Deuteronomo 9 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 9:1-29

Osati Chifukwa cha Kulungama kwa Israeli

1Mvera Israeli. Watsala pangʼono kuwoloka Yorodani ndi kukathamangitsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa iweyo, imene mizinda yake ndi ikuluikulu yokhala ndi makoma ofika mpaka kumwamba. 2Anthuwo ndi ataliatali, Aanaki! Ukudziwa za iwo ndipo unamvapo zikunenedwa kuti, “Ndani amene angalimbane ndi Aanaki?” 3Koma khulupirira lero kuti Yehova Mulungu wako amene ali patsogolo pako ali ngati moto wonyeketsa. Adzawononga iwowo ndipo adzawagonjetsa iweyo ukuona. Pamenepo udzawathamangitsa ndi kuwakantha mwamsanga, monga momwe Yehova wakulonjezera.

4Yehova Mulungu wako akadzawapirikitsa pamaso pako, usadzanene mu mtima mwako kuti, “Yehova wandibweretsa kuno kudzalanda dziko lino chifukwa cha kulungama kwanga.” Ayi, koma ndi chifukwa cha kuyipa kwa anthu amene Yehova ati awapirikitse pamaso pako. 5Sukalowa ndi kutenga dziko lawolo chifukwa cha kulungama kwako kapena kukhulupirika kwako koma chifukwa cha kuyipa kwa anthuwo. Yehova Mulungu wako awapirikitsa pamaso pako kuti akwaniritse zimene analumbira kwa makolo ako Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 6Tsono zindikira kuti si chifukwa cha kulungama kwako kuti Yehova Mulungu wako akukupatsa dziko labwinoli kuti ulitenge popeza ndiwe wokanika.

Mwana Wangʼombe Wagolide

7Kumbukirani izi ndipo musayiwale mmene munaputira mkwiyo wa Yehova Mulungu mʼchipululu muja. Kuyambira tsiku limene munatuluka mu Igupto mpaka pamene munafika kuno, mwakhala owukira Yehova. 8Ku Horebu munaputa mkwiyo wa Yehova, kotero kuti anakwiya kwambiri nafuna kukuwonongani. 9Nditakwera ku phiri kuti ndikalandire miyala iwiri ya malamulo, ya pangano limene Yehova anachita ndi inu, ndinakhala ku phiriko kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana, sindinadye buledi kapena kumwa madzi. 10Yehova anandipatsa miyala iwiri yolembedwa ndi chala chake. Pa miyalapo panali malamulo onse amene Yehova analengeza kwa inu pa phiri kuchokera mʼmoto pa tsiku la msonkhano.

11Pakutha pa masiku makumi anayi usiku ndi usana, Yehova anandipatsa miyala iwiri, miyala ya pangano. 12Tsono Yehova anandiwuza, “Tsikako kuno msanga, chifukwa anthu ako aja unawatulutsa ku Iguptowa adziyipitsa. Iwo apatukapo mofulumira pa zimene ndinawalamulira ndipo adzipangira fano lachitsulo.”

13Ndipo Yehova anati kwa ine, “Anthu awa ndawaona ndipo ndi anthu okanikadi! 14Ndilekeni ndiwawononge ndi kufafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi wochuluka kuposa iwo.”

15Choncho ndinatembenuka ndi kutsika phiri moto ukanayakabe. Ndipo miyala iwiri ya pangano inali mʼmanja mwanga. 16Ine poyangʼana ndinaona kuti inu munachimwira Yehova Mulungu wanu. Munadzipangira fano lowumbidwa ngati mwana wangʼombe. Inuyo munapatuka msanga kuchoka pa njira imene Yehova anakulamulirani. 17Motero ine ndinaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwanga, ndi kuyiphwanya inu mukuona.

18Tsono nthawi yomweyo ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana. Sindinadye buledi kapena kumwa madzi chifukwa cha machimo onse amene munawachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kumukwiyitsa kwambiri. 19Ine ndinachita mantha ndi mkwiyo ndi ukali wa Yehova chifukwa anakwiya nanu kokwanira kukuwonongani. Koma Yehova anandimveranso. 20Ndipo Yehova anakwiya ndi Aaroni ndipo akanamuwononga, koma ine ndinamupemphereranso Aaroniyo. 21Ndiponso ndinatenga chinthu chanu choyipacho, mwana wangʼombe amene munapangayo, ndi kumuwotcha pa moto. Kenaka ndinamuphwanya ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi ndipo ndinawaza fumbilo mu mtsinje umene unkayenda kuchokera mʼphiri.

22Inu munamukwiyitsanso Yehova ku Tabera, ku Masa ndi ku Kibiroti Hatava.

