Ezekieli 28 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 28:1-26

Mawu Odzudzula Mfumu ya Turo

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza

umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu;

ndimakhala pa mpando wa mulungu

pakati pa nyanja.’

Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu,

ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.

3Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.

Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.

4Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako

unadzipezera chuma

ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva

mʼnyumba zosungira chuma chako.

5Ndi nzeru zako zochitira malonda

unachulukitsa chuma chako

ndipo wayamba kunyada

chifukwa cha chuma chakocho.

6“ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Popeza umadziganizira

kuti ndiwe mulungu,

7Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,

kuti adzalimbane nawe.

Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako,

ndipo adzawononga kunyada kwakoko.

8Iwo adzakuponyera ku dzenje

ndipo udzafa imfa yoopsa

mʼnyanja yozama.

9Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’

pamaso pa iwo amene akukupha?

Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu,

mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.

10Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe

mʼmanja mwa anthu achilendo.

Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’ ”

11Yehova anandiyankhula kuti: 12“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni,

wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.

13Iwe unkakhala ngati mu Edeni,

munda wa Mulungu.

Miyala yokongola ya mitundu yonse:

rubi, topazi ndi dayimondi,

kirisoliti, onikisi, yasipa,

safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako.

Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide.

Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.

14Ndinayika kerubi kuti azikulondera.

Unkakhala pa phiri langa lopatulika,

ndipo unkayendayenda

pakati pa miyala ya moto.

15Makhalidwe ako anali abwino

kuyambira pamene unalengedwa

mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.

16Unatanganidwa ndi zamalonda.

Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu

ndi kumachimwa.

Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika.

Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa

kukuchotsa ku miyala yamoto.

17Unkadzikuza mu mtima mwako

chifukwa cha kukongola kwako,

ndipo unayipitsa nzeru zako

chifukwa chofuna kutchuka.

Kotero Ine ndinakugwetsa pansi

kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.

18Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.

Motero unayipitsa malo ako achipembedzo.

Choncho ndinabutsa moto pakati pako,

ndipo unakupsereza,

ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi

pamaso pa anthu onse amene amakuona.

19Anthu onse amitundu amene ankakudziwa

akuchita mantha chifukwa cha iwe.

Watheratu mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’ ”

Za Chilango cha Sidoni

20Yehova anandiyankhula nati: 21“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti, 22‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni,

ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe.

Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova

ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti

ndine woyera pakati pako.

23Ndidzatumiza mliri pa iwe

ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako.

Anthu ophedwa ndi lupanga

adzagwa mbali zonse.

Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

24“ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

25“ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo. 26Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”

La Bible du Semeur

Ezéchiel 28:1-26

Contre le prince orgueilleux

1L’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

2Fils d’homme, dis au prince de Tyr28.2 Ce prince de Tyr pourrait être Ittobaal II qui régnait sur Tyr lors de la prise de Jérusalem par les Babyloniens. : « Voici ce que te dit le Seigneur, l’Eternel : Ton cœur s’est élevé et tu as proclamé : “Voici, je suis un dieu, et j’occupe ma place sur un trône divin au cœur des mers.” Pourtant, tu n’es qu’un homme, tu n’es pas un dieu, mais tu te crois aussi sage que Dieu. 3Voici : tu prétends être plus sage que Danel28.3 Voir 14.14, 20 et note. Autre traduction : Daniel., pensant qu’aucun mystère ne t’est impénétrable. 4Par ta sagesse et ton intelligence, tu t’es constitué une immense fortune et tu as amassé de l’or et de l’argent dans tes trésors. 5Par ton extrême habileté dans ton commerce, tu as accumulé des richesses sans nombre et, avec ta fortune, ton cœur s’est élevé. 6A cause de cela, voici ce que te dit le Seigneur, l’Eternel : Parce que tu t’es cru aussi sage que Dieu, 7j’amène contre toi des peuples étrangers parmi les plus violents : ils tireront l’épée contre tous les chefs-d’œuvre de ton habileté et profaneront ta splendeur. 8Ils te feront descendre dans la fosse, et tu mourras de mort violente, au cœur des mers. 9Oseras-tu encore dire : “Je suis Dieu” face à celui qui t’abattra ? Tu n’es qu’un homme, non, tu n’es pas un dieu entre les mains de ceux qui vont te transpercer ! 10Toi, tu mourras comme un incirconcis sous les coups d’étrangers. Moi, j’ai parlé. C’est là ce que déclare le Seigneur, l’Eternel. »

