Ezekieli 31 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 31:1-18

Mkungudza mu Lebanoni

1Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti,

“ ‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?

3Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni,

wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango.

Unali wautali,

msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.

4Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo,

akasupe ozama ankawutalikitsa.

Mitsinje yake inkayenda

mozungulira malo amene unaliwo

ndipo ngalande zake zinkafika

ku mitengo yonse ya mʼmunda.

5Choncho unatalika kwambiri

kupambana mitengo yonse ya mʼmunda.

Nthambi zake zinachuluka

ndi kutalika kwambiri,

chifukwa inkalandira madzi ambiri.

6Mbalame zonse zamlengalenga

zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo.

Nyama zakuthengo zonse

zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake.

Mitundu yotchuka ya anthu

inkakhala mu mthunzi wake.

7Unali wokongola kwambiri,

wa nthambi zake zotambalala,

chifukwa mizu yake inazama pansi

kumene kunali madzi ochuluka.

8Mʼmunda wa Mulungu munalibe

mkungudza wofanana nawo,

kapena mitengo ya payini

ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake.

Munalibenso mtengo wa mkuyu

nthambi zofanafana ndi zake.

Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse

wofanana ndi iwo kukongola kwake.

9Ine ndinawupanga wokongola

wa nthambi zochuluka.

Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa

Mulungu inawuchitira nsanje.

10“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake, 11ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake. 12Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya. 13Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake. 14Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.

15“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. 16Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. 17Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu.

18“ ‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo.

“ ‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Священное Писание

Езекиил 31:1-18

Египет будет повержен, как Ассирия

1В одиннадцатом году, в первый день третьего месяца (21 июня 587 г. до н. э.), было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, скажи фараону, царю Египта, и его полчищам:

«Кто сравнится с тобой величием?

3Посмотри на Ассирию, этот ливанский кедр31:3 Ливанский кедр – эти огромные, долговечные деревья могут достигать 40 м в высоту и 4 м в толщину. Они часто символизировали величие, славу и мощь (см. 17:3-4, 22-24; 4 Цар. 14:7-10; Заб. 91:13; Ис. 2:12-13).

с ветвями красивыми,

с кроной тенистой.

Был он высоким –

в облака уходила его вершина.

4Питала его вода,

подземные источники растили;

текли их потоки

вокруг того места, где он рос,

ручьи посылая

ко всем деревьям лесным.

5И вырос он выше

всех деревьев в лесу;

ветви его разрослись,

и длинными были ветки

от обилия вод в побегах.

6Все птицы небесные

в ветвях его гнездились.

Все дикие звери

под ветвями его плодились.

Все великие народы

жили в его тени.

7Он красовался величием,

длиною ветвей,

так как корни его

спускались к обильным водам.

8Кедры из сада Всевышнего

не могли с ним соперничать;

не равнялись с ним ветвями сосны,

или побегами – чинары:

ни одно из деревьев сада Всевышнего

не могло сравниться с ним красой.

9Я сделал его прекрасным,

с ветками густыми,

на зависть эдемским деревьям,

которые в саду Всевышнего».

10Поэтому так говорит Владыка Вечный:

– Так как он был высоким, вознося вершину к облакам, и возгордился высотой, 11Я отдал его в распоряжение властелина народов, который поступил с ним так, как заслуживало его беззаконие. Я отверг его. 12Чужеземцы, жесточайшие из народов, срубили его и оставили. Его ветви рухнули на горы и долины; его ветки упали сломанными в ущелья земли. Все народы земли вышли из-под его тени и оставили его. 13Все небесные птицы разместились на мёртвом стволе; все дикие звери расселились среди его веток. 14Всё это было для того, чтобы другие деревья у воды впредь не поднимались так высоко и не возносили вершину к облакам; чтобы другие деревья, которые пьют воду, не достигали такой высоты. Всем им суждена смерть, нижний мир, – вместе со смертными, с теми, кто спускается в пропасть.

15Так говорит Владыка Вечный:

– В день, когда он сошёл в мир мёртвых, Я затворил подземные источники ради него, Я обуздал их потоки, и бурные воды укротились. Ради него Я покрыл Ливан мраком, и поникли лесные деревья. 16Я заставил народы дрожать от звука его падения, когда Я поверг его в мир мёртвых с теми, кто спускается в пропасть. И утешились в нижнем мире деревья Эдема, благороднейшие и лучшие с Ливана, деревья, которые обильно поливались. 17Те, кто жил в его тени, его союзники среди народов, сошли в мир мёртвых вместе с ним, соединившись с павшими от меча.

18Какое из эдемских деревьев могло сравниться с тобой славой и величием? Но и тебя вслед за эдемскими деревьями сведут в нижний мир; ты будешь лежать среди необрезанных, рядом с теми, кто пал от меча.

Это о фараоне и его полчищах, – возвещает Владыка Вечный.