Ezekieli 3 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 3:1-27

1Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.” 2Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.

3Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.

4Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga. 5Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli. 6Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera. 7Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma. 8Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo. 9Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”

10Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako. 11Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”

12Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!” 13Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu. 14Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu. 15Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.

Chenjezo kwa Israeli

16Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti, 17“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza. 18Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 19Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.

20“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake. 21Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”

22Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.” 23Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.

24Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako. 25Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu. 26Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu. 27Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

Священное Писание

Езекиил 3:1-27

1Он сказал мне:

– Смертный, съешь же то, что перед тобой, съешь этот свиток, а потом ступай и говори с народом Исраила.

2Я открыл рот, и Он дал мне съесть свиток.

3Он сказал мне:

– Смертный, съешь свиток, который Я даю тебе, и наполни им своё чрево.

Я съел его, и у меня во рту он был сладким, как мёд.

4Он сказал мне:

– Смертный, ступай теперь к исраильтянам и говори им Мои слова. 5Ты отправляешься не к народу с невнятной речью и непонятным языком, а к народу Исраила, 6не к многочисленным народам с их невнятной речью и непонятным языком, чьи слова для тебя темны. Если бы Я послал тебя к ним, они бы, конечно, тебя послушали. 7Но исраильтяне не хотят слушать тебя, потому что они не хотят слушать Меня, ведь весь народ Исраила упрям и непокорен. 8Но Я сделаю тебя таким же неподатливым и твердолобым, как они сами. 9Я сделаю твой лоб подобным самому твёрдому камню, твёрже кремня. Не бойся, не страшись их, хотя они и мятежный народ.

10Он сказал мне:

– Смертный, слушай внимательно и запомни все слова, что Я тебе говорю. 11Ступай теперь к пленным землякам и поговори с ними. Говори им: «Так говорит Владыка Вечный», независимо от того, станут они слушать или откажутся.

12После этого Дух поднял меня, и я услышал позади себя оглушительный, грохочущий голос: «Благословенна слава Вечного в этом месте». 13И был шум от крыльев живых существ, касавшихся друг друга, и стук от колёс возле них, похожий на оглушительный грохот. 14Дух поднял меня и унёс прочь. Я шёл огорчённый, и дух мой негодовал, но рука Вечного крепко лежала на мне. 15Я пришёл к пленникам, которые жили в Тель-Авиве3:15 Не путать с современным Тель-Авивом в Исраиле. у реки Кевар, остановился у них и оставался там семь дней в оцепенении.

Предостережение Исраила

16По истечении семи дней ко мне было слово Вечного:

17– Смертный, Я сделал тебя стражем для народа Исраила. Слушай же слово, которое Я говорю, и предостереги его от Моего имени. 18Если Я скажу нечестивому: «Ты непременно умрёшь», а ты не станешь его предостерегать и отговаривать от злого пути, чтобы спасти его жизнь, то нечестивый умрёт за свой грех3:18 Или: «в своём грехе»; также в ст. 19 и 20., а Я спрошу с тебя за его кровь. 19Но если ты будешь предостерегать нечестивого, а он не оставит ни своего нечестия, ни своего злого пути, то он умрёт за свой грех, а ты спасёшь свою жизнь. 20И если праведник отвернётся от праведности и совершит зло, Я положу перед ним преткновение, и он умрёт. Так как ты не предостерегал его, он умрёт за свой грех. Добрые дела, которые он совершил, не вспомнятся, и Я спрошу с тебя за его кровь. 21Но если ты будешь предостерегать праведника, чтобы он не грешил, и праведник не будет грешить, то он, несомненно, будет жить, потому что внял предостережениям, а ты спасёшь свою жизнь.

22Там рука Вечного была на мне, и Он сказал мне:

– Встань и выйди на равнину; там Я буду говорить с тобой.

23Я встал и вышел на равнину. Слава Вечного стояла там, подобная славе, которую я видел у реки Кевар, и я пал лицом на землю. 24Дух вошёл в меня и поднял на ноги.

Он заговорил со мной и сказал:

– Ступай, запрись у себя дома. 25Что до тебя, смертный, то тебя свяжут верёвками; тебя так скрутят, что ты не сможешь выходить к народу. 26Я сделаю так, что твой язык прилипнет к нёбу, ты будешь молчать и не сможешь обличать их, хотя они и мятежный народ. 27Но когда Я буду говорить тебе, Я буду открывать тебе рот, и ты будешь говорить им: «Так говорит Владыка Вечный». Кто станет слушать, пусть слушает, а кто откажется, пусть отказывается; ведь это мятежный народ.