Eksodo 28 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 28:1-43

Zovala za Ansembe

1“Aaroni mʼbale wako ndi ana ake aamuna, Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara uwapatule pakati pa Aisraeli. Abwere kwa iwe kuti anditumikire monga ansembe. 2Umusokere mʼbale wako, Aaroni, zovala zopatulika kuti azioneka mwaulemerero ndi molemekezeka. 3Uwawuze anthu onse aluso amene Ine ndawapatsa nzeru pa ntchito yosoka kuti apange zovala za Aaroni za pa mwambo womupatula, kuti iye anditumikire monga wansembe. 4Zovala zoti apange ndi izi: chovala chapachifuwa, efodi, mkanjo, mwinjiro wolukidwa, nduwira ndi lamba. Apangire mʼbale wako Aaroni ndi ana ake aamuna zovala zopatulikazi kuti iwo anditumikire monga ansembe. 5Iwo agwiritse ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira ndi yosalala yofewa.

Efodi

6“Apange efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yolukidwa mwaluso. 7Efodiyo ikhale ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga. 8Lamba womangira efodi akhale wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Akhale wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala.

9“Utenge miyala iwiri ya onikisi ndipo uzokotepo mayina a ana a Israeli. 10Mayina asanu ndi limodzi akhale pa mwala umodzi, ndipo mayina asanu ndi limodzi pa mwala winawo motsata mabadwidwe awo. 11Mayina a ana a Israeli uwazokote pa miyala iwiriyo, monga momwe amachitira mmisiri wozokota miyala. Ndipo uyike miyalayo mu zoyikamo zake zagolide. 12Umangirire miyala iwiriyi pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli. Aaroni azinyamula mayinawo mʼmapewa ake kuti akhale chikumbutso pamaso pa Yehova. 13Upange zoyikamo za maluwa agolide, 14ndiponso maunyolo awiri a golide wabwino kwambiri, wopetedwa ngati zingwe ndipo uwalumikize ku zoyikamozo.

Chovala Chapachifuwa

15“Upange chovala chapachifuwa chogwiritsa ntchito poweruza mlandu ndipo uchipange mwaluso kwambiri. Uchipange ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino. 16Kutalika kwake kukhale kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, ndipo chikhale chopinda pawiri. 17Uyikepo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba ukhale ndi miyala ya rubi, topazi ndi berili. 18Mzere wachiwiri pakhale miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi; 19mzere wachitatu pakhale miyala ya opera, agate ndi ametisiti. 20Mzere wachinayi pakhale miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi uyiike mu zoyikamo zagolide. 21Miyalayo ikhalepo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse uzokotedwe ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.

22“Upange timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe. 23Upangenso mphete ziwiri zagolide ndipo uzimangirire pa ngodya ziwiri za pa chovala chapachifuwa. 24Umangirire timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho. 25Ndipo mbali ina ya timaunyoloto umangirire pa zoyikapo zake ziwiri zija ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi. 26Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndipo uzilumikize ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija. 27Upangenso mphete zina ziwiri zagolide ndipo uzilumikize kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi. 28Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.

29“Pamene Aaroni akulowa kumalo opatulika azivala chovala chapachifuwa cha zoweruzira chija chimene chalembedwa mayina a ana a Israeli kuti Yehova awakumbukire nthawi zonse. 30Ndiponso uyike Urimu ndi Tumimu mu chovala chapachifuwa cha zoweruziracho, kuti zikhale pamtima pa Aaroni. Choncho Aaroniyo adzakhala akutenga nthawi zonse zida zomuthandizira kuweruza ana a Israeli pamene adzafika pamaso pa Yehova.

Zovala Zina za Ansembe

31“Uyipangire efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo. 32Mkanjowo ukhala ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo pakhale chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike. 33Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, upange mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira zokhala ndi maberu agolide pakati pake. 34Choncho pazikhala mphonje imodzi kenaka belu limodzi, kuzungulira mpendero wa mkanjo wonse. 35Aaroni azivala mkanjowo pamene akutumikira ngati wansembe. Kulira kwa maberu kuzimveka pamene akulowa mʼmalo opatulika pamaso pa Yehova ndiponso pamene akutuluka, kuti asafe.

36“Upange duwa lagolide wabwino kwambiri kukhala ngati chidindo ndipo uzokotepo mawu akuti, choperekedwa kwa Yehova. 37Ulimange ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira ya Aaroni, ndipo duwalo likhale kutsogolo kwa nduwirayo. 38Lidzakhala pa mphumi ya Aaroni, motero iye adzasenza cholakwa chilichonse cha pa zopereka zilizonse zimene Aisraeli amazipatulira Yehova. Aaroni azivala chikwangwanichi pa mphumi pake nthawi zonse kuti Yehova alandire zopereka za anthu ake.

39“Uluke mwinjiro wa nsalu yofewa yosalala ndiponso upange nduwira ya nsalu yofewa yosalala. Lamba wake akhale wolukidwa bwino ndi munthu waluso. 40Upangirenso ana a Aaroni mwinjiro, malamba ndi nduwira kuti azioneka mwaulemu ndi molemekezeka. 41Zovala zimenezi umuveke Aaroni, mʼbale wako ndi ana ake. Kenaka uwadzoze, uwapatse udindo ndi kuwapatula kuti anditumikire ngati ansembe anga.

