Ezekieli 33 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 33:1-33

Ezekieli Akhala Mlonda

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda. 3Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo. 4Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha. 5Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka. 6Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’

7“Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze. 8Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 9Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.

10“Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’ ” 11Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?

12“Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’ 13Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake. 14Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna, 15monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa. 16Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.

17“Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama. 18Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo. 19Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo. 20Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”

Mbiri ya Kuwonongeka kwa Yerusalemu

21Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!” 22Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.

23Ndipo Yehova anandiyankhula kuti: 24“Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’ 25Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli? 26Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’

27“Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri. 28Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako. 29Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’

30“Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’ 31Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo. 32Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.

33“Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Езекиил 33:1-33

Езекиил – страж Исраила

1Было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, поговори с соплеменниками и скажи им: «Если Я наведу на какую-либо страну меч, а жители той страны изберут у себя человека, поставят его своим стражем, 3и он увидит, что на страну идёт меч, и затрубит в рог, чтобы предупредить народ, 4то тот, кто услышит рог, но не остережётся, и меч, придя, лишит его жизни, – тот сам будет повинен в своей гибели. 5Раз он услышал рог и не остерёгся, он сам виноват в своей гибели. Если бы он остерёгся, то остался бы жив. 6Но если страж увидит, что идёт меч, и не затрубит в рог, чтобы предупредить народ, и меч придёт и лишит жизни кого-то из них, то этот человек будет взят за свой грех, а стража за эту гибель Я призову к ответу».

7Смертный, Я поставил тебя стражем для народа Исраила. Слушай же Моё слово и передавай им Мои предостережения. 8Если Я скажу нечестивому: «Нечестивый, ты непременно умрёшь», а ты не будешь говорить, чтобы отвести его от злого пути, то нечестивый умрёт за свой грех33:8 Или: «во грехе»; также в ст. 9., а за его гибель Я призову к ответу тебя. 9Но если ты предостерегал нечестивого, чтобы он оставил свой путь, а он этого не сделал, то он умрёт за свой грех, а ты спасёшь свою душу.

10Смертный, скажи исраильтянам: «Вы говорите: „Наши преступления и грехи гнетут нас. Мы угасаем из-за них33:10 Или: «в них».. Как нам выжить?“» 11Скажи им: «Верно, как и то, что Я живу, – возвещает Владыка Вечный, – Я хочу не смерти грешника, но того, чтобы он оставил свой путь и жил. Обратитесь! Оставьте свои неправедные пути! Народ Исраила, зачем вам умирать?»

12Итак, смертный, скажи соплеменникам: «Праведность не спасёт праведника, если тот согрешит, и нечестие не погубит нечестивого, если он отвернётся от него. Также если согрешит праведник, то он не сможет остаться в живых ради его былой праведности». 13Если Я скажу праведнику, что он непременно будет жить, а он понадеется на свою праведность и сделает зло, то ни одно из праведных дел, которые он совершил, не вспомнится; он умрёт за то зло, которое сделал. 14А если Я скажу нечестивому: «Ты непременно умрёшь», а он оставит грех и станет поступать справедливо и праведно: 15отдаст обратно то, что взял в залог за долги, вернёт украденное, будет исполнять установления, которые дают жизнь, и не будет делать зла, то он непременно будет жить; он не умрёт. 16Ни один из совершённых им грехов не будет ему припомнен. Он поступает справедливо и праведно: он непременно будет жить.

17А твои соплеменники говорят: «Путь Владыки несправедлив». Нет, это их пути несправедливы. 18Если праведник оставит праведность и примется делать зло, то он умрёт за это. 19А если нечестивый оставит нечестие и станет делать то, что справедливо и праведно, то, поступая так, он будет жить. 20А вы говорите: «Путь Владыки несправедлив». Я буду судить вас, народ Исраила, каждого по его поступкам.

Падение Иерусалима

21На двенадцатый год нашего плена, в пятый день десятого месяца (8 января 585 г. до н. э.), ко мне пришёл человек, который спасся из Иерусалима, и сказал: «Город пал!» 22А вечером, накануне того дня, когда пришёл беженец, рука Вечного была на мне, и Он открыл мои уста, прежде чем беженец утром пришёл ко мне. Он открыл мои уста, и я уже не молчал.

23И было ко мне слово Вечного:

24– Смертный, жители этих развалин, что в земле Исраила, говорят: «Ибрахим был совсем один и владел этой землёй, а нас много. Конечно же, эта земля отдана нам во владение!» 25Поэтому скажи им: Так говорит Владыка Вечный: «Вы едите мясо с кровью, поклоняетесь идолам и проливаете чужую кровь – вам ли владеть этой землёй? 26Вы полагаетесь на меч, делаете мерзости, и один оскверняет жену другого. Вам ли владеть этой землёй?»

27Скажи им вот что: Так говорит Владыка Вечный: «Верно, как и то, что Я живу, – оставшиеся в развалинах падут от меча; тех, кто находится в открытом поле, Я отдам на съедение диким зверям; а те, кто сидит в укреплениях и в пещерах, погибнут от мора. 28Я превращу эту землю в мёртвую пустыню, её гордая мощь исчезнет, и горы Исраила станут такими дикими, что никто не будет по ним проходить. 29Они узнают, что Я – Вечный, когда Я превращу эту землю в мёртвую пустыню за все те мерзости, которые они сделали».

30А о тебе, смертный, твои соплеменники разговаривают у стен и дверей домов, говоря друг другу: «Идём, послушаем весть от Вечного». 31Мой народ ходит к тебе, как обычно, и садится пред тобой слушать твои слова, но не исполняет их. На устах у них – лесть, а сердца тянутся к нечестной поживе. 32Истинно говорю, ты для них что певец, поющий о любви красивым голосом и хорошо играющий: они слышат твои слова, но не исполняют их.

33Когда всё это сбудется, – а сбудется это непременно, – тогда они и узнают, что среди них был пророк.