Ezekieli 27 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 27:1-36

Nyimbo Yodandaulira Turo

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo. 3Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti,

“Iwe Turo, umanena kuti,

‘Ndine wokongola kwambiri.’

4Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja;

amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.

5Anakupanga ndi matabwa

a payini ochokera ku Seniri;

anatenga mikungudza ya ku Lebanoni

kupangira mlongoti wako.

6Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani

anapanga zopalasira zako;

ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu.

Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.

7Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako,

ndipo inakhala ngati mbendera.

Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo

zochokera ku zilumba za Elisa.

8Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako.

Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.

9Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako,

ngati okonza zibowo zako.

Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake

ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.

10“Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti

anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo.

Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako,

kubweretsa kwa iwe ulemerero.

11Anthu a ku Arivadi ndi Heleki

ankalondera mbali zonse za mpanda wako;

anthu a ku Gamadi

anali mu nsanja zako,

Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse.

Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.

12“Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.

13“Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.

14“Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.

15“Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.

16“Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.

17“Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.

18“Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari. 19Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.

20“Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.

21“Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.

22“Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.

23“Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda. 24Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.

25“Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali

zonyamula malonda ako.

Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi

yodzaza ndi katundu wolemera.

26Anthu opalasa ako amakupititsa

pa nyanja yozama.

Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola

pakati pa nyanja.

27Chuma chako, katundu wako, malonda ako,

okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi,

anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse

ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo

adzamira mʼnyanja

tsiku limene udzawonongeka.

28Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka

chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.

29Onse amene amapalasa sitima zapamadzi,

adzatuluka mʼsitima zawo;

oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi

adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.

30Iwo akufuwula,

kukulira iwe kwambiri;

akudzithira fumbi kumutu,

ndi kudzigubuduza pa phulusa.

31Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe

ndipo akuvala ziguduli.

Akukulira iweyo

ndi mitima yowawa kwambiri.

32Akuyimba nyimbo

yokudandaulira nʼkumati:

‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo

pakati pa nyanja?’

33Pamene malonda ako ankawoloka nyanja

unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu.

Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako

komanso ndi malonda ako.

34Koma tsopano wathyokera mʼnyanja,

pansi penipeni pa nyanja.

Katundu wako ndi onse amene anali nawe

amira pamodzi nawe.

35Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja

aopsedwa ndi zimene zakuchitikira.

Mafumu awo akuchita mantha

ndipo nkhope zangoti khululu.

36Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola.

Watha mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”

Hoffnung für Alle

Hesekiel 27:1-36

Ein Klagelied über den Untergang von Tyrus

1Wieder empfing ich eine Botschaft vom Herrn. Er sprach zu mir: 2»Du Mensch, stimm ein Klagelied über Tyrus an! 3Sag zu der Stadt, die den Zugang zum Meer beherrscht und mit vielen Küstenvölkern Handel treibt:

So spricht Gott, der Herr: Tyrus, du behauptest, von vollendeter Schönheit zu sein. 4Das Meer ist dein Zuhause, und deine Erbauer haben dich wunderschön wie ein Schiff gestaltet: 5Deine Planken bauten sie mit Zypressenholz vom Senir27,5 Anderer Name für den Berg Hermon. Vgl. 5. Mose 3,9., den Mast fertigten sie aus Zedern vom Libanon an. 6Für deine Ruder nahmen sie Eichen aus Baschan, das Deck bauten sie mit Wacholderholz aus Zypern und verkleideten es mit Elfenbein. 7Aus Ägypten kam das feine Leinen für die Segel, die bunten Farben leuchteten weithin. Für das Sonnensegel wurde violetter und roter Purpur aus Elischa verwendet.

8Die Bewohner von Sidon und Arwad waren deine Ruderer, und fähige Männer aus deiner Mitte arbeiteten als Matrosen. 9Wenn man ein Leck fand, besserten es erfahrene Handwerker aus Gebal aus. In deinem Hafen lagen Schiffe aus aller Welt; in den Straßen versammelten sich die Seeleute, um Handel zu treiben. 10Söldner aus Persien, Lydien und Libyen dienten in deinem Heer, ihre Schilde und Helme verliehen dir Glanz. 11Männer aus Arwad verteidigten deine Mauern zusammen mit deinen eigenen Soldaten, und Gammaditer bewachten deine Türme; ihre Schilde hängten sie ringsum an deinen Mauern auf. So machten sie deine Schönheit vollkommen.

