他們看見我如何用大能審判歌革22從那天起,以色列必知道我是他們的上帝耶和華。 23列國必知道以色列人被擄走是因為他們犯罪背叛我,以致我掩面不顧他們,把他們交在敵人手中,讓他們喪身刀下。 24我照他們的污穢和罪惡報應他們,掩面不顧他們。』

25「因此,主耶和華說,『我要使雅各被擄的人回到故土,我要憐憫全以色列人,熱心維護我的聖名。 26當他們在故土安居,沒有人來威脅他們的時候,他們就會忘記自己所有的羞辱和得罪我的惡事。 27我從列國把他們領回,從敵國把他們召回來的時候,我要藉著他們向列國彰顯我的聖潔。 28我讓他們被擄到各國,將來必召集他們返回故土,不撇下一人。這樣,他們便知道我是他們的上帝耶和華。 29我不再掩面不顧以色列人,因為我要把我的靈澆灌在他們身上。這是主耶和華說的。』」