Eksodo 34 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 34:1-35

Miyala ina Yatsopano

1Yehova anati kwa Mose, “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo Ine ndidzalembapo mawu amene anali pa miyala yoyamba ija, imene unayiphwanya. 2Ukonzeke mmamawa, ndipo ubwere ku Phiri la Sinai. Udzaonekera pamaso panga pamwamba pa phiri. 3Palibe amene abwere nawe kapena kuoneka pena paliponse pafupi ndi phiri. Ndipo ngakhale nkhosa kapena ngʼombe zisadye mʼmbali mwa phirilo.”

4Choncho Mose anasema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija ndipo anapita ku Phiri la Sinai mmawa atanyamula miyala iwiri mʼmanja mwake monga momwe Yehova anamulamulira. 5Ndipo Yehova anatsika mu mtambo ndi kuyima pamodzi ndi Mose ndi kulengeza dzina lake lakuti Yehova. 6Ndipo Iye anadutsa kutsogolo kwa Mose akulengeza kuti, “Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima, wosapsa mtima msanga, wodzaza ndi chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, 7waonetsa chikondi chosasinthika kwa anthu miyandamiyanda, wokhululukira zoyipa, kuwukira, ndiponso tchimo, komatu salekerera ochimwa kuti asalangidwe. Iye amalanga ana ndi zidzukulu chifukwa cha machimo a makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi.”

8Pamenepo Mose anawerama pansi napembedza. 9Iye anati, “Chonde Ambuye, ngati ndapeza chisomo pamaso panu, lolani Ambuye kuti mupite nafe pamodzi. Ngakhale kuti anthuwa ndi nkhutukumve, khululukirani zoyipa ndi machimo athu, ndipo mutenge ife kukhala anthu anu.”

10Choncho Yehova anati: “Ine ndikuchita nanu pangano. Ndidzachita zodabwitsa pamaso pa anthu onse zimene sizinachitikenso ndi mtundu wina uliwonse wa anthu pa dziko lonse lapansi. Anthu amene mudzakhala pakati pawo adzaona kuopsa kwa ntchito imene Ine Yehova ndidzakuchitireni. 11Mverani zimene ndikukulamulirani lero. Ine ndidzathamangitsa pamaso panu Aamori, Akanaani, Ahiti, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi. 12Musamale kuti musakachite mgwirizano ndi anthu amene akukhala mʼdziko limene mukupitalo, chifukwa mukadzatero iwo adzakhala ngati msampha pakati panu. 13Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, ndipo mukadule mitengo yawo ya Asera. 14Musapembedze mulungu wina, pakuti Yehova amene dzina lake ndi Nsanje, ndi Mulungu wa nsanje.

15“Musamale kuti musakachite mgwirizano ndi anthu amene akukhala mʼdziko limene mukupitalo, chifukwa iwo akamakachita zadama ndi milungu yawo ndi kupereka nsembe, adzakuyitanani ndipo inu mudzadya nsembe zawo. 16Ndipo inu mukasankha ena mwa ana awo aakazi kukhala akazi a ana anu, akaziwo akakachita zadama ndi milungu yawo, akatsogolera ana anu aamuna kuchita chimodzimodzi.

17“Musadzipangire milungu yosungunula.

18“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti. Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti monga momwe ndinakulamulirani. Muzichita zimenezi pa nthawi yoyikika mwezi wa Abibu, pakuti mwezi umenewu inu munatuluka mʼdziko la Igupto.

19“Mwana aliyense woyamba kubadwa ndi wanga, pamodzi ndi ziweto zoyamba kubadwa zazimuna kuchokera ku ngʼombe kapena nkhosa. 20Muziwombola mwana woyamba kubadwa wa bulu popereka mwana wankhosa. Mukapanda kumuwombola mupheni. Muziwombola ana anu onse aamuna.

“Palibe ndi mmodzi yemwe adzaonekere pamaso panga wopanda kanthu mʼdzanja lake.

