Deuteronomo 32 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 32:1-52

1Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;

imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.

2Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula

ndipo mawu anga atsike ngati mame,

ngati mvumbi pa udzu watsopano,

ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.

3Ndidzalalikira dzina la Yehova.

Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!

4Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,

njira zake zonse ndi zolungama.

Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa,

Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.

5Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,

iwo si ana akenso,

koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.

6Kodi mukumubwezera Yehova chotere,

inu anthu opusa ndi opanda nzeru?

Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu,

amene anakupangani ndi kukuwumbani?

7Kumbukirani masiku amakedzana;

ganizirani za mibado yakalekale.

Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,

akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.

8Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,

pamene analekanitsa anthu onse,

anayikira malire anthu onse

molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.

9Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,

Yakobo ndiye cholowa chake.

10Anamupeza mʼchipululu,

ku malo owuma ndi kopanda kanthu.

Anamuteteza ndi kumusamalira;

anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,

11ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake

nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,

chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo

ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.

12Yehova yekha ndiye anamutsogolera;

popanda thandizo la mulungu wachilendo.

13Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko

ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.

Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,

ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,

14pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,

ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,

pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani

ndiponso tirigu wabwino kwambiri.

Munamwa vinyo wa thovu lofiira.

15Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;

atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.

Anasiya Mulungu amene anamulenga

ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.

16Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo

ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.

17Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,

milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,

milungu yongobwera kumene,

milungu imene makolo anu sankayiopa.

18Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;

munayiwala Mulungu amene anakubalani.

19Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana

chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.

20Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga,

ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani;

pakuti ndi mʼbado wopotoka,

ana amene ndi osakhulupirika.

21Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu

ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe.

Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake;

ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.

22Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto,

umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa.

Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake

ndipo udzapsereza maziko a mapiri.

23“Ndidzawawunjikira masautso

ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.

24Ndidzawatumizira njala yoopsa,

malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo;

ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta,

ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.

25Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana;

mantha adzalamulira nyumba zawo.

Anyamata ndi atsikana adzafa,

ngakhalenso makanda ndi okalamba.

26Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza

ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,

27koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze,

mwina adani anga sadzandimvetsetsa

ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife;

Yehova sanachite zonsezi.’ ”

28Iwo ndi mtundu wopanda maganizo,

iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.

29Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi

ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!

30Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000

kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse,

Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa,

Yehova akanapanda kuwataya?

31Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,

ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.

32Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu

ndiponso ku minda ya ku Gomora.

Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha

ndipo maphava ake ndi owawa.

33Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka,

ululu woopsa wa mphiri.

34“Kodi zimenezi sindinazisunge

ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?

35Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.

Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera;

tsiku lawo la masautso layandikira

ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”

36Yehova adzaweruza anthu ake

ndipo adzachitira atumiki ake chifundo

pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha

ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.

37Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo,

thanthwe limene ankabisalamo,

38milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo

ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?”

Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni!

Ibwere kuti idzakutetezenitu!

39“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo!

Palibe mulungu wina koma Ine ndekha.

Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo,

ndavulaza ndipo ndidzachiritsa,

ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.

40Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,

‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,

41pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira

ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo,

ndidzabwezera chilango adani anga

ndi kulanga onse odana nane.

42Mivi yanga idzakhuta magazi awo

pamene lupanga langa lidzawononga mnofu:

magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo,

mitu ya atsogoleri a adani.’ ”

43Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,

pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake;

adzabwezera chilango adani ake

ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.

44Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva. 45Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli, 46iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa. 47Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”

Mose Adzafera pa Phiri la Nebo

48Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti, 49“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo. 50Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 51Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli. 52Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

King James Version

Deuteronomy 32:1-52

1Give ear, O ye heavens, and I will speak; and hear, O earth, the words of my mouth. 2My doctrine shall drop as the rain, my speech shall distil as the dew, as the small rain upon the tender herb, and as the showers upon the grass: 3Because I will publish the name of the LORD: ascribe ye greatness unto our God. 4He is the Rock, his work is perfect: for all his ways are judgment: a God of truth and without iniquity, just and right is he. 5They have corrupted themselves, their spot is not the spot of his children: they are a perverse and crooked generation.32.5 They have…: Heb. He hath corrupted to himself32.5 their…: or, that they are not his children, that is their blot 6Do ye thus requite the LORD, O foolish people and unwise? is not he thy father that hath bought thee? hath he not made thee, and established thee?

7¶ Remember the days of old, consider the years of many generations: ask thy father, and he will shew thee; thy elders, and they will tell thee.32.7 many…: Heb. generation and generation 8When the most High divided to the nations their inheritance, when he separated the sons of Adam, he set the bounds of the people according to the number of the children of Israel. 9For the LORD’s portion is his people; Jacob is the lot of his inheritance.32.9 lot: Heb. cord 10He found him in a desert land, and in the waste howling wilderness; he led him about, he instructed him, he kept him as the apple of his eye.32.10 led: or, compassed 11As an eagle stirreth up her nest, fluttereth over her young, spreadeth abroad her wings, taketh them, beareth them on her wings: 12So the LORD alone did lead him, and there was no strange god with him. 13He made him ride on the high places of the earth, that he might eat the increase of the fields; and he made him to suck honey out of the rock, and oil out of the flinty rock; 14Butter of kine, and milk of sheep, with fat of lambs, and rams of the breed of Bashan, and goats, with the fat of kidneys of wheat; and thou didst drink the pure blood of the grape.

