Eksodo 40 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 40:1-38

Adzutsa Chihema

1Kenaka Yehova anati kwa Mose, 2“Imika chihema, tenti ya msonkhano, tsiku loyamba la mwezi. 3Uyikemo bokosi la umboni ndipo uphimbe bokosilo ndi katani. 4Ulowetsemo tebulo ndi kuyika zimene zimakhala pamenepo. Kenaka ulowetse choyikapo nyale ndipo uyikepo nyale zake. 5Uyike guwa lofukiza la golide patsogolo pa bokosi la umboni ndipo uyike katani ya pa chipata cha chihema.

6“Uyike guwa lansembe yopsereza patsogolo pa chipata cha chihema, tenti ya msonkhano. 7Uyike beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo uyikemo madzi. 8Upange bwalo lozungulira chihemacho ndipo uyike katani ya pa chipata cha bwalolo.

9“Utenge mafuta wodzozera ndipo udzoze chihema ndi chilichonse chili mʼmenemo ndipo zidzakhala zoyeretsedwa. 10Kenaka udzoze guwa lansembe lopsereza ndi ziwiya zake zonse. Ulipatule guwalo ndipo lidzakhala loyera kwambiri. 11Udzoze beseni ndi miyendo yake ndipo uzipatule.

12“Ubwere ndi Aaroni ndi ana ake pa chipata cha tenti ya msonkhano ndipo uwasambitse ndi madzi. 13Kenaka umuveke Aaroni zovala zopatulika, umudzoze ndi kumupatula kotero kuti athe kunditumikira monga wansembe. 14Ubweretse ana ake ndipo uwaveke minjiro. 15Uwadzoze monga momwe unadzozera abambo awo, kotero kuti anditumikire monga ansembe. Kudzozedwako kudzakhala unsembe wawo pa mibado ndi mibado” 16Mose anachita zonse monga Yehova anamulamulira.

17Kotero anayimika chihema tsiku loyamba la mwezi woyamba mʼchaka chachiwiri. 18Nthawi imene Mose anayimika chihema, anayika matsinde mʼmalo ake, kuyimitsa maferemu, kulowetsa mitanda ndi kuyika nsichi. 19Kenaka anayika tenti pamwamba pa chihema ndipo anayika chophimba pa tenti monga momwe Yehova analamulira Mose.

20Iye anatenga miyala ya umboni nayika mʼbokosi lija ndi kuyika chivundikiro pamwamba pake. 21Kenaka analowetsa bokosilo mʼchihema ndipo anapachika katani ndi kubisa bokosi la umboni monga momwe Yehova analamulira iye.

22Mose anayika tebulo mu tenti ya msonkhano kumpoto kwa chihema, kunja kwa katani, 23ndipo anayikapo buledi pamaso pa Yehova, monga momwe Yehova analamulira Mose.

24Iye anayikanso choyikapo nyale mu tenti ya msonkhano moyangʼanana ndi tebulo mbali yakummwera kwa chihema. 25Ndipo anayikapo nyale zija pamaso pa Yehova, monga Yehova analamulira Mose.

26Mose anayika guwa la golide mu tenti ya msonkhano patsogolo pa katani 27ndipo anapserezapo lubani wonunkhira monga Yehova anamulamulira. 28Kenaka anayika katani ya pa chipata cha chihema.

29Iye anayika guwa lansembe yopsereza pafupi ndi chipata cha chihema, tenti ya msonkhano, ndipo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya ufa monga Yehova anamulamulira.

30Iye anayika beseni pakati pa tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe ndipo anathiramo madzi wosamba, 31ndipo Mose, Aaroni ndi ana ake amasamba manja ndi mapazi awo. 32Iwo amasamba nthawi zonse akamalowa mu tenti ya msonkhano kapena kuyandikira guwa lansembe monga Yehova analamulira Mose.

33Kenaka Mose anamanga bwalo kuzungulira chihema ndi guwa lansembe ndipo anayika katani ya pa chipata cha bwalo. Kotero Mose anamaliza ntchito.

Ulemerero wa Yehova

34Kenaka mtambo unaphimba tenti ya msonkhano, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho. 35Mose sanathe kulowa mu tenti ya msonkhano chifukwa mtambo unali utakhazikika pa chihemacho, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza mʼchihemacho.

