Deuteronomo 28 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 28:1-68

Madalitso Akumvera

1Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi. 2Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:

3Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.

4Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.

5Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.

6Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.

7Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.

8Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.

9Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake. 10Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani. 11Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.

12Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense. 13Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi. 14Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.

Matemberero Akusamvera

15Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:

16Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.

17Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.

18Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.

19Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.

20Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova. 21Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali. 22Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka. 23Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo. 24Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.

25Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi. 26Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse. 27Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo. 28Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo. 29Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.

30Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake. 31Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa. 32Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako. 33Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse. 34Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu. 35Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.

36Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala. 37Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.

38Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga. 39Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo. 40Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka. 41Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo. 42Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.

43Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi. 44Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.

45Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani. 46Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale. 47Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino, 48chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.

49Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva, 50mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana. 51Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja. 52Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.

53Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani. 54Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo, 55ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse. 56Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi 57zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.

58Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu, 59Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika. 60Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani. 61Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka. 62Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu. 63Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.

64Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo. 65Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika. 66Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu. 67Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona. 68Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

O Livro

Deuteronómio 28:1-68

Bênção para a obediência

(Lv 26.1-13; Dt 7.12-16)

1Se obedecerem inteiramente a estes mandamentos do Senhor, vosso Deus, a todas estas leis que vos estou a declarar hoje, o Senhor, vosso Deus, fará de vocês a maior nação da Terra. 2E são estas as bênçãos que virão sobre vocês:

3Serão abençoados nas povoações, serão abençoados nos campos.

4Terão muitos filhos, serão abundantes as vossas colheitas, terão grandes rebanhos e manadas.

5Será abençoado o teu cesto e a tua masseira de farinha.

6Serão abençoados quando chegarem a um sítio e quando partirem para outro local.

7O Senhor derrotará os vossos inimigos na vossa presença; marcharão juntos contra vocês, mas depois fugirão e se dispersarão em sete direções. 8O Senhor vos abençoará com boas colheitas e com gado saudável, fazendo prosperar tudo quanto fizerem ao chegar à terra que o Senhor, vosso Deus, vos dá. 9Fará de vocês um povo santo que lhe seja consagrado. Isto é o que o Senhor, vosso Deus, vos promete se lhe obedecerem e andarem nos seus caminhos. 10Todas as nações do mundo constatarão que pertencem ao Senhor e sentirão respeito por vocês.

11O Senhor dar-vos-á abundância de boas coisas na terra como prometeu aos vossos antepassados: muitos filhos, muito gado e ricas colheitas. 12Abrirá para os seus tesouros maravilhosos de chuvas dos céus, para vos dar belas colheitas em todas as épocas. Abençoará tudo quanto fizerem e poderão ceder empréstimos a muitas outras nações estrangeiras, sem terem de pedir emprestado a outros. 13Se obedecerem aos mandamentos do Senhor, vosso Deus, que hoje vos dou, o Senhor vos porá à cabeça e não na cauda; terão sempre a supremacia. 14No entanto, cada uma destas bênçãos depende de não se desviarem nem para um lado nem para o outro das leis que hoje vos dou e de nunca adorarem outros deuses.

Consequências da desobediência

(Lv 26.14-39)

15Contudo, se não quiserem ouvir o Senhor, vosso Deus, nem obedecer a estas leis que hoje vos estou a dar, então todas estas maldições cairão sobre vocês.

16Serão malditos nas povoações, serão malditos nos campos.

17Será maldito o teu cesto e a tua masseira de farinha.

18Serão amaldiçoados com madres estéreis, as vossas searas serão malditas, também o vosso gado e os vossos rebanhos serão malditos.

19Serão amaldiçoados quando chegarem a qualquer sítio ou quando partirem.

20Será o próprio Senhor que vos amaldiçoará. Andarão em confusão e tudo o que empreenderem falhará. Até que por fim serão destruídos por causa de se terem esquecido dele. 21Mandar-vos-á a doença até que sejam destruídos da face da terra de que vão tomar posse agora. 22Mandar-vos-á a tuberculose, febre, infeções, pragas e guerra. Queimará as vossas searas, cobrindo-as de míldio. Todas estas devastações vos perseguirão até que todos pereçam. 23Os céus por cima parecerão de bronze e a terra debaixo de vocês será como o ferro. 24A terra ficará seca como o pó, por falta de água, e até as tempestades de pó vos destruirão.

25O Senhor fará com que sejam destruídos pelos vossos inimigos. Avançarão para a batalha, mas acabarão por fugir perante os inimigos no meio da maior confusão; serão sacudidos dum lado para o outro entre as nações da Terra. 26Os vossos corpos mortos servirão de alimento às aves de rapina e aos animais selvagens, e não haverá ninguém para os afugentar.

27O Senhor vos ferirá com úlceras do Egito, com tumores, com escorbuto e com sarna. E para nenhum desses males haverá remédio. 28Mandar-vos-á loucura, cegueira, terrores e pânico. 29Em pleno dia andarão às apalpadelas como um cego em plena escuridão. Não prosperarão em nada do que fizerem. Serão continuamente oprimidos e explorados; nada vos salvará.

30Será um outro indivíduo que virá a casar com a mulher de quem estavam noivos; outra pessoa virá a morar na casa que construíram; outros comerão o fruto das vinhas que plantaram. 31Os vossos bois serão abatidos contra a vossa vontade, à vossa frente, sem que venham a comer a sua carne. Roubar-vos-ão os jumentos na vossa presença e nunca mais os verão. As vossas ovelhas serão dadas aos vossos inimigos; ninguém quererá dar-vos proteção. 32Sob os vossos olhos serão os vossos filhos e filhas levados como escravos. O vosso coração ficará despedaçado pela saudade sem conseguirem ir socorrê-los. 33Uma nação estrangeira, da qual nunca antes tinham ouvido falar, comerá as searas que vos custaram tanto a fazer crescer. Serão sempre oprimidos e esmagados. 34Ficarão loucos por causa da tragédia que verão à vossa volta. 35O Senhor vos cobrirá os joelhos e pernas com chagas incuráveis. Realmente, vocês ficarão cobertos da cabeça aos pés.

