Eksodo 8 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 8:1-32

1Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Ukamuwuze Farao kuti, Lolani anthu anga kuti apite, akandipembedze. 2Ndipo ngati simulola kuti apite Ine ndidzalanga dziko lonse la Igupto polidzaza ndi achule. 3Mtsinje wa Nailo udzadzaza ndi achule. Achulewo adzatuluka ndi kukalowa mʼnyumba yaufumu, ku chipinda chogona ndi pa bedi lako, mʼnyumba za nduna zako ndi pa anthu ako ndi mophikira buledi ndiponso mopangira bulediyo. 4Achulewo adzakulumphira iwe ndi anthu ako ndiponso nduna zako.”

5Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti, ‘Loza ndodo yako ku mitsinje, ku ngalande ndi ku zithaphwi ndipo pakhale achule pa dziko lonse la Igupto.’ ”

6Kotero Aaroni analoza dzanja lake pa madzi a ku Igupto, ndipo achule anatuluka nadzaza dziko lonse la Igupto. 7Koma amatsenga anachita zinthu zomwezo mʼmatsenga awo. Iwonso anatulutsa achule mʼdziko lonse la Igupto.

8Kenaka, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Pemphera kwa Yehova kuti achulewa achoke kwa ine ndi anthu anga, ndipo ine ndidzalola kuti anthu anu apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”

9Mose anati kwa Farao, “Inu mungonditchulira nthawi imene mukufuna kuti ndikupempherereni, nduna zanu pamodzi ndi anthu anu kuti achule achoke mʼnyumba zanu ndi kuti atsale okhawo ali mu mtsinje wa Nailo.”

10Farao anati, “Mawa.”

Mose anamuyankha kuti, “Chabwino zidzakhala monga mwaneneramu, kuti mudzadziwe kuti palibe wina wofanana ndi Yehova Mulungu wathu. 11Achule adzachoka mʼnyumba yanu, mʼnyumba za nduna zanu pamodzi ndi za anthu anu. Koma adzatsala mu mtsinje wa Nailo basi.”

12Mose ndi Aaroni anachoka, ndipo Mose anapemphera kwa Yehova kuti achotse achule amene anatumiza kwa Farao. 13Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha. Achule amene anali mʼnyumba, mʼmabwalo ndi mʼminda anafa 14Aigupto anawunjika achulewo milumilu ndipo dziko linanunkha. 15Koma Farao ataona kuti zinthu zinayambanso kukhala bwino, anawumitsanso mtima wake ndipo sanamverenso mawu a Mose ndi Aaroni, monga momwe Yehova ananenera.

Mliri wa Nsabwe

16Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Uza Aaroni kuti akweze ndodo yake ndi kumenya fumbi la pa nthaka, ndipo fumbilo lidzasanduka nsabwe pa dziko lonse la Igupto.” 17Iwo anachita momwemo, ndipo pamene Aaroni anakweza ndodo yake ndi kumenya fumbi, nsabwe zinafika pa munthu aliyense ndi pa ziweto. Fumbi lonse la mʼdziko la Igupto linasanduka nsabwe. 18Koma amatsenga atayesa kupanga nsabwe mwa matsenga awo, analephera. Ndipo nsabwezo zinali pa munthu aliyense ndi pa ziweto zawo.

19Amatsenga anati kwa Farao, “Izi wachita ndi Mulungu.” Koma mtima wa Farao unali wowumabe ndipo sanamvere zonena za Mose ndi Aaroni monga momwe Yehova ananenera.

Mliri wa Ntchentche Zoluma

20Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Mmawa, upite ukakumane ndi Farao maso ndi maso pamene azidzapita ku madzi ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Lola anthu anga kuti apite akandipembedze. 21Koma ngati suwalola anthu anga kuti apite, Ine ndidzatumiza pa iwe ntchentche zoluma ndi pa nduna zako ndi anthu ako ndi mʼnyumba zanu. Mʼnyumba za Aigupto mudzadzaza ntchentche zoluma. Ngakhale pa nthaka pamene akhalapo padzadzaza ndi ntchentche zoluma.’ ”

22“Koma pa tsikulo ndidzapatula dera la Goseni, kumene kumakhala anthu anga, motero kuti sikudzakhala ntchentche zoluma. Choncho iwe udzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndikulamulira dziko lino. 23Ndidzasiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako. Chizindikiro chozizwitsa ichi chidzachitika mawa.”

24Ndipo Yehova anachita zimenezi: Ntchentche zoluma zochuluka zinalowa mʼnyumba yaufumu ya Farao ndi nyumba za nduna zake. Choncho ntchentche zolumazi zinawononga dziko lonse la Igupto.

25Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kaperekeni nsembe kwa Mulungu wanu mʼdziko lomwe lino.”

26Koma Mose anati, “Sitingathe kutero pakuti nsembe zathu kwa Yehova Mulungu ndi zowayipira Aigupto. Ngati tipereke nsembe zowayipira Aigupto mʼmaso mwawo, adzatiponya miyala kuti tife. 27Ife tiyenera kuyenda ulendo wa masiku atatu kupita ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wathu monga anatilamulira.”

28Farao anati, “Ine ndikulolani kuti mupite ku chipululu kukapereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu, koma musapite kutali kwambiri. Tsopano ndipempherereni.”

