Ezekieli 14 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 14:1-23

Yehova Adzudzula Opembedza Mafano

1Tsiku lina ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kwa ine ndipo anakhala pansi pamaso panga. 2Ndipo Yehova anandipatsa uthenga uwu nati, 3“Iwe mwana wa munthu, anthu awa ayika mtima pa mafano awo. Ayikanso maso awo pa zinthu zina zoyipa zopunthwitsa. Kodi ayembekezera kuti ndiwayankhe chimene atandifunse? 4Tsono yankhula nawo ndi kuwawuza kuti zimene akunena Ambuye Yehova: ‘Ngati Mwisraeli aliyense ayika mtima wake pa mafano ndi kuyika maso ake pa zinthu zoyipa zopunthwitsa, kenaka nʼkupita kwa mneneri, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha molingana ndi kuchuluka kwa mafano ake. 5Ine ndidzachita zimenezi kuti mwina nʼkukopa mitima ya anthu a Israeli, amene andisiya chifukwa cha mafano awo.’

6“Nʼchifukwa chake uwawuze Aisraeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Lapani! Siyani mafano anu ndi ntchito zanu zonse zonyansa!

7“ ‘Ngati Mwisraeli wina aliyense kapena mlendo wina aliyense wokhala pakati pa Israeli adzichotsa yekha kwa Ine ndi kuyika mtima pa mafano ake ndi kuyikanso maso ake pa zinthu zopunthwitsa ndipo kenaka nʼkupita kwa mneneri kukafunsa nzeru, Ineyo Yehova mwini wakene ndidzamuyankha. 8Ine ndidzalimbana naye munthu ameneyo ndipo ndidzamusandutsa chitsanzo ndi chisudzo. Ndidzamuchotsa pakati pa anthu anga. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Ndipo ngati mneneri anyengedwa nanenera, Ine Yehova ndiye ndamunyenga mneneri ameneyo, ndipo ndidzatambasula dzanja langa kumukantha ndi kumuwononga pakati pa anthu anga Aisraeli. 10Iwo adzalangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo. Chilango cha wodzafunsira nzeru kwa mneneri chidzafanana ndi chilango cha mneneriyo. 11Ndidzachita zimenezi kuti Aisraeli asasocherenso kundisiya Ine ndi kuti asadziyipitsenso ndi machimo awo. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, akutero Ambuye Yehova.’ ”

Chilango Chosathawika

12Yehova anayankhula nane kuti, 13“Iwe mwana wa munthu, ngati dziko lindichimwira posandikhulupirira, Ine ndidzatambasula dzanja langa kulikantha pochepetsa chakudya chake. Ndidzatumiza njala pa dzikolo ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe. 14Ngakhale anthu atatu awa, Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, akanangopulumutsa moyo wawo chifukwa cha chilungamo chawo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

15“Kapena ndikanatumiza zirombo mʼdziko monse ndi kulisiya lopanda anthu, ndipo dzikolo nʼkukhala chipululu chakuti munthu sangadutse chifukwa cha zirombo. 16Apanso, ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna ndi aakazi. Iwo okha akanapulumuka, koma dziko likanasanduka chipululu.’

17“Kapena ndikanatumiza lupanga mʼdzikolo ndi kunena kuti, ‘Lupanga lipite mʼdziko monse,’ ndi kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe. 18Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Ngakhale anthu atatu awa akanakhalamo, sakanatha kupulumutsa ana awo aamuna kapena ana aakazi. Iwo okha akanapulumuka.’

19“Kapena ndikanatumiza mliri mʼdzikomo ndi kuonetsa ukali wanga pokhetsa magazi, kuwononga anthu ake ndi nyama zomwe. 20Apanso ndikunenetsa Ine Ambuye Yehova kuti ngakhale Nowa, Danieli ndi Yobu akanakhala mʼmenemo, sakanatha ngakhale kupulumutsa mwana wamwamuna kapena wamkazi. Akanangodzipulumutsa okha chifukwa cha chilungamo chawo.

