Eksodo 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 3:1-22

Kuyitanidwa kwa Mose pa Chitsamba Choyaka Moto

1Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu. 2Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka. 3Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”

4Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!”

Ndipo anayankha, “Wawa.”

5Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.” 6Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.

7Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo. 8Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. 9Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira. 10Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”

11Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”

12Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”

13Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”

14Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’ ”

15Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.

16“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani. 17Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’

18“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’ 19Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza. 20Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.

21“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu. 22Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

出埃及記 3:1-22

上帝呼召摩西

1摩西為岳父米甸祭司葉忒羅放羊。一天他領著羊群穿越曠野,來到上帝的山——何烈山。 2忽然有耶和華的天使在荊棘裡的火焰中向他顯現。摩西看見荊棘雖然在燃燒,卻沒有被燒毀。 3摩西想:「我要過去看這個奇異的景象,荊棘為什麼沒有被燒掉呢?」 4耶和華上帝見他要上前觀看,就從荊棘叢中呼喚他說:「摩西摩西!」摩西說:「我在這裡。」 5上帝說:「別再靠近,脫下你腳上的鞋子,因為你所站的地方是聖地。」 6又說:「我是你祖先的上帝,是亞伯拉罕的上帝,以撒的上帝,雅各的上帝。」摩西害怕看上帝,就把臉蒙起來。 7耶和華說:「我已經看見我子民在埃及所受的苦難,聽見了他們因監工的壓迫而發出的呼求。我知道他們的痛苦。 8我下來是要從埃及人手中救他們,帶他們離開那裡,到一個遼闊肥沃的奶蜜之鄉,就是現在迦南人、人、亞摩利人、比利洗人、希未人和耶布斯人居住的地方。 9現在,以色列人的呼求傳到我耳中,我也看到了埃及人怎樣壓迫他們。 10現在去吧,我要派你到法老那裡,帶領我的以色列子民離開埃及。」 11摩西對上帝說:「我是誰啊?怎麼能去見法老,把以色列人從埃及領出來呢?」 12上帝說:「我必與你同在,你帶百姓離開埃及後,你們必在這座山上事奉我——這將是我派你去的證據。」 13摩西問上帝:「假如我到以色列人那裡,對他們說,『你們祖先的上帝派我來你們這裡。』他們如果問我,『祂叫什麼名字?』我該怎樣回答他們呢?」 14上帝對摩西說:「我是自有永有者。你要這樣回答以色列人,『那位自有永有者派我到你們這裡。』」 15上帝又對摩西說:「你要告訴以色列人是我派遣你到他們那裡,我是他們祖先的上帝耶和華,是亞伯拉罕的上帝,以撒的上帝,雅各的上帝。耶和華是我的名字,直到永遠,世世代代的人都要這樣稱呼我。 16你去招聚以色列的長老,對他們說,『你們祖先的上帝耶和華,就是亞伯拉罕以撒雅各的上帝向我顯現,說祂關切你們,知道你們在埃及的遭遇。 17祂應許要帶領你們脫離在埃及所受的苦難,到迦南人、人、亞摩利人、比利洗人,希未人和耶布斯人住的地方,那裡是奶蜜之鄉。』 18以色列的長老們必定聽從你的話,你就跟他們一起去見埃及王,對他說,『希伯來人的上帝耶和華向我們顯現。現在請你容許我們走三天的路程,到曠野去,向我們的上帝耶和華獻祭。』 19我也知道除非我用大能的手向他施壓,不然埃及王不會讓你們離開。 20因此,我必伸手行各種神蹟攻擊埃及,之後他必讓你們離開。 21我必使埃及人恩待你們,好叫你們不致空手離開埃及22你們的婦女只管向埃及鄰居及住在鄰居家的婦女索取金器、銀器和衣服,給自己的兒女穿戴,你們必這樣奪取埃及人的財物。」