Estere 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 3:1-15

Chiwembu cha Hamani Chopha a Yuda

1Zitachitika izi, mfumu Ahasiwero anamukweza Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, anamulemekeza ndikumupatsa mpando wa ulemu kuposa nduna zina zonse. 2Atumiki onse a mfumu amene anali pa chipata cha nyumba ya mfumu ankagwadira ndi kuweramira Hamani monga mwa lamulo la mfumu. Koma Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira.

3Kenaka atumiki a mfumu amene anali pa chipata anafunsa Mordekai kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani sumvera lamulo la mfumu?” 4Tsiku ndi tsiku ankayankhula naye koma iye sanamverebe. Choncho anamuwuza Hamani kuti aone ngati angavomereze khalidwe lotere la Mordekai, popeza anawawuza kuti anali Myuda.

5Hamani ataona kuti Mordekai sankamugwadira kapena kumuweramira, anapsa mtima kwambiri. 6Hamani atamva kuti Mordekai anali Myuda, anatsimikiza kuti ndi kosakwanira kulanga Mordekai yekha. Mʼmalo mwake anapeza njira yowonongera Ayuda onse okhala mʼdziko lonse limene mfumu Ahasiwero ankalamulira.

7Mwezi woyamba, umene ndi mwezi wa Nisani, chaka cha khumi ndi chiwiri cha ufumu wa Ahasiwero anachita maere, otchedwa Purimu pamaso pa Hamani kuti apeze tsiku ndi mwezi woyenera. Ndipo maere anagwera pa mwezi wa khumi ndi chiwiri ndiwo mwezi wa Adara.

8Kenaka Hamani anakawuza mfumu Ahasiwero kuti, “Pali mtundu wina wa anthu umene unabalalika ndipo wamwazikana pa mitundu ina mʼzigawo zonse za ufumu wanu umene miyambo yawo ndi yosiyana ndi ya anthu ena onse ndiponso amene safuna kumvera malamulo a mfumu, kotero si chinthu cha phindu kuti mfumu iwalekerere anthu otere. 9Ngati chingakukomereni mfumu, ikani lamulo kuti tiwawononge, ndipo ndidzalipira matalente 10,000 asiliva mosungiramo chuma cha mfumu za anthu amene adzachite ntchito imeneyi.”

10Choncho mfumu inavula mphete yodindira ku chala chake ndi kumupatsa Hamani mwana wa Hamedata Mwagagi, mdani wa Ayuda. 11Mfumu inati kwa Hamani, “Sunga ndalamazo, ndipo uchite ndi anthuwo monga ufunira.”

12Alembi analemba zonse zimene Hamani analamula mʼmakalata opita kwa akazembe a mfumu, abwanamkubwa a zigawo zonse ndi kwa oyangʼanira mtundu uliwonse wa anthu. Kalatazo zinali za mʼchiyankhulo cha mtundu uliwonse ndipo zinalembedwa mʼdzina la Mfumu Ahasiwero ndi kusindikizidwa ndi mphete yake. 13Makalatawa anawatumiza amithenga ku zigawo zonse za mfumu kuti awononge, aphe ndi kufafaniziratu a Yuda onse, anyamata, anthu okalamba, ana ndi amayi, pa tsiku limodzi la 13 la mwezi wa Adara ndipo alande katundu wawo. 14Mwachidule kalatayi inanena kuti mawu olembedwamowo anayenera kuperekedwa ngati lamulo mʼchigawo chilichonse ndi kuti anthu a mtundu uliwonse adziwe ndi kukhala okonzeka pa tsikulo.

15Potsata lamulo la mfumu, amithenga aja anapita mwachangu ndipo lamuloli linaperekedwanso ku Susa, likulu la dziko. Mfumu ndi Hamani anakhala pansi ndikumamwa, koma mzinda onse wa Susa unasokonezeka.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以斯帖記 3:1-15

哈曼圖謀滅絕猶太人

1後來,亞哈隨魯王擢升亞甲哈米大他的兒子哈曼,使他的權位高過他所有的同僚。 2王命令所有在宮門供職的臣僕都要向哈曼跪拜,但末底改不肯跪拜。 3在宮門供職的臣僕問末底改:「你為何違抗王的命令?」 4他們天天勸他,他卻不聽。他們便把這件事告訴哈曼,想看看末底改這樣做是否能站得住,因為末底改已告訴他們自己是猶太人。 5哈曼末底改不肯向他跪拜,就怒氣填胸。 6他得知末底改猶太人後,便不屑於只害末底改一人,而是要剷除亞哈隨魯王國內所有的猶太人,即末底改的同胞。

7亞哈隨魯王十二年一月,即尼散月,有人在哈曼面前抽普珥,也就是抽籤,來決定哪月哪日下手,結果抽中十二月,即亞達月。

8哈曼亞哈隨魯王說:「有一個民族散居在王境內各省的眾民族中,他們的律例與各族的律例不同,他們不遵守王的律例,所以容忍他們對王不利。 9王若願意,就請降旨消滅他們。我願捐三百四十五噸銀子交給管理國事的人,納入王的庫房。」 10於是,王摘下手上的戒指,交給猶太人的仇敵——亞甲哈米大他的兒子哈曼11對他說:「這些銀子歸你,這個民族也交給你,隨你處置。」

12一月十三日,王的書記被召來,他們以亞哈隨魯王的名義,照哈曼的吩咐,用各省的文字和各族的語言寫諭旨,用王的戒指蓋印,送交各總督、各省省長和各族首領。 13諭旨由信差送到王的各省,限令在一天之內,即十二月,也就是亞達月十三日,把猶太人的男女老少全部剷除、殺光、滅盡,並奪取他們的財物。 14諭旨的抄本作為法令頒佈到各省,通知各族為那天做好準備。 15信差奉王的命令急忙上路,諭旨也在書珊城裡頒佈了。王和哈曼坐下飲酒,書珊城一片慌亂。