12Du warst eine reiche Stadt; viele Güter konnte man bei dir kaufen. Tarsis bot dir dafür Silber, Eisen, Zinn und Blei. 13Händler aus Jawan, aus Tubal und Meschech kauften bei dir und brachten dir dafür Sklaven und Gegenstände aus Kupfer. 14Die Bewohner von Bet-Togarma tauschten deine Waren gegen Zugpferde, Reitpferde und Maultiere. 15Die Kaufleute von Rhodos27,15 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: Dedan. und vielen anderen Inseln brachten dir Elefantenzähne und Ebenholz. 16Die Syrer27,16 Oder: Edomiter. – Aram (= Syrien) und Edom sind in der hebräischen Schrift leicht zu verwechseln. kauften viele deiner reichen Güter und gaben dir dafür roten Purpur, bunte Stoffe, feines Leinen, Korallen, Rubine und andere Edelsteine. 17Juda und Israel tauschten deine Waren gegen Weizen aus Minnit27,17 Dieser Ort wird in Richter 11,33 erwähnt. Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten., Hirse27,17 Oder: Feigen, Konfekt. – Die Bedeutung des hebräischen Wortes ist unsicher., Honig, Öl und duftendes Harz. 18Die Bewohner von Damaskus boten dir Wein aus Helbon und Wolle aus Zahar und bekamen dafür zahlreiche Schätze aus deinem großen Besitz. 19Die Leute von Wedan und Jawan aus dem Gebiet von Usal gaben dir Gegenstände aus Eisen sowie Zimt und andere Gewürze. 20Dedan tauschte deine Waren gegen Satteldecken ein. 21Die Fürsten von Arabien und Kedar gaben dir Lämmer, Schaf- und Ziegenböcke. 22Die Kaufleute von Saba und Ragma brachten dir die besten Balsamöle, allerlei Edelsteine und Gold. 23Haran, Kanne, Eden, die Händler von Saba, Assyrien und Kilmad – sie alle trieben Handel mit dir. 24Prächtige Gewänder boten sie dir, Mäntel aus violettem Purpur, bunte Stoffe, mehrfarbige Teppiche und gedrehte, feste Seile.27,24 Nicht alle in den Versen 12‒24 genannten Waren und Orte sind eindeutig zu bestimmen. 25Die Handelsschiffe27,25 Wörtlich: Tarsis-Schiffe. – So wurden große Handelsschiffe bezeichnet, die in der Lage waren, die weite Strecke bis nach Tarsis (im heutigen Spanien) zu segeln. kamen in großen Flotten zu dir und brachten deine Waren überallhin. So wurdest du immer reicher – ein voll beladenes Schiff mitten im Meer. 26Deine Ruderer fuhren mit dir über die hohe See. Doch es dauert nicht mehr lange, da wirst du mitten auf dem Meer vom Ostwind erfasst und zerbrochen! 27Alles, was dir gehört, stürzt dann in die Fluten: deine Waren, deine Seeleute und Matrosen, die Männer, die deine Lecks ausbessern, deine Kaufleute und Soldaten. Ja, wenn du fällst, versinkt deine ganze Pracht mit dir im Meer. 28Die Küsten erzittern, wenn sie das laute Geschrei deiner Besatzung hören. 29Alle Seeleute verlassen ihre Schiffe und bleiben voller Entsetzen an Land. 30Laut schreien und klagen sie über dich, streuen sich Staub auf den Kopf und wälzen sich in der Asche. 31Die Haare scheren sie sich ab und hüllen sich in Trauergewänder, sie vergießen bittere Tränen und halten die Totenklage über dich. 32Ja, in ihrem Schmerz stimmen sie ein Klagelied an:

›Was auf der Welt konnte man mit Tyrus vergleichen,

dieser Stadt, die nun totenstill im Meer ruht?

33Als deine Kaufleute über die Ozeane segelten,

haben sie vielen Völkern Schätze gebracht.

Deine Waren ließen Könige aus allen Winkeln der Erde

zu großem Reichtum gelangen.

34Jetzt aber bist du zerbrochen

und in den Tiefen des Meeres versunken.

Deine Güter und dein ganzer Reichtum –

nichts ist mehr davon zu sehen!

35Die Bewohner der Küstenländer

sind über dein Schicksal entsetzt,

ihren Königen stehen die Haare zu Berge,

das Grauen ist ihnen ins Gesicht geschrieben.

36Völker, die vorher deine Waren kauften –

sie alle verachten dich nun.

Ein Bild des Schreckens bist du geworden,

es ist aus mit dir für alle Zeit!‹«