15¶ But Jeshurun waxed fat, and kicked: thou art waxen fat, thou art grown thick, thou art covered with fatness; then he forsook God which made him, and lightly esteemed the Rock of his salvation. 16They provoked him to jealousy with strange gods, with abominations provoked they him to anger. 17They sacrificed unto devils, not to God; to gods whom they knew not, to new gods that came newly up, whom your fathers feared not.32.17 not to…: or, which were not God 18Of the Rock that begat thee thou art unmindful, and hast forgotten God that formed thee.

19And when the LORD saw it, he abhorred them, because of the provoking of his sons, and of his daughters.32.19 abhorred: or, despised 20And he said, I will hide my face from them, I will see what their end shall be: for they are a very froward generation, children in whom is no faith. 21They have moved me to jealousy with that which is not God; they have provoked me to anger with their vanities: and I will move them to jealousy with those which are not a people; I will provoke them to anger with a foolish nation. 22For a fire is kindled in mine anger, and shall burn unto the lowest hell, and shall consume the earth with her increase, and set on fire the foundations of the mountains.32.22 shall burn: or, hath burned32.22 shall consume: or, hath consumed 23I will heap mischiefs upon them; I will spend mine arrows upon them. 24They shall be burnt with hunger, and devoured with burning heat, and with bitter destruction: I will also send the teeth of beasts upon them, with the poison of serpents of the dust.32.24 heat: Heb. coals 25The sword without, and terror within, shall destroy both the young man and the virgin, the suckling also with the man of gray hairs.32.25 within: Heb. from the chambers32.25 destroy: Heb. bereave

26I said, I would scatter them into corners, I would make the remembrance of them to cease from among men: 27Were it not that I feared the wrath of the enemy, lest their adversaries should behave themselves strangely, and lest they should say, Our hand is high, and the LORD hath not done all this.32.27 Our…: or, Our high hand, and not the LORD hath done 28For they are a nation void of counsel, neither is there any understanding in them. 29O that they were wise, that they understood this, that they would consider their latter end! 30How should one chase a thousand, and two put ten thousand to flight, except their Rock had sold them, and the LORD had shut them up? 31For their rock is not as our Rock, even our enemies themselves being judges. 32For their vine is of the vine of Sodom, and of the fields of Gomorrah: their grapes are grapes of gall, their clusters are bitter:32.32 of the vine: or, worse than the vine 33Their wine is the poison of dragons, and the cruel venom of asps. 34Is not this laid up in store with me, and sealed up among my treasures? 35To me belongeth vengeance, and recompence; their foot shall slide in due time: for the day of their calamity is at hand, and the things that shall come upon them make haste. 36For the LORD shall judge his people, and repent himself for his servants, when he seeth that their power is gone, and there is none shut up, or left.32.36 power: Heb. hand 37And he shall say, Where are their gods, their rock in whom they trusted, 38Which did eat the fat of their sacrifices, and drank the wine of their drink offerings? let them rise up and help you, and be your protection.32.38 your…: Heb. an hiding for you

39See now that I, even I, am he, and there is no god with me: I kill, and I make alive; I wound, and I heal: neither is there any that can deliver out of my hand. 40For I lift up my hand to heaven, and say, I live for ever. 41If I whet my glittering sword, and mine hand take hold on judgment; I will render vengeance to mine enemies, and will reward them that hate me. 42I will make mine arrows drunk with blood, and my sword shall devour flesh; and that with the blood of the slain and of the captives, from the beginning of revenges upon the enemy. 43Rejoice, O ye nations, with his people: for he will avenge the blood of his servants, and will render vengeance to his adversaries, and will be merciful unto his land, and to his people.32.43 Rejoice…: or, Praise his people, ye nations: or, Sing ye

44¶ And Moses came and spake all the words of this song in the ears of the people, he, and Hoshea the son of Nun.32.44 Hoshea: or, Joshua 45And Moses made an end of speaking all these words to all Israel: 46And he said unto them, Set your hearts unto all the words which I testify among you this day, which ye shall command your children to observe to do, all the words of this law. 47For it is not a vain thing for you; because it is your life: and through this thing ye shall prolong your days in the land, whither ye go over Jordan to possess it. 48And the LORD spake unto Moses that selfsame day, saying, 49Get thee up into this mountain Abarim, unto mount Nebo, which is in the land of Moab, that is over against Jericho; and behold the land of Canaan, which I give unto the children of Israel for a possession: 50And die in the mount whither thou goest up, and be gathered unto thy people; as Aaron thy brother died in mount Hor, and was gathered unto his people: 51Because ye trespassed against me among the children of Israel at the waters of Meribah-Kadesh, in the wilderness of Zin; because ye sanctified me not in the midst of the children of Israel.32.51 Meribah-Kadesh: or, strife at Kadesh 52Yet thou shalt see the land before thee; but thou shalt not go thither unto the land which I give the children of Israel.