29Mose anayankha kuti, “Ine ndikangochoka pano, ndikapemphera kwa Yehova ndipo mawa lomweli ntchentche zoluma zidzachoka kwa Farao, nduna zake pamodzi ndi anthu ake. Koma Farao, onetsetsani kuti musachitenso zachinyengo ndi kuwakaniza anthu kuti asakapereke nsembe kwa Yehova.”

30Choncho Mose anasiyana ndi Farao nakapemphera kwa Yehova. 31Ndipo Yehova anachita zomwe Mose anapempha: Ntchentche zoluma zinachoka kwa Farao ndi nduna zake ndiponso kwa anthu ake. Palibe ngakhale imodzi yomwe inatsala. 32Koma nthawi imeneyinso Farao anawumitsa mtima wake ndipo sanalole kuti anthu atuluke.

New Russian Translation

Исход 8:1-32

Второе наказание: лягушки

1Господь сказал Моисею:

– Пойди к фараону и скажи ему: «Так говорит Господь: Отпусти Мой народ поклониться Мне. 2Если ты откажешься, Я наведу на всю твою страну лягушек. 3Нил будет кишеть лягушками. Они вылезут из реки и прискачут в твой дворец, в спальню, на постель, в дома твоих приближенных и народа8:3 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «и на твой народ»., в твои печи и квашни. 4Лягушки будут прыгать на тебя, на твой народ и на твоих приближенных».

5Господь сказал Моисею:

– Скажи Аарону: «Занеси руку с посохом над реками, каналами и прудами и наведи лягушек на египетскую землю».

6Аарон занес руку с посохом над водами Египта, и вылезли лягушки и покрыли всю землю. 7Но чародеи с помощью колдовства сделали то же самое. Они тоже навели лягушек на Египет. 8Фараон позвал Моисея и Аарона и сказал:

– Помолитесь Господу, чтобы Он избавил от лягушек меня и мой народ, и я отпущу народ принести жертву Господу.

9Моисей сказал фараону:

– Я предоставляю тебе честь выбрать, когда мне помолиться за тебя, за твоих приближенных и народ. После этого лягушки уйдут от тебя и из твоих дворцов и останутся только в Ниле.

10– Завтра, – сказал фараон.

Моисей ответил:

– Будет по-твоему для того, чтобы ты узнал: нет никого, подобного Господу, нашему Богу. 11Лягушки уйдут от тебя и из твоих дворцов, от твоих приближенных и народа. Они останутся только в Ниле.

12Моисей и Аарон ушли от фараона, и Моисей попросил Господа уничтожить всех лягушек, которых Он навел на фараона. 13Господь исполнил просьбу Моисея. Лягушки вымерли в домах, во дворах и на полях. 14Их собирали в кучи, и земля начала испускать зловоние. 15Но когда фараон увидел, что пришло облегчение, его сердце исполнилось упрямством, и он опять не послушал Моисея и Аарона, как и говорил Господь.

Третье наказание: комары

16Господь сказал Моисею:

– Скажи Аарону: «Подними посох и ударь по пыли на земле: по всему Египту пыль превратится в комаров».

17Они сделали так. Аарон поднял руку с посохом, ударил по пыли, и на людей и скот налетели комары. Пыль по всему Египту превратилась в комаров. 18Чародеи попытались с помощью колдовства навести комаров, но не смогли. Комары облепляли людей и скотину. 19И тогда чародеи сказали фараону:

– Это сделал Бог.

Но сердце фараона оставалось упрямым. Он не послушал их, как и говорил Господь.

Четвертое наказание: мухи

20Господь сказал Моисею:

– Поднимись завтра рано утром, встань перед фараоном, когда он пойдет к реке, и скажи ему: «Так говорит Господь: Отпусти Мой народ поклониться Мне. 21Если не отпустишь, Я пошлю на тебя, на твоих приближенных, на твой народ и в твои дворцы рои мух. Дома египтян наполнятся мухами и вся земля будет покрыта ими. 22Но Я сделаю так, что в земле Гошен, где живет Мой народ, не будет мух, чтобы ты знал – Я, Господь, пребываю в той земле. 23Я сделаю различие8:23 Так в некоторых древних переводах; в нормативном еврейском тексте: «положу избавление». между Моим и твоим народом. Это знамение будет завтра».

24Господь так и сделал. Густые рои мух налетели во дворец фараона и в дома его приближенных. Из-за мух погибала вся египетская земля. 25Фараон позвал Моисея и Аарона и сказал:

– Идите, принесите жертву вашему Богу в этой стране.

26Но Моисей сказал:

– Так делать нельзя. То, что мы приносим в жертву Господу, нашему Богу, для египтян – мерзость. Если мы станем приносить жертву, которой они гнушаются, они забьют нас камнями. 27Нет, чтобы принести жертву Господу, нашему Богу, как Он велел, нам нужно удалиться на три дня в пустыню.

28Фараон сказал:

– Я отпущу вас принести жертву Господу, вашему Богу, в пустыню, но только не уходите далеко. Помолитесь и обо мне.

29Моисей ответил:

– Как только я уйду от тебя, я помолюсь Господу, и завтра мухи оставят тебя, твоих приближенных и народ. Но и ты больше не обманывай, не отпуская народ принести жертву Господу.

30Моисей ушел от фараона и помолился Господу. 31Господь сделал то, что просил Моисей: избавил фараона, его приближенных и народ от мух. Ни одной мухи не осталось. 32Но и на этот раз сердце фараона осталось упрямым, и он не отпустил народ.