Ezekieli 24 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 24:1-27

Mʼphika Wophikira

1Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino. 3Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Ikani mʼphika pa moto,

ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.

4Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama,

nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba.

Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.

5Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri.

Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo.

Madzi awire.

Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’

6“ ‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi,

tsoka kwa mʼphika wadzimbiri;

dzimbiri lake losachoka!

Mutulutsemo nthuli imodzimodzi

osasankhulapo.

7“ ‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo.

Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala.

Sanawakhutulire pa dothi

kuopa kuti fumbi lingawafotsere.

8Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala

kuti asafotseredwe ndi fumbi

chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.

9“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi!

Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.

10Choncho wonjeza nkhuni

ndipo muyatse moto.

Phikani nyamayo bwinobwino,

muthiremo zokometsera,

mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.

11Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo

mpaka utenthe kuchita kuti psuu

kuti zonyansa zake zisungunuke

ndi kuti dzimbiri lake lichoke.

12Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa.

Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka

ngakhale ndi moto womwe.

13“ ‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.

14“ ‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Imfa ya Mkazi wa Ezekieli

15Yehova anandiyankhula kuti: 16“Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi. 17Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”

18Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.

19Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”

20Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti, 21‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga. 22Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa. 23Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu. 24Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’

25“Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi. 26Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo. 27Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Hoffnung für Alle

Hesekiel 24:1-27

Jerusalem, ein rostiger Topf auf dem Feuer

1Im 9. Jahr unserer Verbannung24,1 Oder: der Regierung Zedekias. – Der Bezugspunkt der Datierung ist nicht ganz sicher. Vgl. 2. Könige 25,1., am 10. Tag des 10. Monats, empfing ich eine Botschaft vom Herrn. Er sagte zu mir: 2»Du Mensch, schreib dir das Datum des heutigen Tages auf, denn gerade heute beginnt der König von Babylonien mit der Belagerung Jerusalems! 3Und nun erzähl den Israeliten ein Gleichnis! Sag diesem widerspenstigen Volk: So spricht Gott, der Herr:

Stell einen Topf auf die Kochstelle

und gieß reichlich Wasser hinein!

4Füll ihn mit dem besten Fleisch,

mit Stücken von Lende und Schulter,

und gib auch Knochen voller Mark dazu!

5Nimm nur die besten deiner Schafe,

schichte Holz unter dem Topf auf

und lass das Fleisch tüchtig sieden,

zusammen mit all den Knochen!

6Denn ich, Gott, der Herr, sage: Wehe dir, du Stadt voller Bluttaten! Du bist ein Topf mit Rost, der nicht mehr abgeht! Wahllos wird das Fleisch aus dir herausgefischt, Stück für Stück, nichts bleibt zurück.

7Zum Himmel schreit das Blut, das deine Einwohner vergossen haben. Die nackten Felsen sind damit besudelt, und man deckt noch nicht einmal Erde darüber. 8Ich selbst habe dafür gesorgt, dass es so ist. Ja, das Blut soll nicht zugedeckt werden, damit sich mein Zorn daran entzündet und ich Rache nehme! 9Denn ich, Gott, der Herr, sage:

Wehe dir, du Stadt voller Bluttaten!

Auch ich schichte einen Holzstoß unter dir auf.

10Ja, bringt große Mengen Holz herbei!

Zündet das Feuer an, kocht das Fleisch,

bis die Brühe verdampft ist24,10 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten.

und die Knochen verkohlen!

11Stellt den leeren Topf auf das Feuer,

damit das Metall glühend heiß wird,

ja, damit der ganze Rost wegschmilzt,

der ihn beschmutzt!

12Vergebliche Mühe! Selbst im Feuer geht der Rost nicht ab!24,12 Oder: Der Rost geht einfach nicht ab, darum werft ihn ins Feuer!

13Jerusalem, durch dein schamloses Treiben hast du dich unrein gemacht, und selbst als ich dich reinigen wollte, bliebst du lieber, wie du warst. Darum wirst du nicht eher wieder rein werden, bis ich meinen Zorn an dir gestillt habe! 14Das sage ich, Gott, der Herr, und ich werde es auch tun. Ja, es kommt ganz bestimmt! Ich sehe nicht länger tatenlos zu. Keine Träne werde ich um dich vergießen, kein Mitleid mit dir haben. Ich ziehe dich zur Rechenschaft für das, was du getan hast. Mein Wort gilt!«

Der Tod von Hesekiels Frau – ein Zeichen für Jerusalem

15Wieder empfing ich eine Botschaft vom Herrn. Er sprach zu mir: 16»Du Mensch, durch einen plötzlichen Tod werde ich dir jemanden nehmen, der dir lieb und teuer ist. Doch du sollst nicht in lautes Klagen ausbrechen und nicht weinen. Keine Träne sollst du vergießen! 17Nur heimlich darfst du stöhnen, aber keine Totenklage halten! Lass dir deine Trauer nicht anmerken: Reiß dir nicht den Turban vom Kopf, und zieh auch deine Schuhe nicht aus! Verhüll nicht dein Gesicht, und nimm keine Trauermahlzeit ein!«

18Noch am selben Abend starb meine Frau, und am nächsten Morgen verhielt ich mich so, wie Gott es mir befohlen hatte. 19Da fragten mich die Leute: »Was hat dein seltsames Verhalten zu bedeuten? Willst du es uns nicht erklären?« 20Ich antwortete:

»Der Herr hat mir befohlen, 21euch Israeliten diese Botschaft weiterzugeben: So spricht Gott, der Herr: Ich weiß, dass der Tempel euch lieb und teuer ist. Ihr seid stolz auf den Schutz, den er euch bietet, und ihr sehnt euch nach ihm zurück. Doch ich werde dafür sorgen, dass mein Heiligtum entweiht und zerstört wird. Eure Söhne und Töchter, die ihr in Jerusalem zurückgelassen habt, fallen durchs Schwert. 22Dann werdet ihr euch genauso verhalten wie Hesekiel. Euer Gesicht werdet ihr nicht verhüllen und keine Trauermahlzeit zu euch nehmen. 23Eure Turbane und Schuhe werdet ihr anbehalten. Kein lautes Klagen und Weinen wird man von euch hören. Vor Trauer über eure Sünden geht ihr zugrunde, ihr könnt nur noch seufzen und stöhnen. 24Hesekiel ist ein Mahnzeichen für euch, es wird euch genauso ergehen wie ihm. Wenn es so weit ist, dann werdet ihr erkennen, dass ich Gott, der Herr, bin.«

25Weiter sprach Gott zu mir: »Du Mensch, lass es dir gesagt sein: Ich werde den Israeliten ihren Tempel entreißen, ihren Zufluchtsort, der ihnen so lieb und teuer ist. Ja, sie freuen sich über ihn und sehnen sich nach ihm zurück. Doch ich werde ihn zerstören, und auch ihre Söhne und Töchter lasse ich umkommen. 26An jenem Tag wird ein Überlebender aus Jerusalem zu dir kommen und dir davon berichten. 27Wenn er bei dir eintrifft, wirst du wieder reden können. Du wirst mit ihm sprechen und nicht länger stumm sein. So wirst du zu einem Mahnzeichen für die Israeliten, damit sie erkennen, dass ich der Herr bin.«