42“Uwapangire akabudula a nsalu yofewa oyambira mʼchiwuno kulekeza mʼntchafu kuti asamaonetse maliseche. 43Aaroni ndi ana ake ayenera kuvala akabudulawo pamene akulowa mu tenti ya msonkhano kapena pamene akupita ku guwa lansembe kukatumikira malo oyera kuopa kuti angachimwe ndi kufa.

“Ili likhale lamulo la nthawi zonse kwa Aaroni ndi zidzukulu zake.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

出埃及记 28:1-43

祭司圣衣的规定

1“你要从以色列百姓当中把你的哥哥亚伦和他四个儿子——拿答亚比户以利亚撒以他玛带到你身边,立他们为祭司事奉我。 2你要为你哥哥亚伦做一件圣衣,显出他职位的荣耀和尊贵。 3你要吩咐所有我赋予智慧的巧手裁缝师为亚伦缝制衣服,使他分别出来,做圣洁的祭司事奉我。 4他们要做的圣衣包括胸牌、以弗得、外袍、杂色的内袍、礼冠和腰带。要为你哥哥亚伦及其众子做这样的圣衣,好让他们做祭司事奉我。 5要用金线和细麻线及蓝色、紫色、朱红色的线制作圣衣。

以弗得

6“以弗得要用金线和细麻线及蓝色、紫色、朱红色的线精工制作。 7要在以弗得两边用两条肩带缝合起来。 8用金线和细麻线及蓝色、紫色、朱红色的线精工制作一条带子,缝在以弗得上,连成一整件。

9“你要找两块红玛瑙,刻上以色列十二个儿子的名字, 10按他们的长幼次序,每一块宝石刻上六个名字。 11要用工匠雕刻图章的方法将他们的名字刻在两块宝石上,把宝石镶在两个金框里面。 12然后将镶着金框的宝石缝在以弗得的两条肩带上,作以色列人的纪念石。亚伦要把他们的名字放在肩上,在耶和华面前作纪念。 13要做两个金框, 14并像搓绳子一样用纯金搓成两条金链,把链子连接在镶宝石的金框上。

胸牌

15“要精心制作一个用来明白上帝旨意的胸牌,制作的方法和造以弗得一样,用金线和细麻线及蓝色、紫色、朱红色的线制作。 16胸牌是方形的,长宽各二十二厘米,分成上下两层。 17上面要镶上四行宝石:第一行是红宝石、黄玉和翠玉; 18第二行是绿宝石、蓝宝石和金刚石; 19第三行是紫玛瑙、白玛瑙和紫晶; 20第四行是水苍玉、红玛瑙和碧玉。这些宝石都要用金框围着,镶在胸牌上。 21要用刻图章的方法在每一颗宝石上刻一个以色列儿子的名字,十二颗宝石代表十二支派。

22“要用纯金拧成两条像绳子一样的链子,连在胸牌上, 23造两个金环安在胸牌两端, 24把链子穿在金环上, 25再把金链的另一端接在以弗得肩带的两个金框上。 26造两个金环,安在胸牌下端靠近以弗得内侧的两边。 27再造两个金环安在以弗得前面两条肩带的下端,靠近接缝处,在精致的以弗得腰带上方。 28再用一条蓝色的绳子系住以弗得和胸牌上面的金环,使胸牌贴在精工织成的以弗得腰带上,不会从以弗得上松脱。 29亚伦进圣所时,要佩戴这块刻着以色列众子名字的胸牌,在耶和华面前常作纪念。 30又要把乌陵和土明放在胸牌里面,亚伦到耶和华面前的时候,要佩带这胸牌,以便明白上帝的旨意,为以色列人做决定。

外袍

31“也要缝制一件蓝色的以弗得的外袍, 32袍上要留领口,还要在领口周围织领边,好像铠甲上的领口,免得领口破裂。 33外袍的底边要另外用蓝色、紫色、朱红色的线做成石榴状的饰物,石榴中间要挂金铃铛。 34一个石榴一个金铃铛,相间排列,围在外袍的底边。 35亚伦事奉的时候,要穿上这外袍,以便他进圣所到耶和华面前和出圣所的时候,铃铛会发出响声,他就不至于死。

36“你也要用纯金造一块牌子,以刻印章的方法刻上‘奉献给耶和华’的字样, 37再拿一条蓝色带子,把它系在礼冠前面。 38亚伦要把这金牌戴在额上,表示他承担以色列人献圣物时的过犯,这圣物是以色列百姓特别献上的礼物。这金牌要常常留在亚伦的额上,好使百姓蒙耶和华悦纳。

39“要用杂色的细麻线织成祭司的内袍,用细麻布做礼冠,腰带上要有刺绣, 40也要为亚伦的儿子们缝制内袍、腰带、帽子,显出他们职位的荣耀和尊贵。 41你哥哥亚伦及其众子穿上这些衣服后,你要用油膏立他们,使他们分别出来,做圣洁的祭司事奉我。

裤子

42“要用细麻布为他们做裤子,以遮盖下体,裤子要从腰部到大腿。 43亚伦父子们进出会幕或到圣所的祭坛事奉的时候,都要穿上裤子,免得因为触犯圣礼而死亡。这是亚伦及其子孙永远当遵守的条例。