Ezekieli 15 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 15:1-8

Yerusalemu, Mtengo Wamphesa Wosabereka

1Yehova anayankhulanso nane kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, kodi mtengo wamphesa umapambana bwanji mtengo wina uliwonse? Nthambi zake zimapambana bwanji nthambi ina iliyonse. 3Mtengo umene uja nʼkupangira chiyani? Kodi anthu angathe kupangira chikhomo chokolekapo zinthu zawo? 4Taonani, ndi nkhuni chabe zosonkhera moto. Ukaponyedwa pa moto monga nkhuni ndi kuyaka mbali zonse ndi kusanduka makala, kodi ungagwiritsidwe ntchito ina iliyonse? 5Ngati pamene unali wosapsa sukanatheka kuwugwiritsa ntchito, nanga bwanji utapserera ndi moto, adzawugwiritsa ntchito bwanji?

6“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mtengo wamphesa ndidzawuponya mʼmoto monga ndimachitira ndi mitengo ina ya ku nkhalango. Momwemonso ndidzachita ndi anthu a ku Yerusalemu. 7Ndidzawalanga pamenepo ngakhale iwo atuluka pa moto, motowo udzawatenthabe. Ndipo pamene ndidzatsutsana nawo, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. 8Ine ndidzasandutsa dziko kukhala chipululu chifukwa anthu akhala osakhulupirika, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Thai New Contemporary Bible

เอเสเคียล 15:1-8

เยรูซาเล็มเถาองุ่นไร้ค่า

1พระดำรัสขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาถึงข้าพเจ้าว่า 2“บุตรมนุษย์เอ๋ย ไม้องุ่นมีอะไรดีกว่ากิ่งก้านของต้นไม้ใดๆ ในป่าหรือ? 3ไม้องุ่นจะนำมาใช้ประโยชน์อะไรได้เล่า? เอามาทำที่แขวนสิ่งใดได้หรือ? 4และเมื่อโยนลงไปในไฟเป็นเชื้อเพลิง ไฟเผาปลายทั้งสองข้าง และลุกไหม้ตรงกลางแล้ว มันจะใช้ประโยชน์อะไรได้? 5เมื่อมันยังดีอยู่ก็ทำประโยชน์อะไรไม่ได้ เมื่อถูกไฟเผาก็ยิ่งไม่มีประโยชน์

6“ฉะนั้นพระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตตรัสดังนี้ว่า เราโยนไม้องุ่นซึ่งอยู่ท่ามกลางไม้ป่าต่างๆ เป็นเชื้อไฟฉันใด เราก็จะปฏิบัติต่อผู้คนที่อาศัยอยู่ในเยรูซาเล็มฉันนั้น 7เราจะตั้งตนเป็นศัตรูกับพวกเขา แม้พวกเขาจะตะเกียกตะกายหนีออกมาจากไฟ ไฟก็ยังจะเผาผลาญพวกเขา และเมื่อเราตั้งตนเป็นศัตรูกับพวกเขา เจ้าจะรู้ว่าเราคือพระยาห์เวห์ 8เราจะทำให้ดินแดนนั้นถูกทิ้งร้าง เพราะพวกเขาไม่ซื่อสัตย์ พระยาห์เวห์องค์เจ้าชีวิตประกาศดังนั้น”