Deuteronomo 32 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 32:1-52

1Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;

imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.

2Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula

ndipo mawu anga atsike ngati mame,

ngati mvumbi pa udzu watsopano,

ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.

3Ndidzalalikira dzina la Yehova.

Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!

4Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,

njira zake zonse ndi zolungama.

Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa,

Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.

5Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,

iwo si ana akenso,

koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.

6Kodi mukumubwezera Yehova chotere,

inu anthu opusa ndi opanda nzeru?

Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu,

amene anakupangani ndi kukuwumbani?

7Kumbukirani masiku amakedzana;

ganizirani za mibado yakalekale.

Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,

akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.

8Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,

pamene analekanitsa anthu onse,

anayikira malire anthu onse

molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.

9Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,

Yakobo ndiye cholowa chake.

10Anamupeza mʼchipululu,

ku malo owuma ndi kopanda kanthu.

Anamuteteza ndi kumusamalira;

anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,

11ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake

nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,

chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo

ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.

12Yehova yekha ndiye anamutsogolera;

popanda thandizo la mulungu wachilendo.

13Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko

ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.

Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,

ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,

14pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,

ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,

pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani

ndiponso tirigu wabwino kwambiri.

Munamwa vinyo wa thovu lofiira.

15Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;

atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.

Anasiya Mulungu amene anamulenga

ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.

16Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo

ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.

17Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,

milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,

milungu yongobwera kumene,

milungu imene makolo anu sankayiopa.

18Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;

munayiwala Mulungu amene anakubalani.

19Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana

chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.

20Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga,

ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani;

pakuti ndi mʼbado wopotoka,

ana amene ndi osakhulupirika.

21Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu

ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe.

Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake;

ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.

22Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto,

umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa.

Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake

ndipo udzapsereza maziko a mapiri.

23“Ndidzawawunjikira masautso

ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.

24Ndidzawatumizira njala yoopsa,

malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo;

ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta,

ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.

25Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana;

mantha adzalamulira nyumba zawo.

Anyamata ndi atsikana adzafa,

ngakhalenso makanda ndi okalamba.

26Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza

ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,

27koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze,

mwina adani anga sadzandimvetsetsa

ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife;

Yehova sanachite zonsezi.’ ”

28Iwo ndi mtundu wopanda maganizo,

iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.

29Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi

ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!

30Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000

kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse,

Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa,

Yehova akanapanda kuwataya?

31Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,

ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.

32Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu

ndiponso ku minda ya ku Gomora.

Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha

ndipo maphava ake ndi owawa.

33Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka,

ululu woopsa wa mphiri.

34“Kodi zimenezi sindinazisunge

ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?

35Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.

Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera;

tsiku lawo la masautso layandikira

ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”

36Yehova adzaweruza anthu ake

ndipo adzachitira atumiki ake chifundo

pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha

ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.

37Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo,

thanthwe limene ankabisalamo,

38milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo

ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?”

Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni!

Ibwere kuti idzakutetezenitu!

39“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo!

Palibe mulungu wina koma Ine ndekha.

Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo,

ndavulaza ndipo ndidzachiritsa,

ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.

40Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,

‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,

41pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira

ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo,

ndidzabwezera chilango adani anga

ndi kulanga onse odana nane.

42Mivi yanga idzakhuta magazi awo

pamene lupanga langa lidzawononga mnofu:

magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo,

mitu ya atsogoleri a adani.’ ”

43Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,

pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake;

adzabwezera chilango adani ake

ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.

44Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva. 45Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli, 46iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa. 47Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”

Mose Adzafera pa Phiri la Nebo

48Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti, 49“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo. 50Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 51Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli. 52Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 32:1-52

摩西之歌

1「諸天啊,請留心聽;

大地啊,請聽我說。

2願我的教導如雨降下,

願我的話語如露滴落,

像水滴滋潤嫩草,

像甘霖澆灌草木。

3我要宣揚耶和華的名,

你們要頌讚我們上帝的偉大。

4「祂是磐石,

祂的作為完美,

祂按公義行事,

祂信實可靠,公平正直。

5狡詐、墮落的一代啊,

你們卻對祂不忠,行事敗壞,

不配做祂的兒女。

6愚昧無知的人啊,

你們就這樣報答耶和華嗎?