36Pa maulendo awo onse, mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso pamene analipo. 37Koma ngati mtambo sunachoke, iwo sankasamukanso mpaka tsiku limene udzachoke. 38Kotero mtambo wa Yehova unkakhala pamwamba pa chihema usana, ndi mtambo wamoto umakhala usiku, pamaso pa nyumba yonse ya Israeli pa masiku onse aulendo wawo.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Éxodo 40:1-38

Se levanta el santuario

1El Señor habló con Moisés y le dijo: 2«En el día primero del mes primero, levanta el santuario, es decir, la Tienda de reunión. 3Pon en su interior el arca del pacto, y cúbrela con la cortina. 4Lleva adentro la mesa y ponla en orden. Pon también dentro del santuario el candelabro, y enciende sus lámparas. 5Coloca el altar del incienso frente al arca del pacto, y cuelga la cortina a la entrada del santuario.

6»Coloca el altar de los holocaustos frente a la entrada del santuario, la Tienda de reunión; 7coloca el lavamanos entre la Tienda de reunión y el altar, y pon agua en él. 8Levanta el atrio en su derredor, y coloca la cortina a la entrada del atrio.

9»Toma el aceite de la unción, y unge el santuario y todo lo que haya en él; conságralo, junto con todos sus utensilios, para que sea un objeto sagrado. 10Unge también el altar de los holocaustos y todos sus utensilios; conságralo, para que sea un objeto muy sagrado. 11Unge además, y consagra, el lavamanos y su pedestal.

12»Lleva luego a Aarón y a sus hijos a la entrada de la Tienda de reunión, haz que se bañen, 13y ponle a Aarón sus vestiduras sagradas. Úngelo y conságralo, para que ministre como sacerdote mío. 14Acerca entonces a sus hijos, ponles sus túnicas, 15y úngelos como ungiste a su padre, para que ministren como mis sacerdotes. La unción les conferirá un sacerdocio válido para todas las generaciones venideras».

16Moisés hizo todo tal y como el Señor se lo mandó. 17Fue así como el santuario se instaló el día primero del mes primero del año segundo. 18Al instalar el santuario, Moisés puso en su lugar las bases, levantó los tablones, los insertó en los travesaños, y levantó los postes; 19luego extendió la tienda de campaña sobre el santuario, y encima de esta puso el toldo, tal y como el Señor se lo mandó.

20A continuación, tomó el documento del pacto y lo puso en el arca; luego ajustó las varas al arca, y sobre ella puso el propiciatorio. 21Llevó el arca al interior del santuario, y colgó la cortina para resguardarla. De este modo protegió el arca del pacto, tal y como el Señor se lo había ordenado.

22Moisés puso la mesa en la Tienda de reunión, en el lado norte del santuario, fuera de la cortina, 23y puso el pan en orden ante el Señor, como el Señor se lo había ordenado. 24Colocó luego el candelabro en la Tienda de reunión, frente a la mesa, en el lado sur del santuario, 25y encendió las lámparas ante el Señor, como el Señor se lo había ordenado. 26Puso también el altar de oro en la Tienda de reunión, frente a la cortina, 27y sobre él quemó incienso aromático, tal y como el Señor se lo había ordenado. 28Después de eso colgó la cortina a la entrada del santuario.

29Moisés puso también el altar de los holocaustos a la entrada del santuario, la Tienda de reunión, y sobre él ofreció holocaustos y ofrendas de grano, tal y como el Señor se lo había ordenado. 30Colocó luego el lavamanos entre la Tienda de reunión y el altar, y echó en ella agua para lavarse, 31y Moisés, Aarón y sus hijos se lavaron allí las manos y los pies. 32Siempre que entraban en la Tienda de reunión o se acercaban al altar se lavaban, tal y como el Señor se lo había ordenado.

33Después levantó Moisés el atrio en torno al santuario y al altar, y colgó la cortina a la entrada del atrio. Así terminó Moisés la obra.

La gloria del Señor

34En ese instante, la nube cubrió la Tienda de reunión, y la gloria del Señor llenó el santuario. 35Moisés no podía entrar en la Tienda de reunión porque la nube se había posado en ella y la gloria del Señor llenaba el santuario.

36Siempre que la nube se levantaba y se apartaba del santuario, los israelitas levantaban campamento y se ponían en marcha. 37Si la nube no se levantaba, ellos no se ponían en marcha. 38Durante todas las marchas de los israelitas, la nube del Señor reposaba sobre el santuario durante el día, pero durante la noche había fuego en la nube, a la vista de todo el pueblo de Israel.