21“Muzigwira ntchito masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri, musagwire ntchito ina iliyonse, Ngakhale nthawi yolima ndi yokolola muyenera kupuma.

22“Muzichita Chikondwerero cha Masabata, chifukwa ndi chikondwerero cha tirigu woyambirira kucha, ndiponso ndi chikondwerero cha kututa zokolola pakutha pa chaka. 23Amuna onse azionekera pamaso pa Yehova Mulungu wa Israeli, katatu pa chaka. 24Ine ndidzapirikitsa mitundu inayo pamene inu mukufikako ndi kukulitsa malire anu. Palibe ndi mmodzi yemwe adzafune kulanda dziko lanu ngati inu muzidzapita katatu pa chaka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, chaka chilichonse.

25“Musapereke magazi anyama ngati nsembe kwa Ine pamodzi ndi chilichonse chimene chili ndi yisiti, ndipo musasunge nsembe ya pa Chikondwerero cha Paska mpaka mmawa.

26“Muzibwera ndi zipatso zoyambirira kucha zabwino kwambiri ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu.

“Musamaphike kamwana kambuzi mu mkaka wa mayi wake.”

27Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba mawu awa pakuti potsatira mawuwa, ine ndipangana pangano ndi iwe ndi Israeli.” 28Mose anakhala kumeneko pamodzi ndi Yehova masiku 40, usana ndi usiku, wosadya kanthu kapena kumwa madzi. Ndipo iye analemba pa miyala ija mawu a pangano, malamulo khumi.

Nkhope ya Mose Inyezimira

29Mose anatsika kuchokera mʼPhiri la Sinai pamodzi ndi miyala iwiri ija ya pangano mʼmanja mwake. Iye sanazindikire kuti nkhope yake imanyezimira pakuti anayankhula ndi Yehova. 30Aaroni ndi Aisraeli ataona kuti nkhope ya Mose imanyezimira anaopa kumuyandikira. 31Koma Mose anawayitana. Kotero Aaroni ndi atsogoleri onse a gululo anabwera kwa iye, ndipo anawayankhula. 32Kenaka Aisraeli onse anamuyandikira, ndipo anawapatsa malamulo onse omwe Yehova anamupatsa pa Phiri la Sinai.

33Mose atamaliza kuyankhula nawo anaphimba nkhope yake. 34Koma nthawi zonse popita pamaso pa Yehova kukayankhula naye amachotsa chophimbacho mpaka atatuluka. Ndipo akatuluka kudzawuza Aisraeli zimene walamulidwa, 35iwo amaona nkhope yake ikunyezimira. Choncho Mose amaphimba nkhope yake ngakhale pamene amapita kukayankhula ndi Yehova.

New Russian Translation

Исход 34:1-35

Новые каменные плитки

(Втор. 10:1-5)

1Господь сказал Моисею:

– Высеки две каменные плитки, подобные прежним, а Я напишу на них слова, что были на первых плитках, которые ты разбил. 2Утром приготовься и поднимись на гору Синай. Предстань предо Мной на вершине горы. 3Пусть никто не поднимается вместе с тобой и не показывается на горе; даже отарам и стадам нельзя пастись у подножия горы.

4Моисей вытесал две каменные плитки, подобные прежним, и, встав ранним утром, поднялся на гору Синай, как повелел ему Господь. Две каменные плитки он нес в руках. 5Господь спустился в облаке, встал рядом с ним и возвестил имя Господа. 6Он прошел перед Моисеем, провозглашая: «Господь, Господь, сострадательный и милостивый Бог, медленный на гнев, богатый милостью и верностью, 7хранящий милость к тысячам34:7 Или: «к тысячам поколений». и прощающий проступок, отступничество и грех. И все же Он не оставит виновного без наказания; за проступки отцов Он карает детей и внуков до третьего и четвертого поколения».

8Моисей тотчас пал на колени, опустив голову до земли, и 9воскликнул:

– О Владыка, если я нашел у Тебя милость, молю, пусть Владыка пойдет с нами. Хоть этот народ и упрям, прости нам проступки и грехи и возьми нас Себе в удел.

