Eksodo 4 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 4:1-31

Mulungu Apatsa Mose Mphamvu Zochita Zodabwitsa

1Mose anayankha, “Aisraeliwo sakandikhulupirira ndipo sakandimvera. Iwowo adzati, ‘Yehova sanakuonekere iwe.’ ”

2Ndipo Yehova anamufunsa nati, “Nʼchiyani chili mʼdzanja lakolo?”

Mose anayankha kuti, “Ndodo.”

3Yehova anati, “Tayiponya pansi.”

Mose anayiponya pansi ndipo inasanduka njoka ndipo anayithawa. 4Kenaka Yehova anati kwa iye, “Igwire mtchira.” Ndipo Mose anayigwira mchira njokayo ndipo inasandukanso ndodo mʼdzanja lake. 5Yehova anati, “Ukachite zimenezi ndipo akakukhulupirira kuti Yehova, Mulungu wa makolo awo, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo, wakuonekera iwe.”

6Yehova anatinso, “Pisa dzanja lako mʼmalaya akowo.” Choncho Mose anapisa dzanja lake mʼmalaya ake ndipo pamene analitulutsa, linali la khate kuchita kuti mbuu ngati ufa.

7Yehova anati, “Tsopano pisanso dzanja lako mʼmalaya.” Mose anapisanso dzanja lakelo mʼmalaya ake ndipo atalitulutsa, linali labwinobwino, ngati thupi lake lonse.

8Tsono Yehova anati “Akakapanda kukukhulupirira, osalabadira chozizwitsa choyambacho, akakhulupirira ndithu chifukwa cha chozizwitsa chachiwiricho. 9Koma ngati sakakhulupirira zizindikiro ziwiri izi kapena kukumvera, ukatunge madzi a mu mtsinje wa Nailo ndi kuwathira pa mtunda powuma ndipo madziwo adzasanduka magazi.”

10Mose anati kwa Yehova, “Chonde Ambuye, chikhalire ine ndakhala munthu wosatha kuyankhula bwino. Ngakhale tsopano pamene mukundiyankhula, lilime langa ndi lolemera. Ndine wachibwibwi.”

11Yehova anati kwa iye, “Kodi anapatsa munthu pakamwa ndani? Ndani amasandutsa munthu kuti akhale wosayankhula kapena wosamva? Ndani amapanga munthu kukhala wopenya kapena wosaona? Kodi si Ine Yehova? 12Tsopano pita, Ine ndidzakuthandiza kuyankhula ndipo ndidzakulangiza zoti ukanene.”

13Koma Mose anati, “Chonde Ambuye, pepani, tumani wina kuti akachite zimenezi.”

14Kenaka Yehova anamupsera mtima Mose ndipo anati, “Kodi suli ndi mʼbale wako Aaroni wa fuko la Levi? Ine ndikudziwa kuti iye amayankhula bwino. Iye wanyamuka kale kudzakumana nawe ndipo adzasangalala akadzakuona. 15Iwe udzayankhula naye ndi kumuwuza mawu oti akanene. Ine ndidzakuthandizani kuyankhula nonse awirinu ndi kukulangizani zoti mukachite. 16Iye akayankhula kwa anthu mʼmalo mwako. Iye adzakhala wokuyankhulira ndipo iweyo udzakhala ngati Mulungu kwa iye. 17Koma utenge ndodo imene ili mʼdzanja lakoyo kuti ukachite nayo zizindikiro zozizwitsa.”

Mose Abwerera ku Igupto

18Tsono Mose anabwerera kwa Yetero, mpongozi wake ndipo anati kwa Iye, “Chonde ndiloleni kuti ndibwerere ku Igupto kwa anthu anga kuti ndikaone ngati ali moyo.”

Yeteri anati, “Pitani mu mtendere.”

19Nthawiyi Yehova anali atamuwuza kale Mose ku Midiyani kuti, “Bwerera ku Igupto, pakuti anthu onse amene amafuna kukupha aja anamwalira.” 20Kotero Mose anatenga mkazi wake ndi ana ake aamuna, ndipo anawakweza pa bulu nayamba ulendo wobwerera ku Igupto. Ndipo anatenga ndodo ya Mulungu ija mʼdzanja lake.

21Yehova anati kwa Mose, “Ukaonetsetse kuti wachita pamaso pa Farao zodabwitsa zonse zimene ndayika mphamvu mwa iwe kuti ukachite. Koma Ine ndidzawumitsa mtima wake kotero kuti sadzalola anthuwo kuti apite. 22Ndipo iwe ukati kwa Farao, ‘Yehova akuti, Israeli ali ngati mwana wanga wachisamba.’ 23Choncho ndikuti, ‘Mulole mwana wanga apite kuti akandipembedze. Koma ngati ukana, Ine ndidzapha mwana wako wachisamba.’ ”

24Pambuyo pake Mose ali mʼnjira, pamalo wogona, Yehova anakumana naye, ndipo anafuna kumupha. 25Koma Zipora anatenga mwala wakuthwa nachita mdulidwe mwana wake ndipo khungulo analikhudzitsa pa mapazi a Mose. Iye anati “Zoonadi, kwa ine ndiwe mkwati wamagazi.” 26Choncho Yehova anamuleka Mose wosamupha. Pa nthawiyo, Zipora anati, “Mkwati wa magazi,” ponena za mdulidwe.