23Ndipo Yehova atakutulutsani ku Kadesi Barinea anati, “Pitani mukatenge dziko limene ndakupatsani.” Koma munawukira ulamuliro wa Yehova Mulungu wanu. Inu simunamukhulupirire kapena kumumvera. 24Kuyambira pamene ndinakudziwani, mwakhala owukira Yehova.

25Ine ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku chifukwa Yehova ananena kuti akuwonongani. 26Ndinapemphera kwa Ambuye ndi kuti, “Haa Yehova Wamkulukulu, musawawononge anthu anu, chuma chanuchanu chimene munachipulumutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ku Igupto ndi dzanja lanu la mphamvu. 27Kumbukirani atumiki anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Musatengere kupulupudza, kuyipa ndi kuchimwa kwawo anthuwa. 28Kupanda kutero, ndiye kuti anthu a ku dziko lija munatitulutsaku adzati, ‘Yehova anawatulutsa kuti akawaphe mʼchipululu popeza sanathe kukawalowetsa mʼdziko limene anawalonjeza ndipo anadana nawo.’ 29Koma iwowa ndi anthu anu, chuma chanu chimene munachitulutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ndi mkono wanu wotambasuka.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 9:1-29

以色列人的悖逆

1以色列人啊,你們要聽!今天你們要過約旦河,去趕出那些比你們強大的民族。他們住在城牆高聳入雲的大城裡, 2是長得高大威猛的亞衲人。你們瞭解他們,也聽人說過,『誰能抵擋亞衲人呢?』 3但今天你們要知道,你們的上帝耶和華要走在你們前面,像烈火一樣吞噬他們。祂要制伏他們,使你們迅速趕走他們,毀滅他們,正如祂對你們的應許。

4「你們的上帝耶和華趕走他們以後,你們不要以為耶和華帶領你們佔領那片土地是因為你們公義,其實是因為那裡的民族邪惡,耶和華才將他們從你們面前趕走。 5你們能佔領他們的土地並非因為你們公義、行為正直。你們的上帝耶和華從你們面前趕走那些民族,是因為他們邪惡,也是為了實現祂給你們祖先亞伯拉罕以撒雅各的誓言。 6你們要知道,耶和華賜給你們那佳美之地不是因為你們有好品德。其實你們是頑固不化的人。

7「要牢記你們在曠野怎樣觸怒你們的上帝耶和華。從你們離開埃及那天到現在,你們屢屢背叛耶和華。 8何烈山,你們觸怒了耶和華,以致祂要毀滅你們。 9那時,我上山去接受耶和華與你們立約的石版,在山上待了四十晝夜,不吃也不喝。 10耶和華把兩塊立約的石版交給我,上面刻著那天你們聚會時祂在山上的火焰中對你們說的話,是祂用手指刻上去的。 11四十晝夜後,耶和華把那兩塊刻著約的石版交給我, 12對我說,『快下山吧,你從埃及領出來的百姓已經敗壞了。他們這麼快就偏離了我吩咐他們走的道,為自己鑄造了神像。』

13「耶和華又對我說,『我已看出,這是頑固不化的百姓。 14不要攔我,我要毀滅他們,從世上抹去他們的名字。我要使你的子孫成為一個比他們更強大的民族。』 15我雙手拿著那兩塊石版,轉身從烈火熊熊的山上下來, 16看見你們為自己鑄造了牛犢像,得罪了你們的上帝耶和華,這麼快就偏離了耶和華吩咐你們走的道, 17就當著你們的面摔碎了那兩塊石版。

18「我又俯伏在耶和華面前,四十晝夜不吃不喝,因為你們犯了大罪,做耶和華憎惡的事,惹祂發怒。 19耶和華向你們發烈怒,要毀滅你們,我非常懼怕。但耶和華再次垂聽了我的祈求。 20耶和華對亞倫非常憤怒,以致要殺掉他,於是我也為他祈求。 21我焚燒了你們鑄造的罪惡之物——牛犢像,把它磨成細粉,撒在從山上流下來的溪水中。

22「你們在他備拉瑪撒基博羅·哈他瓦三番四次地觸怒耶和華。 23你們的上帝耶和華吩咐你們離開加低斯·巴尼亞,去佔領祂賜給你們的土地,你們卻背叛祂,不信靠祂,也不聽從祂。 24自從我認識你們以來,你們就不斷地背叛耶和華。

25「因為耶和華說要毀滅你們,我就俯伏在耶和華面前四十晝夜, 26向祂祈求說,『主耶和華啊,求你不要毀滅你的子民!他們是你的產業,是你用大能的手從埃及拯救出來的。 27求你看在你僕人亞伯拉罕以撒雅各的份上,不要計較這個民族的頑固和罪惡, 28免得你帶領我們離開之地的人說,你不能把他們領到你應許給他們的地方,你憎惡他們,所以把他們帶到曠野殺了。 29他們畢竟是你的子民,你的產業,是你伸出大能的臂膀從埃及帶出來的。』