Возобновление завета

10Господь сказал:

– Я заключаю завет: Я совершу перед твоим народом чудеса, каких не бывало прежде ни в каком народе на всей земле. Народ, среди которого ты живешь, увидит, как сильно внушает страх дело Господа, которое Я для тебя совершу. 11Слушайтесь того, что Я повелеваю вам ныне. Я прогоню от вас аморреев, хананеев, хеттов, ферезеев, хиввеев и иевусеев. 12Смотрите, не вступайте в союз с жителями той земли, куда вы идете, иначе они станут для вас западней. 13Разрушьте их жертвенники, разбейте священные камни и срубите столбы Ашеры34:13 Евр.: «ашерим»; по-видимому, символы богини Ашеры.. 14Не поклоняйтесь чужому богу, ведь Господь, чье имя Ревнитель, – ревнивый Бог.

15Смотрите, не вступайте в союз с жителями той земли, потому что, когда они будут распутничать со своими богами и приносить им жертвы, они позовут и вас, и вы станете есть их жертвы. 16Вы станете брать из их народа дочерей в жены своим сыновьям, и их дочери, которые распутничают со своими богами, заставят делать то же самое и ваших сыновей. 17Не делайте себе литых идолов.

18Справляйте праздник Пресных хлебов: семь дней ешьте пресный хлеб, как Я повелел вам, в установленное время месяца авива, потому что в этом месяце вы вышли из Египта.

19Все перворожденное принадлежит Мне, считая самцов-первенцев вашего крупного и мелкого скота. 20Выкупайте первородного осла ягненком, а если не будете выкупать, сломайте ему шею. Выкупайте всех первенцев из ваших сыновей.

Пусть никто не появляется предо Мной с пустыми руками.

21Шесть дней трудитесь, а на седьмой отдыхайте; отдыхайте даже во время пахоты и жатвы.

22Справляйте праздник Недель, когда собираете первый урожай пшеницы, и праздник Сбора плодов34:22 Позже этот праздник стали называть праздником Шалашей (см. Лев. 23:39-43). в конце года. 23Пусть три раза в год все мужчины предстают пред лицо Владыки Господа, Бога Израиля. 24Я прогоню от вас народы и расширю границы ваших земель. Никто не посягнет на вашу землю, когда вы три раза в год будете ходить и представать перед Господом, вашим Богом.

25Когда приносишь Мне жертву, не проливай кровь животного на дрожжевой хлеб, и пусть от жертвы праздника Пасхи ничего не остается до утра.

26Лучшее из первых плодов твоей земли приноси в дом Господа, твоего Бога.

Не вари козленка в молоке его матери.

27Господь сказал Моисею:

– Запиши эти слова – на их основании Я заключаю завет с тобой и с Израилем.

28Моисей пробыл там с Господом сорок дней и сорок ночей; он ничего не ел и не пил. Он написал на плитках слова завета – десять заповедей34:28 Букв.: «десять слов»..

Сияющее лицо Моисея

29Спустившись с горы Синай с двумя каменными плитками свидетельства в руках, Моисей не знал, что его лицо сияет после того, как он поговорил с Господом. 30Когда Аарон и израильтяне увидели, что лицо Моисея сияет, они боялись приблизиться к нему. 31Но Моисей позвал их, и тогда Аарон и вожди народа подошли к нему, и он говорил с ними. 32После этого к нему приблизились израильтяне, и он передал им заповеди, которые Господь дал ему на горе Синай.

33Закончив говорить с ними, Моисей опустил на лицо покрывало. 34Но входя к Господу, чтобы говорить с Ним, он снимал покрывало до тех пор, пока не выходил. Когда он выходил и передавал израильтянам, что ему было велено, 35они видели, что его лицо сияет. Потом Моисей опять опускал на лицо покрывало до тех пор, пока не входил говорить с Господом.