Ezekieli 18 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 18:1-32

Munthu Wochimwa Adzafa

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti:

“ ‘Nkhuyu zodya akulu zimapota

ndi ana omwe?’ ”

3“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli. 4Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.

5“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama

amene amachita zolungama ndi zolondola.

6Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo

kapena kupembedza mafano a Aisraeli.

Iye sayipitsa mkazi wa mnzake

kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.

7Iye sapondereza munthu wina aliyense,

koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake.

Iye salanda zinthu za osauka,

koma amapereka chakudya kwa anthu anjala,

ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.

8Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira,

kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu.

Amadziletsa kuchita zoyipa

ndipo sakondera poweruza milandu.

9Iye amatsatira malangizo anga,

ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika.

Munthu ameneyo ndi wolungama;

iye adzakhala ndithu ndi moyo,

akutero Ambuye Yehova.

10“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere. 11Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo.

“Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo.

Amayipitsa mkazi wa mnzake.

12Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa.

Amalanda zinthu za osauka.

Sabweza chikole cha munthu wa ngongole.

Iye amatembenukira ku mafano

nachita zonyansa.

13Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu.

Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.

14“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.

15“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo.

Sapembedza mafano a ku Israeli.

Sayipitsa mkazi wa mnzake.

16Sapondereza munthu wina aliyense.

Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka.

Salanda zinthu za munthu.

Amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.

17Amadziletsa kuchita zoyipa.

Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja.

Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga.

Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu. 18Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.

19“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse. 20Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.

21“ ‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi. 22Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo. 23Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.

24“ ‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.

25“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama? 26Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo. 27Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake. 28Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa. 29Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?

30“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo. 31Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli? 32Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

New International Reader’s Version

Ezekiel 18:1-32

People Will Die Because of Their Own Sins

1A message from the Lord came to me. The Lord said, 2“You people have a proverb about the land of Israel. What do you mean by it? It says,

“ ‘The parents eat sour grapes.

But the children have a bitter taste in their mouths.’

3“You will not use that proverb in Israel anymore,” announces the Lord and King. “And that is just as sure as I am alive. 4Everyone belongs to me. Parents and children alike belong to me. A person will die because of their own sins.

5“Suppose there is a godly man

who does what is fair and right.

6And he does not eat at the mountain temples.

He does not worship the statues of Israel’s gods.

He does not sleep with another man’s wife.

He does not have sex with his own wife

during her monthly period.

7He does not treat anyone badly.

Instead, he always returns things he takes

to make sure loans are paid back.

He does not steal.

Instead, he gives his food to hungry people.

He provides clothes for those who are naked.

8He does not charge interest when he lends money to them.

He does not make money from them.

He keeps himself from doing what is wrong.

He judges cases fairly.

9He obeys my rules.

He is faithful in keeping my laws.

He always does what is right.

You can be sure he will live,”

announces the Lord and King.

10“But suppose he has a mean son who harms other people. The son commits murder. Or he does some other things that are wrong. 11Suppose he does these things even though his father never did.

“Suppose the son eats at the mountain temples.

And he sleeps with another man’s wife.

12He treats poor and needy people badly.

He steals.

He does not pay back what he owes.

He worships statues of gods.

He does other things I hate.

13He charges interest when he lends money to poor people. He makes money from them.

Will a man like that live? He will not! He must be put to death. And what happens to him will be his own fault. He did many things I hate.

14“But suppose this son has a son of his own. And the son sees all the sins his father commits. He sees them, but he does not do them.

15“Suppose he does not eat at the mountain temples.

And he does not worship the statues of Israel’s gods.

He does not sleep with another man’s wife.

16He does not treat anyone badly.

He does not make people give him something

to prove they will pay back what they owe him.

He does not steal.

Instead, he gives his food to hungry people.

He provides clothes for those who are naked.

17He keeps himself from committing sins.

He does not charge interest when he lends money to poor people.

He does not make money from them.

He keeps my laws and obeys my rules.

He will not die because of his father’s sin. You can be sure he will live. 18But his father will die because of his own sin. He got rich by cheating others. He robbed his relatives. He also did what was wrong among his people.

19“But you still ask, ‘Is the son guilty along with his father?’ No! The son did what was fair and right. He was careful to obey all my rules. So you can be sure he will live. 20A person will die because of their own sins. A child will not be guilty because of what their parent did. And a parent will not be guilty because of what their child did. The right things a godly person does will be added to their account. The wrong things a sinful person does will be charged against them.

21“But suppose a sinful person turns away from all the sins they have committed. And they obey all my rules. They do what is fair and right. Then you can be sure they will live. They will not die. 22None of the sins they have committed will be held against them. Because of the godly things they have done, they will live. 23When sinful people die, it does not give me any joy,” announces the Lord and King. “But when they turn away from their sins and live, that makes me very happy.

24“Suppose a godly person stops doing what is right. And they sin. They do the same evil things a sinful person does. They do things I hate. Then they will not live. I will not remember any of the right things they have done. They have not been faithful to me. They have also committed many other sins. So they are guilty. They will die.

25“But you say, ‘What the Lord does isn’t fair.’ Listen to me, you Israelites. What I do is always fair. What you do is not. 26Suppose a godly person stops doing what is right. And they sin. Then they will die because of it. They will die because of the sin they have committed. 27But suppose a sinful person turns away from the evil things they have done. And they do what is fair and right. Then they will save their life. 28They think about all the evil things they have done. And they turn away from them. So you can be sure they will live. They will not die. 29But the Israelites still say, ‘What the Lord does isn’t fair.’ People of Israel, what I do is always fair. What you do is not.

30“So I will judge you Israelites. I will judge each of you in keeping with what you have done,” announces the Lord and King. “Turn away from your sins! Turn away from all the evil things you have done. Then sin will not bring you down. 31Get rid of all the evil things you have done. Let me give you a new heart and a new spirit. Then you will be faithful to me. Why should you die, people of Israel? 32When anyone dies, it does not give me any joy,” announces the Lord and King. “So turn away from your sins. Then you will live!