Ezekieli 34 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 34:1-31

Abusa a Israeli

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa? 3Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo. 4Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza. 5Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo. 6Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.

7“ ‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani. 8Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga. 9Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani. 10Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.

11“ ‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira. 12Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima. 13Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu. 14Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli. 15Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 16Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.

17“ ‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna. 18Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu? 19Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?

20“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda. 21Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali, 22tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso. 23Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo. 24Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.

25“ ‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo. 26Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso. 27Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo. 28Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze. 29Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso. 30Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 31Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’ ”

New International Reader’s Version

Ezekiel 34:1-31

The Lord Will Be the Shepherd of His People

1A message from the Lord came to me. The Lord said, 2“Son of man, prophesy against the shepherds of Israel. Tell them, ‘The Lord and King says, “How terrible it will be for you shepherds of Israel! You only take care of yourselves. You should take good care of your flocks. 3Instead, you eat the butter. You dress yourselves with the wool. You kill the finest animals. But you do not take care of your flocks. 4You have not made the weak ones in the flock stronger. You have not healed the sick. You have not bandaged those who are hurt. You have not brought back those who have wandered away. You have not searched for the lost. When you ruled over them, you were mean to them. You treated them badly. 5So they were scattered because they did not have a shepherd. They became food for all of the wild animals. 6My sheep wandered all over the mountains and high hills. They were scattered over the whole earth. No one searched for them. No one looked for them.”

7“ ‘Shepherds, listen to the Lord’s message. He says, 8“My flock does not have a shepherd. Many of my sheep have been stolen. They have become food for all the wild animals. My shepherds did not care for my sheep. They did not even search for them. Instead, they only took care of themselves. And that is just as sure as I am alive,” announces the Lord and King. 9Shepherds, listen to the Lord’s message. 10The Lord and King says, “I am against the shepherds. I will hold them responsible for my flock. I will stop them from taking care of the flock. Then they will not be able to feed themselves anymore. I will save my flock from their mouths. My sheep will no longer be food for them.” ’ ”

11The Lord and King says, “I myself will search for my sheep. I will look after them. 12A shepherd looks after his scattered flock when he is with them. And I will look after my sheep. I will save them from all the places where they were scattered on a dark and cloudy day. 13I will bring them out from among the nations. I will gather them together from other countries. I will bring them into their own land. There they will eat grass on the mountains and in the valleys. And they will eat in all the fields of Israel. 14I will take care of them in the best grasslands. They will eat grass on the highest mountains of Israel. There they will lie down in the finest grasslands. They will eat grass in the best places on Israel’s mountains. 15I myself will take care of my sheep. I will let them lie down in safety,” announces the Lord and King. 16“I will search for the lost. I will bring back those who have wandered away. I will bandage the ones who are hurt. I will make the weak ones stronger. But I will destroy those who are fat and strong. I will take good care of my sheep. I will treat them fairly.”

17The Lord and King says, “You are my flock. I will judge between one sheep and another. I will judge between rams and goats. 18You already eat in the best grasslands. Must you also stomp all over the other fields? You already drink clear water. Must you also make the rest of the water muddy with your feet? 19Must my flock have to eat the grass you have stomped on? Must they drink the water you have made muddy?”

20So the Lord and King speaks to them. He says, “I myself will judge between the fat sheep and the skinny sheep. 21You push the other sheep around with your hips and shoulders. You use your horns to butt all the weak sheep. Finally, you drive them away. 22But I will save my sheep. They will not be carried off anymore. I will judge between one sheep and another. 23I will place one shepherd over them. He will belong to the family line of my servant David. He will take good care of them. He will look after them. He will be their shepherd. 24I am the Lord. I will be their God. And my servant from David’s family line will be the prince among them. I have spoken. I am the Lord.

25“I will make a covenant with them. It promises to give them peace. I will get rid of the wild animals in the land. Then my sheep can live safely in the desert. They can sleep in the forests. 26I will make them and the places surrounding my holy mountain of Zion a blessing. I will send down rain at the right time. There will be showers of blessing. 27The trees will bear their fruit. And the ground will produce its crops. The people will be secure in their land. I will break the chains that hold them. I will save them from the power of those who made them slaves. Then they will know that I am the Lord. 28The nations will not carry them off anymore. Wild animals will no longer eat them up. They will live in safety. And no one will make them afraid. 29I will give them a land that is famous for its crops. They will never again be hungry there. The nations will not make fun of them anymore. 30Then they will know that I am with them. I am the Lord their God. And the Israelites will know that they are my people,” announces the Lord and King. 31“You are my sheep. You belong to my flock. And I am your God,” announces the Lord and King.