Autrefois et maintenant

11L’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

12Fils d’homme, prononce une complainte contre le roi de Tyr. Dis-lui : « Ainsi te parle le Seigneur, l’Eternel : Par ta grande sagesse et ta beauté parfaite, tu étais un modèle de perfection. 13Tu étais en Eden, dans le jardin de Dieu. Tu étais recouvert de pierres très précieuses28.13 Sur Eden et ses pierres précieuses, voir Gn 2.8-17. de toutes sortes : rubis, topaze et diamant, chrysolithe et onyx, jaspe, saphir, escarboucle, émeraude. Tes tambourins, tes fifres28.13 Tes tambourins, tes fifres: traduction incertaine. étaient d’or ouvragé, ils furent préparés le jour même où tu fus créé. 14Or, je t’avais placé, avec un chérubin28.14 avec un chérubin: en adoptant une autre vocalisation du texte hébreu traditionnel, avec l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel, tel qu’il est vocalisé, signifie : tu étais un chérubin. Sur le chérubin, voir Gn 3.24. qui était oint: sens incertain. D’autres comprennent : aux ailes déployées. protecteur qui était oint, sur la montagne sainte de Dieu ; c’est là que tu étais, te promenant au milieu de ces pierres aux feux étincelants.

15Tu as été irréprochable dans toute ta conduite depuis le jour où tu as été créé, jusqu’à ce que le mal se soit trouvé chez toi. 16Ton commerce prospère t’a entraîné à la violence qui a rempli ton cœur. Alors tu as péché, je t’ai mis au rang des profanes en te chassant de ma montagne. Et le chérubin protecteur t’a expulsé28.16 En modifiant la vocalisation du texte hébreu traditionnel, avec l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel, tel qu’il est vocalisé, signifie : je t’ai expulsé, chérubin protecteur. du milieu de ces pierres aux feux étincelants. 17De ta grande beauté, tu t’es enorgueilli et tu as laissé ta splendeur pervertir ta sagesse. Je t’ai précipité à terre, et te donne en spectacle aux autres rois. 18Par tes nombreux péchés dans ton commerce malhonnête, tu as profané tes sanctuaires et, du milieu de toi, j’ai fait surgir un feu afin qu’il te consume, je t’ai réduit en cendres sur la terre, à la vue de tous. 19Et tous ceux qui te connaissaient parmi les peuples sont frappés de stupeur, car tu es devenu un objet d’épouvante. Et pour toujours, tu ne seras plus ! »

Contre Sidon

20L’Eternel m’adressa la parole en ces termes :

21Fils d’homme, tourne-toi vers Sidon28.21 Autre port phénicien, proche de Tyr., prophétise sur elle. 22Dis-lui : « Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Je vais m’en prendre à toi, Sidon, et, au milieu de toi, je vais faire éclater ma gloire, et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel quand j’exécuterai la sentence contre toi. Ainsi je manifesterai ma sainteté par ma façon de te traiter. 23J’enverrai contre toi la peste, le sang coulera dans tes rues et les morts tomberont, tués au milieu de toi par l’épée venue de toutes parts contre toi, et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel.

Israël délivré

24Il n’y aura donc plus, contre la communauté d’Israël, d’écharde douloureuse ou de ronce blessante : elle n’aura plus de voisins pleins de mépris pour elle, et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel.

25Voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Quand je rassemblerai la communauté d’Israël du milieu des peuples parmi lesquels elle est dispersée, je manifesterai ma sainteté par la façon dont j’agirai envers eux aux yeux des peuples non israélites. Alors, ils habiteront dans leur propre pays, celui que j’ai donné à mon serviteur Jacob. 26Ils y habiteront en sécurité, ils bâtiront des maisons et planteront des vignes ; ils y habiteront en sécurité quand j’aurai exécuté les jugements sur tous leurs voisins qui les méprisent. Et l’on reconnaîtra que je suis l’Eternel, leur Dieu. »