36Vocês e o vosso rei serão levados para uma terra que nem vocês nem os vossos antepassados conheceram e durante o exílio chegarão a adorar deuses feitos de madeira e de pedra. 37Tornar-se-ão objeto de horror, um provérbio, uma fábula entre todas as nações, pois o Senhor vos espalhará.

38Semearão muito, mas colherão quase nada, visto que os gafanhotos comerão as vossas colheitas. 39Plantarão vinhas, tratarão delas, mas não chegarão a comer das suas uvas nem a beber do seu vinho, porque serão destruídas por vermes. 40Plantarão oliveiras por toda a parte, mas não haverá azeite bastante sequer para se ungirem! Porque as árvores perderão as azeitonas antes de estarem maduras. 41Os vossos filhos e filhas serão levados para serem escravos. 42Os gafanhotos destruirão as vossas árvores e as vossas vinhas.

43Os estrangeiros no vosso meio tornar-se-ão cada vez mais ricos, enquanto vocês serão cada vez mais pobres. 44Serão eles quem vos emprestará aquilo de que precisam e não vocês a eles. Eles estarão à cabeça e vocês na cauda.

45Todas estas maldições vos seguirão e vos alcançarão, até que sejam destruídos, por terem recusado ouvir o Senhor, vosso Deus, e não terem obedecido aos mandamentos e às leis que vos deu. 46Estes horrores cairão sobre vocês e os vossos descendentes como um sinal. 47Tornar-se-ão escravos dos vossos inimigos, por não terem servido com alegria e satisfação o Senhor, vosso Deus, por tudo o que vos deu. 48O Senhor mandará os vossos inimigos contra vós; terão fome, sede, frio e necessidades em todos os domínios. Um jugo de ferro será posto no vosso pescoço, até que sejam destruídos.

49O Senhor trará uma nação distante que vos cairá em cima como uma águia; uma nação cuja língua não compreenderão; 50gente feroz que não terá compaixão nem de velhos nem de novos. 51Comerão tudo o que é vosso, em casa e nos campos; levarão todo o gado e as colheitas; desaparecerão com os cereias, o vinho novo, o azeite, as crias das vacas e das ovelhas. 52Essa nação sitiará as vossas cidades e derrubará as muralhas, por mais altas que sejam e por muito que pensem que vos protejem. 53Chegarão a comer a carne dos vossos próprios filhos e filhas nesses dias terríveis, que hão de vir, em que estarão cercados.

54Até o mais sensível e delicado se tornará endurecido e mau para com o seu próprio irmão, a sua querida mulher e os filhos que ainda lhe restarem com vida. 55Recusará mesmo deixá-los partilhar da carne que possa estar a devorar, a carne dos seus próprios filhos, porque sente que morre de fome no meio daquele cerco à cidade. 56A mulher mais terna e mais branda, aquela que quase nem assenta os pés no chão, recusará repartir com o seu querido marido, filhos e filhas o que tem para comer. 57Esconderá deles, quando tiver dado à luz, a placenta e a criança que lhe nasceu, para que possa comê-los ela própria; tão terrível será a fome durante esse ataque, e tão terrível a depressão causada pela presença dos inimigos às vossas portas.

58Se recusarem obedecer a todos os mandamentos desta Lei escritos neste livro, negando-se a temer o nome tremendo e glorioso do Senhor, o vosso Deus, 59então o Senhor vos enviará chagas perpétuas, a vocês e aos vossos filhos. 60Mandará todas as doenças e males do Egito que vocês receiam tanto; toda a terra será flagelada dessa maneira. 61E não será tudo! O Senhor trará sobre vocês toda a espécie de doenças e de pragas que existem, mesmo as que não são mencionadas neste livro da Lei, até que sejam destruídos. 62Serão poucos os que ficarão vivos depois disto, ainda que tenham sido tão numerosos como as estrelas do firmamento. É o que vos acontecerá se não quiserem ouvir o Senhor, vosso Deus.

63Da mesma forma que o Senhor se alegrou convosco e fez coisas tão maravilhosas, tendo-vos multiplicado, assim também nesse tempo ele sentir-se-á satisfeito em destruir-vos. E vocês desaparecerão da terra. 64Porque o Senhor vos espalhará entre as nações, duma extremidade à outra da Terra. Lá adorarão os deuses desses povos pagãos, que nem vocês nem os vossos antepassados conheceram, deuses feitos de madeira e de pedra. 65Lá entre essas nações não encontrarão repouso; antes vos dará o Senhor constante desassossego interior, escuridão e corpos esgotados pela tristeza e pelo cansaço. As vossas vidas andarão sempre como que suspensas pela dúvida. 66Viverão noite e dia em temores e nunca chegarão a ter a certeza de poder ver a luz da manhã. 67Ao amanhecer dirão: “Quem dera que já fosse noite!” E ao cair da noite: “Que venha depressa a manhã!” Isto dirão por causa dos terríveis horrores que vos rodeiam. 68Então o Senhor vos mandará de novo para o Egito em navios, viagem que vos tinha prometido que nunca mais haveriam de fazer. Lá vender-se-ão aos vossos próprios inimigos como escravos e ninguém quererá comprar-vos.