21“Pakuti Ambuye Yehova akuti: Kudzakhala zoopsa kwambiri pamene ndidzatumiza pa Yerusalemu zilango zanga zinayi izi: lupanga, njala, zirombo ndi mliri kuti ziwononge anthu ake ndi nyama zomwe! 22Komabe padzakhala ena opulumuka, ana aamuna ndi ana aakazi amene adzatulutsidwa mʼdzikomo. Iwo adzabwera kwa inu, ndipo mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo, mitima yanu idzakhala pansi mukadzakumbukira chilango chimene ndinachita pa Yerusalemu. 23Mitima yanu idzakhala pansi mukadzaona makhalidwe awo ndi zochita zawo. Tsono mudzadziwa kuti Yerusalemu sindinamuchite zimenezi popanda chifukwa, akutero Ambuye Yehova.”

New International Reader’s Version

Ezekiel 14:1-23

The Lord Judges Those Who Worship Other Gods

1Some of the elders of Israel came to see me. They sat down with me. 2Then a message from the Lord came to me. The Lord said, 3“Son of man, these men have thought about nothing but other gods. They have fallen into the evil trap of worshiping them. Should I let these men ask me for any advice? 4Speak to them. Tell them, ‘The Lord and King says, “Suppose any of the Israelites think about other gods. And they fall into the evil trap of worshiping them. Then they go to a prophet to ask for advice. If they do, I myself will tell the prophet to answer them in keeping with their worship of many gods. 5I will win back the hearts of the people of Israel. All of them have deserted me for their other gods.” ’

6“So speak to the people of Israel. Tell them, ‘The Lord and King says, “Turn away from your sins! Also turn away from your gods. Give up all the evil things you have done. I hate them.

7“ ‘ “Suppose any of the Israelites or any outsiders who live in Israel separate themselves from me. And they think about other gods. They fall into the evil trap of worshiping them. Then they go to a prophet to ask me for advice. If they do, I myself will tell the prophet to answer them. 8I will turn against them. I will make an example out of them. People will talk about the bad things that happen to them. I will remove them from you. Then you will know that I am the Lord.

9“ ‘ “Suppose that prophet is stirred up to give a prophecy. Then I am the one who has stirred him up. And I will reach out my powerful hand against him. I will destroy him from among my people Israel. 10The prophet will be as much to blame as the one who asks him for advice. Both of them will be guilty. 11Then the people of Israel will no longer wander away from me. And they will not make themselves ‘unclean’ anymore with their many sins. They will be my people. And I will be their God,” ’ announces the Lord and King.”

Jerusalem Can’t Escape the Lord’s Judgment

12A message from the Lord came to me. The Lord said, 13“Son of man, suppose the people in a certain country sin against me. And they are not faithful to me. So I reach out my powerful hand against them. I cut off their food supply. I make them very hungry. I kill them and their animals. 14And suppose Noah, Daniel and Job were in that country. Then these three men could save only themselves by doing what is right,” announces the Lord and King.

15“Or suppose I send wild animals through that country. And they kill all its children. It becomes a dry and empty desert. No one can pass through it because of the animals. 16And suppose these three men were in that country. Then they could not save their own sons or daughters. They alone would be saved. But the land would become a dry and empty desert. And that is just as sure as I am alive,” announces the Lord and King.

17“Or suppose I send swords to kill the people in that country. And I say, ‘Let swords sweep all through the land.’ And I kill its people and their animals. 18And suppose these three men were in that country. Then they could not save their own sons or daughters. They alone would be saved. And that is just as sure as I am alive,” announces the Lord and King.

19“Or suppose I send a plague into that land. And I pour out my great anger on it by spilling blood. I kill its people and their animals. 20And suppose Noah, Daniel and Job were in that land. Then they could not save their own sons or daughters. They could save only themselves by doing what is right. And that is just as sure as I am alive,” announces the Lord and King.

21The Lord and King says, “It will get much worse. I will punish Jerusalem in four horrible ways. There will be war, hunger, wild animals and plague. They will destroy the people and their animals. 22But some people will be left alive. Some children will be brought out of the city. They will come to you. You will see how they act and the way they live. And you will be comforted in spite of all the trouble I brought on Jerusalem. 23You will be comforted when you see how they act and the way they live. Then you will know that I did not do anything there without a reason,” announces the Lord and King.