Deuteronomo 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 5:1-33

Malamulo Khumi

1Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati:

Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata. 2Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu. 3Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero. 4Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja. 5(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:

6“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.

7“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.

8“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko. 9Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane, 10koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.

11“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.

12“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira. 13Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi, 14koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo. 15Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.

16“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.

17“Usaphe.

18“Usachite chigololo.

19“Usabe.

20“Usapereke umboni womunamizira mnzako.

21“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”

22Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.

23Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine. 24Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye. 25Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu. 26Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo? 27Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”

28Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino. 29Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.

30“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo. 31Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”

32Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere. 33Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 5:1-33

The Ten Commandments

1Moses sent for all the Israelites. Here is what he said to them.

Israel, listen to me. Here are the rules and laws I’m announcing to you today. Learn them well. Be sure to obey them. 2The Lord our God made a covenant with us at Mount Horeb. 3He didn’t make it only with our people of long ago. He also made it with us. In fact, he made it with all of us who are alive here today. 4The Lord spoke to you face to face. His voice came out of the fire on the mountain. 5At that time I stood between the Lord and you. I announced to you the Lord’s message. I did it because you were afraid of the fire. You didn’t go up the mountain.

The Lord said,

6“I am the Lord your God. I brought you out of Egypt. That is the land where you were slaves.

7“Do not put any other gods in place of me.

8“Do not make statues of gods that look like anything in the sky or on the earth or in the waters. 9Do not bow down to them or worship them. I am the Lord your God. I want you to worship only me. I cause the sins of the parents to affect their children. I will cause the sins of those who hate me to affect even their grandchildren and great-grandchildren. 10But for all time to come I show love to all those who love me and keep my commandments.

11“Do not misuse the name of the Lord your God. The Lord will find guilty anyone who misuses his name.

12“Keep the Sabbath day holy. Do this just as the Lord your God has commanded you. 13Do all your work in six days. 14But the seventh day is a sabbath to honor the Lord your God. Do not do any work on that day. The same command applies to your sons and daughters, your male and female servants, your oxen, your donkeys and your other animals. It also applies to any outsiders who live in your towns. I want your male and female servants to rest, just as you do. 15Remember that you were slaves in Egypt. The Lord your God reached out his mighty hand and powerful arm and brought you out of there. So the Lord your God has commanded you to keep the Sabbath day holy.

16“Honor your father and mother, just as the Lord your God has commanded you. Then you will live a long time in the land he is giving you. And things will go well with you there.

17“Do not murder.

18“Do not commit adultery.

19“Do not steal.

20“Do not be a false witness against your neighbor.

21“Do not want to have your neighbor’s wife. Do not desire anything your neighbor owns. Do not desire to have your neighbor’s house or land, male or female servant, ox or donkey.”

22These are the commandments the Lord announced in a loud voice to your whole community. He gave them to you there on the mountain. He spoke out of the fire, cloud and deep darkness. He didn’t add anything else. Then he wrote the commandments on two stone tablets. And he gave them to me.

23The mountain was blazing with fire. You heard the voice coming out of the darkness. So your elders and all the leaders of your tribes came to me. 24You said, “The Lord our God has shown us his glory and majesty. We have heard his voice coming out of the fire. Today we have seen that a person can still stay alive even if God speaks with them. 25But why should we die? This great fire will burn us up. We’ll die if we hear the voice of the Lord our God again. 26We have heard the voice of the living God. We’ve heard him speaking out of the fire. Has any other human being ever heard him speak like that and stayed alive? 27Go near and listen to everything the Lord our God says. Then tell us what he tells you. We will listen and obey.”

28The Lord heard you when you spoke to me. He said to me, “I have heard what these people said to you. Everything they said was good. 29But I wish they would always have respect for me in their hearts. I wish they would always obey all my commands. Then things would go well with them and their children forever.

30“Go and tell them to return to their tents. 31But you stay here with me. Then I will give you all my commands, rules and laws. You must teach the people to obey them in the land I am giving them as their very own.”

32So be careful to do what the Lord your God has commanded you. Don’t turn away from his commands to the right or the left. 33Live exactly as the Lord your God has commanded you to live. Then you will enjoy life in the land you will soon own. Things will go well with you there. You will live there for a long time.