27Yehova anati kwa Aaroni, “Pita ku chipululu ukakumane ndi Mose.” Iye anapitadi nakakumana ndi Mose pa phiri la Mulungu namupsompsona. 28Kenaka Mose anamufotokozera Aaroni chilichonse chimene Yehova anamutuma kuti akanene. Anamufotokozera za zizindikiro zozizwitsa zimene anamulamulira kuti akazichite.

29Mose ndi Aaroni anapita kukasonkhanitsa pamodzi akuluakulu onse a Aisraeli. 30Ndipo Aaroni anawafotokozera zonse zimene Yehova ananena kwa Mose. Anachita zizindikirozo pamaso pa anthu onse, 31ndipo anakhulupirira. Iwo atamva kuti Yehova anadzawayendera ndi kuti waona mmene akuzunzikira, anaweramitsa mitu pansi napembedza.

New International Version – UK

Exodus 4:1-31

Signs for Moses

1Moses answered, ‘What if they do not believe me or listen to me and say, “The Lord did not appear to you”?’

2Then the Lord said to him, ‘What is that in your hand?’

‘A staff,’ he replied.

3The Lord said, ‘Throw it on the ground.’

Moses threw it on the ground and it became a snake, and he ran from it. 4Then the Lord said to him, ‘Reach out your hand and take it by the tail.’ So Moses reached out and took hold of the snake and it turned back into a staff in his hand. 5‘This,’ said the Lord, ‘is so that they may believe that the Lord, the God of their fathers – the God of Abraham, the God of Isaac and the God of Jacob – has appeared to you.’

6Then the Lord said, ‘Put your hand inside your cloak.’ So Moses put his hand into his cloak, and when he took it out, the skin was leprous4:6 The Hebrew word for leprous was used for various diseases affecting the skin. – it had become as white as snow.

7‘Now put it back into your cloak,’ he said. So Moses put his hand back into his cloak, and when he took it out, it was restored, like the rest of his flesh.

8Then the Lord said, ‘If they do not believe you or pay attention to the first sign, they may believe the second. 9But if they do not believe these two signs or listen to you, take some water from the Nile and pour it on the dry ground. The water you take from the river will become blood on the ground.’

10Moses said to the Lord, ‘Pardon your servant, Lord. I have never been eloquent, neither in the past nor since you have spoken to your servant. I am slow of speech and tongue.’

11The Lord said to him, ‘Who gave human beings their mouths? Who makes them deaf or mute? Who gives them sight or makes them blind? Is it not I, the Lord? 12Now go; I will help you speak and will teach you what to say.’

13But Moses said, ‘Pardon your servant, Lord. Please send someone else.’

14Then the Lord’s anger burned against Moses and he said, ‘What about your brother, Aaron the Levite? I know he can speak well. He is already on his way to meet you, and he will be glad to see you. 15You shall speak to him and put words in his mouth; I will help both of you speak and will teach you what to do. 16He will speak to the people for you, and it will be as if he were your mouth and as if you were God to him. 17But take this staff in your hand so that you can perform the signs with it.’

Moses returns to Egypt

18Then Moses went back to Jethro his father-in-law and said to him, ‘Let me return to my own people in Egypt to see if any of them are still alive.’

Jethro said, ‘Go, and I wish you well.’

19Now the Lord had said to Moses in Midian, ‘Go back to Egypt, for all those who wanted to kill you are dead.’ 20So Moses took his wife and sons, put them on a donkey and started back to Egypt. And he took the staff of God in his hand.

21The Lord said to Moses, ‘When you return to Egypt, see that you perform before Pharaoh all the wonders I have given you the power to do. But I will harden his heart so that he will not let the people go. 22Then say to Pharaoh, “This is what the Lord says: Israel is my firstborn son, 23and I told you, ‘Let my son go, so that he may worship me.’ But you refused to let him go; so I will kill your firstborn son.” ’

24At a lodging place on the way, the Lord met Moses4:24 Hebrew him and was about to kill him. 25But Zipporah took a flint knife, cut off her son’s foreskin and touched Moses’ feet with it.4:25 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain. ‘Surely you are a bridegroom of blood to me,’ she said. 26So the Lord let him alone. (At that time she said ‘bridegroom of blood’, referring to circumcision.)

27The Lord said to Aaron, ‘Go into the wilderness to meet Moses.’ So he met Moses at the mountain of God and kissed him. 28Then Moses told Aaron everything the Lord had sent him to say, and also about all the signs he had commanded him to perform.

29Moses and Aaron brought together all the elders of the Israelites, 30and Aaron told them everything the Lord had said to Moses. He also performed the signs before the people, 31and they believed. And when they heard that the Lord was concerned about them and had seen their misery, they bowed down and worshipped.