Nyimbo ya Maliro a Akalonga a Israeli
1“Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli. 2Uzinena kuti,
“ ‘Amayi ako anali ndani?
Anali ngati mkango waukazi!
Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna;
unkalera ana ake pakati pa misona.
3Unalera mmodzi mwa ana ake,
ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu.
Unaphunzira kugwira nyama,
ndipo unayamba kudya anthu.
4Anthu amitundu anamva za mkangowo,
ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo.
Iwo anawukoka ndi ngowe
kupita nawo ku dziko la Igupto.
5“ ‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera,
amayiwo anatenganso mwana wina
namusandutsa mkango wamphamvu.
6Unkayendayenda pakati pa mikango inzake,
pakuti tsopano unali mkango wamphamvu.
Unaphunzira kugwira nyama
ndipo unayamba kudya anthu.
7Unagwetsa malinga awo,
ndikuwononga mizinda yawo.
Onse a mʼdzikomo
anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
8Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira,
inabwera kudzalimbana nawo.
Anawutchera ukonde wawo,
ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
9Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga.
Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni
ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende
ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso
ku mapiri a Israeli.
10“ ‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa
wodzalidwa mʼmbali mwa madzi.
Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri
chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11Nthambi zake zinali zolimba,
zoyenera kupangira ndodo yaufumu.
Unatalika nusomphoka pakati pa
zomera zina.
Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake,
ndi nthambi zake zambiri.
12Koma unazulidwa mwaukali
ndipo unagwetsedwa pansi.
Unawuma ndi mphepo ya kummawa,
zipatso zake zinayoyoka;
nthambi zake zolimba zinafota
ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu,
dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14Moto unatulukanso mu mtengomo
ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake.
Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo
yoyenera kupangira ndodo yaufumu.
Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’ ”
Lamento por los príncipes de Israel
1»Dedícale este lamento a los príncipes de Israel:
2»“En medio de los leones,
tu madre era toda una leona.
Recostada entre leoncillos,
amamantaba a sus cachorros.
3A uno de ellos lo crio
y este llegó a ser un león fuerte
que aprendió a desgarrar su presa
y a devorar a la gente.
4Las naciones oyeron de él,
lo atraparon en una fosa
y lo llevaron con garfios a la tierra de Egipto.
5»”Cuando la leona madre perdió toda esperanza,
con sus expectativas perdidas,
tomó a otra de sus crías
y la hizo un león fuerte.
6Cuando este león se hizo fuerte,
merodeaba entre los leones.
Aprendió a desgarrar su presa
y a devorar a la gente.
7Demolía palacios19:7 Demolía palacios (lectura probable; véanse LXX y Targum); Conocía viudas (TM).
y asolaba ciudades.
La tierra y sus habitantes
estaban aterrorizados con sus rugidos.
8Las naciones y provincias vecinas
se dispusieron a atacarlo.
Extendieron su red sobre él
y quedó atrapado en la fosa.
9Enjaulado y con garfios
lo llevaron ante el rey de Babilonia.
Lo pusieron en prisión
para que no se oyeran sus rugidos
en los montes de Israel.
10»”Tu madre era como una vid en medio del viñedo,19:10 del viñedo (dos mss. hebreos); de tu sangre (TM).
plantada junto al agua.
Era fructífera y frondosa,
gracias al agua abundante.
11Sus ramas crecieron vigorosas,
¡aptas para ser cetros de reyes!
Tanto creció que se destacaba
por encima del follaje.
Se le reconocía por su altura
y por sus ramas frondosas.
12Pero fue desarraigada con furia
y arrojada por el suelo.
El viento del este la dejó marchita
y fueron arrancados sus frutos.
Secas quedaron sus vigorosas ramas,
y fueron consumidas por el fuego.
13Ahora está plantada en el desierto,
en tierra árida y reseca.
14De una de sus ramas brotó un fuego
y consumió sus frutos.
¡No queda en ella una rama vigorosa,
apta para ser cetro de gobernante!”.
Este es un lamento y debe entonarse como tal».