祂是你們的父,你們的創造主,

祂創造了你們,塑造了你們。

7「要回顧往昔,追溯歷史;

問你們的父親,

他們必回答你們;

問你們的長者,

他們必告訴你們。

8當初,至高者賜萬國產業,

把人類分開,

祂依照天使32·8 天使」希伯來文是「以色列的兒子」。的數目,

為萬族定疆界。

9以色列人屬於耶和華,

雅各是祂的產業。

10「在荒涼的曠野,

在野獸吼叫的荒野,

耶和華找到他們,

庇護他們,看顧他們,

保護他們如同保護眼中的瞳人,

11又如老鷹攪動窩巢,

盤旋在雛鷹之上,展開雙翼,

背著雛鷹飛翔。

12耶和華獨自帶領他們,

身邊沒有外族神明。

13耶和華使他們馳騁在大地的高處,

吃田間的五穀,

磐石中的蜂蜜,

石頭地產的油;

14吃牛酪和羊奶,

肥美的羔羊,

巴珊的綿羊和山羊,

上好的麥子;

喝葡萄汁釀的酒。

15「但耶書崙32·15 耶書崙」是以色列的暱稱。吃飽喝足,

養肥長壯後,就得意忘形,

背棄造他們的上帝,

藐視救他們的磐石。

16他們拜外族的神明,令祂憤恨;

行可憎之事,惹祂發怒。

17他們祭拜的不是真神,

而是鬼魔,

是他們素不認識的新神明,

是他們祖先所不敬畏的。

18他們輕視生他們的磐石,

忘記養他們的上帝。

19「耶和華看見祂兒女的惡行,

就憤然厭棄他們,

20說,『這墮落的子民,

不忠的兒女!

我要掩面不理他們,

看他們的結局如何。

21他們拜假神,讓我憤恨;

供虛無之物,惹我發怒。

我要藉無名之民挑起他們的嫉妒,

用愚昧的國民激起他們的怒氣。

22我的怒火已經點燃,

要燒到陰間的盡頭,

吞滅大地及其出產,

甚至燒毀山的根基。

23『我要使災禍連連臨到他們,

我的箭都射向他們。

24他們必飽受饑荒之苦,

被瘟疫和災禍吞噬,

被猛獸和毒蛇襲擊。

25外有刀劍殺戮,

內有恐懼籠罩,

少男、少女、嬰兒、

老人無一倖免。

26我本要消滅他們,

使世人忘記他們;

27但我不願讓敵人誇口,

宣稱這是他們的勝利,

而非我的作為。』

28以色列人愚昧無知,毫無見識。

29如果他們有智慧,

就能明白這一切、

知道自己的結局。

30若不是他們的磐石賣掉他們,

若不是耶和華拋棄他們,

一人怎能趕散他們千人?

二人怎能擊潰他們萬人?

31我們的敵人也承認他們的磐石不如我們的磐石。

32他們猶如來自所多瑪

長在蛾摩拉的葡萄樹,

結的葡萄粒粒有毒,串串苦澀;

33釀的酒如蛇的毒液,

如眼鏡蛇的毒液。

34「祂說,『我把這一切積存起來,

封在我的倉庫裡。

35伸冤在我,我必報應,

到時候他們必站不住腳,

他們遭禍的日子近了,

他們的末日來了。』

36「耶和華見自己的子民力量衰竭,

奴隸和自由人所剩無幾,

必為他們主持公道,

憐憫祂的僕人。

37祂必說,『你們的神明在哪裡?

庇護你們的磐石在哪裡?

38它們吃你們祭牲的脂肪,

喝你們的奠酒。

讓它們起來幫助你們,

庇護你們吧!

39『你們要知道,

唯有我是上帝;

除我之外,別無他神。

我掌管生死,我打傷、我醫治;

無人能逃出我的掌心。

40我向天伸手,

憑我的永恆起誓,

41我要磨快閃亮的劍,

主持公道,報應仇敵,

懲罰恨我的人。

42我要使我的箭飽飲鮮血,

被殺被擄之人的血;

我的劍要吞噬人肉,

敵人將領的肉。』

43「列邦啊,

你們當與祂的子民一同歡樂!

因為祂要為自己的僕人報血仇,

報應祂的仇敵,

潔淨祂的土地和子民。」

44摩西的兒子約書亞把這首詩歌讀給會眾聽。

摩西的遺囑

45讀完後,摩西又對以色列人說: 46「要謹記我今天警告你們的話,要吩咐你們的子孫謹遵這律法上的話。 47這律法不是空話,而是你們的生命。你們若遵守這律法,就必長住在約旦河對岸你們將要佔領的土地上。」

預言摩西的死

48當天,耶和華對摩西說: 49「你去耶利哥對面的摩押,登上亞巴琳山區的尼波山,觀看我要賜給以色列人作產業的迦南50之後,你會死在山上,歸到你祖先那裡,如亞倫何珥山離世歸祖一樣。 51因為在曠野,在加低斯米利巴泉旁,你和亞倫對我不忠,沒有在以色列人中尊我為聖。 52所以,你只能遠遠地觀看我要賜給以色列人的土地,卻不能進去。」