Deuteronomo 25 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 25:1-19

1Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa. 2Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake, 3koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.

4Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.

5Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo. 6Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.

7Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.” 8Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,” 9mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.” 10Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.

11Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo, 12muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.

13Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka. 14Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono. 15Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. 16Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.

17Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto. 18Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu. 19Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 25:1-19

1「如果發生糾紛,雙方告上法庭,審判官要判明是非。 2如果有罪的一方被判受鞭打,審判官要命令他當場伏在地上,按罪行輕重受刑。 3最多可以鞭打他四十下。如果超過四十下,你們就是在公開羞辱自己的同胞。

4「牛在踩穀時,不可籠住牠的嘴。

為死亡的兄弟傳宗接代

5「如果兄弟們住在一起,其中一個沒有兒子便死了,死者的妻子不可改嫁給外人。死者的兄弟要盡兄弟的責任娶她為妻。 6她生的第一個兒子要算為死者的兒子,免得死者在以色列絕後。 7如果死者的兄弟不願娶那寡婦,她要到城門口見長老們,告訴他們,『我丈夫的兄弟不肯盡兄弟的責任娶我,不肯為我丈夫留後。』 8長老們要把死者的兄弟召來,與他商談。如果他執意不肯, 9那寡婦要當著眾長老的面,上前脫下他的鞋,吐唾沫在他臉上,說,『這就是不肯為兄弟留後之人的下場。』 10從此以後,他的家在以色列要被稱為『被脫鞋者之家』。

其他條例

11「如果兩個男人打架,其中一人的妻子為幫助丈夫而伸手抓住另外一人的下體, 12就要砍掉她的手,不可憐憫她。

13「你們做買賣時,口袋裡不可有一大一小兩種法碼, 14家裡也不可用一大一小兩種量器。 15你們必須誠實無欺,使用同樣的法碼和量器,以便在你們的上帝耶和華要賜給你們的土地上得享長壽。 16因為你們的上帝耶和華憎惡行事詭詐的人。

滅絕亞瑪力人的命令

17「你們要記住,你們從埃及出來的路上,亞瑪力人是怎樣對待你們的。 18他們趁你們疲憊不堪時,襲擊你們當中掉隊的人,毫不敬畏上帝。 19所以,當你們的上帝耶和華賜給你們那片土地作產業、使你們四境安寧時,要滅絕亞瑪力人,抹去世人對他們的記憶。你們要切記!