Ezekieli 28 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 28:1-26

Mawu Odzudzula Mfumu ya Turo

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza

umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu;

ndimakhala pa mpando wa mulungu

pakati pa nyanja.’

Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu,

ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.

3Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.

Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.

4Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako

unadzipezera chuma

ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva

mʼnyumba zosungira chuma chako.

5Ndi nzeru zako zochitira malonda

unachulukitsa chuma chako

ndipo wayamba kunyada

chifukwa cha chuma chakocho.

6“ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Popeza umadziganizira

kuti ndiwe mulungu,

7Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,

kuti adzalimbane nawe.

Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako,

ndipo adzawononga kunyada kwakoko.

8Iwo adzakuponyera ku dzenje

ndipo udzafa imfa yoopsa

mʼnyanja yozama.

9Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’

pamaso pa iwo amene akukupha?

Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu,

mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.

10Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe

mʼmanja mwa anthu achilendo.

Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’ ”

11Yehova anandiyankhula kuti: 12“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni,

wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.

13Iwe unkakhala ngati mu Edeni,

munda wa Mulungu.

Miyala yokongola ya mitundu yonse:

rubi, topazi ndi dayimondi,

kirisoliti, onikisi, yasipa,

safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako.

Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide.

Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.

14Ndinayika kerubi kuti azikulondera.

Unkakhala pa phiri langa lopatulika,

ndipo unkayendayenda

pakati pa miyala ya moto.

15Makhalidwe ako anali abwino

kuyambira pamene unalengedwa

mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.

16Unatanganidwa ndi zamalonda.

Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu

ndi kumachimwa.

Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika.

Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa

kukuchotsa ku miyala yamoto.

17Unkadzikuza mu mtima mwako

chifukwa cha kukongola kwako,

ndipo unayipitsa nzeru zako

chifukwa chofuna kutchuka.

Kotero Ine ndinakugwetsa pansi

kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.

18Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.

Motero unayipitsa malo ako achipembedzo.

Choncho ndinabutsa moto pakati pako,

ndipo unakupsereza,

ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi

pamaso pa anthu onse amene amakuona.

19Anthu onse amitundu amene ankakudziwa

akuchita mantha chifukwa cha iwe.

Watheratu mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’ ”

Za Chilango cha Sidoni

20Yehova anandiyankhula nati: 21“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti, 22‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni,

ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe.

Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova

ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti

ndine woyera pakati pako.

23Ndidzatumiza mliri pa iwe

ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako.

Anthu ophedwa ndi lupanga

adzagwa mbali zonse.

Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

24“ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

25“ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo. 26Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Езекиил 28:1-26

Пророчество о царе Тира

1Было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, скажи правителю Тира: Так говорит Владыка Вечный:

«Объятый гордыней,

ты говоришь: „Я – бог.

Я сижу на божьем престоле

посреди моря“.

Но ты человек, не Бог,

хотя мнишь, что равняешься мудростью с Ним.

3Ты думаешь, что ты мудрее Данияла;

нет для тебя неведомой тайны.

4Мудростью и умом

ты приобрёл богатство.

Ты наполнил золотом и серебром

свои кладовые.

5Великим умением торговать

ты умножил свои богатства,

и из-за них тебя обуяла гордость».

6Поэтому так говорит Владыка Вечный:

«За то, что ты мнишь о себе,

что сравнялся мудростью с Аллахом,

7Я нашлю на тебя чужеземцев,

ужаснейший из народов.

На твои красоту и мудрость они обнажат мечи

и осквернят твой блеск.

8Они сведут тебя в могилу;

ты погибнешь насильственной смертью

над бездной морской.

9Разве станешь ты твердить: „Я – бог!“ –

перед своими убийцами,

когда ты не бог, а человек

в руках своих палачей?

10Ты умрёшь смертью необрезанных

от рук чужеземцев.

Я так сказал», – возвещает Владыка Вечный.

11Было ко мне слово Вечного:

12– Смертный, подними плач о царе Тира и скажи ему: Так говорит Владыка Вечный:

«Ты был примером совершенства,

исполненный мудрости и безупречной красоты.

13Ты был в Эдемском саду,

в саду Аллаха.

Все драгоценные камни тебя украшали:

рубин, топаз, изумруд,

хризолит, оникс и яшма,

сапфир, бирюза и берилл28:13 В некоторых случаях невозможно точно установить, какой камень имеется в виду под тем или иным названием..

Из золота были сделаны для них оправы и гнёзда;

в день твоего сотворения они были приготовлены.

14Ты был помазан быть охраняющим херувимом,

ведь Я освятил тебя.

Ты был на святой горе Аллаха

и ходил среди горящих камней.

15Ты был беспорочен в своих путях

со дня твоего сотворения

до того, как нашлось в тебе преступление.

16От размаха своей торговли

ты исполнился неправды

и согрешил.

Я низверг тебя, как осквернённого, с горы Аллаха,

Я изгнал тебя, о херувим охраняющий,

из среды горящих камней.

17Из-за твоей красоты

тебя обуяла гордость;

ты погубил свою мудрость

ради своей известности.

И поверг Я тебя на землю,

сделав зрелищем для царей28:11-17 В этом отрывке образ царя Тира сливается с образом Шайтана, низверженного с небес (ср. Ис. 14:12-15; Лк. 10:18)..

18Множеством преступлений в бесчестной своей торговле

осквернил ты свои святилища.

И Я вывел из тебя огонь,

который тебя поглотил;

Я превратил тебя в пепел на земле

на глазах у всех, кто смотрел.

19Народы, знавшие тебя,

ужаснулись твоей судьбе.

Тебя постиг страшный конец,

и не будет тебя больше».

Пророчество о Сидоне

20Было ко мне слово Вечного:

21– Смертный, обрати лицо к Сидону; пророчествуй против него 22и скажи: Так говорит Владыка Вечный:

«Я – твой противник, Сидон,

и среди тебя Я прославлюсь.

Люди узнают, что Я – Вечный,

когда Я исполню над тобой приговор

и явлю Свою святость среди тебя.

23Я пошлю на тебя мор,

и на улицы твои – кровопролитие.

Посреди тебя будут падать убитые

от меча, что станет разить со всех сторон.

Тогда они узнают, что Я – Вечный.

24У народа Исраила больше не будет соседей, подобных ранящему терновнику и острым шипам, которые презирают его. Тогда они узнают, что Я – Владыка Вечный».

25Так говорит Владыка Вечный: «Когда Я соберу исраильтян из всех народов, среди которых они были рассеяны, Я явлю среди них Свою святость на глазах у народов. И они будут жить на своей земле, которую Я дал Моему рабу Якубу. 26Они будут жить в безопасности; будут строить дома и разводить виноградники. Они будут жить в безопасности, когда Я исполню приговор над их соседями, которые их презирают. Тогда они узнают, что Я – Вечный, их Бог».