Deuteronomo 17 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 17:1-20

1Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.

2Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake, 3ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba, 4ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli, 5mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala. 6Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi. 7Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

Mabwalo a Milandu

8Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 9Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita. 10Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo. 11Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere. 12Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli. 13Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.

Mfumu

14Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,” 15mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli. 16Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.” 17Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.

18Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi. 19Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa. 20Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.

Thai New Contemporary Bible

เฉลยธรรมบัญญัติ 17:1-20

1อย่าถวายแกะหรือวัวที่มีตำหนิหรือพิการแด่พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่าน เพราะเป็นสิ่งที่น่ารังเกียจสำหรับพระองค์

2หากชายหรือหญิงคนใดที่อยู่ท่ามกลางท่านในเมืองใดเมืองหนึ่งที่องค์พระผู้เป็นเจ้าประทานแก่ท่าน ทำสิ่งที่ชั่วในสายพระเนตรของพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านโดยการละเมิดพันธสัญญาของพระองค์ 3ไปนมัสการกราบไหว้พระอื่นๆ ดวงอาทิตย์ ดวงจันทร์ หรือดวงดาว ซึ่งข้าพเจ้าได้สั่งห้ามไว้ 4และมีผู้มาร้องเรียนต่อท่าน ท่านต้องไต่สวนอย่างรอบคอบ หากเป็นจริงและมีข้อพิสูจน์ว่ามีสิ่งที่น่ารังเกียจเช่นนี้เกิดขึ้นในอิสราเอล 5ก็จงนำชายหรือหญิงที่ทำชั่วนั้นออกไปที่ประตูเมือง แล้วเอาหินขว้างให้ตาย 6แต่อย่าประหารใครเมื่อมีพยานเพียงปากเดียว จะต้องมีพยานอย่างน้อยสองหรือสามปาก 7พยานต้องลงมือขว้างก่อน จากนั้นประชาชนจะร่วมขว้างด้วย ท่านต้องขจัดความชั่วร้ายออกไปจากหมู่พวกท่าน

ศาลยุติธรรม

8หากมีคดีความใดยุ่งยากเกินกว่าท่านจะตัดสิน ไม่ว่าเป็นคดีฆ่าคนตายโดยเจตนา คดีฟ้องร้อง หรือคดีทำร้ายร่างกาย จงนำคดีเหล่านั้นไปยังสถานที่ซึ่งพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านจะทรงเลือก 9ไปแจ้งต่อปุโรหิตซึ่งเป็นคนเลวี และแจ้งตุลาการซึ่งประจำการอยู่ในขณะนั้น คนเหล่านี้จะเป็นผู้ไต่สวนและตัดสิน 10ท่านจะต้องปฏิบัติตามคำตัดสินของเขาที่แจ้งท่านในที่ซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงเลือก จงใส่ใจปฏิบัติตามทุกสิ่งที่พวกเขาสั่งท่าน 11จงปฏิบัติตามบทบัญญัติที่พวกเขาสั่งสอนและทำตามคำตัดสินของเขา อย่าหันเหจากสิ่งที่เขาแจ้งท่านไปทางขวาหรือทางซ้าย 12ผู้ใดดูหมิ่นตุลาการหรือปุโรหิตซึ่งปรนนิบัติพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านที่นั่นจะต้องถูกประหาร ท่านจะต้องขจัดความชั่วออกจากอิสราเอล 13ประชาชนทั้งปวงจะได้ยินเรื่องราวแล้วเกรงกลัวและจะไม่กล้าหมิ่นประมาทอีก

กษัตริย์

14เมื่อท่านได้เข้าไปครอบครองและตั้งถิ่นฐานในดินแดนซึ่งพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านประทานแก่ท่านแล้ว และกล่าวว่า “ให้พวกเราตั้งกษัตริย์ปกครองเราเหมือนชนชาติทั้งปวงรอบๆ เรา” 15จงแน่ใจว่าท่านแต่งตั้งคนที่พระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านทรงเลือกให้เป็นกษัตริย์ เขาจะต้องเป็นคนอิสราเอล ไม่ใช่คนต่างด้าว 16กษัตริย์ต้องไม่หาม้ามากมายมาเป็นของตัว หรือส่งคนไปที่อียิปต์เพื่อหาม้ามาเพิ่ม เพราะองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสสั่งไว้ว่า “เจ้าจะต้องไม่หวนกลับไปทางนั้นอีก” 17เขาจะต้องไม่มีภรรยาหลายคน มิฉะนั้นจิตใจของเขาจะหันเหไป และเขาจะต้องไม่สะสมเงินทองไว้มากมาย

18เมื่อเขาขึ้นครองราชย์ ให้เขาคัดลอกบทบัญญัตินี้จากหนังสือม้วนของปุโรหิตผู้เป็นชนเลวี 19บทบัญญัตินี้จะได้อยู่กับเขา ให้เขาอ่านตลอดชีวิต เพื่อเขาจะเรียนรู้ที่จะยำเกรงพระยาห์เวห์พระเจ้าของเขาและใส่ใจที่จะปฏิบัติตามทุกถ้อยคำของบทบัญญัติและกฎหมายเหล่านี้ 20เพื่อเขาจะไม่ถือว่าตัวเองดีกว่าพี่น้องร่วมชาติและหันเหจากบทบัญญัติไปทางขวาหรือทางซ้าย แล้วเขากับวงศ์วานจะได้ครอบครองราชบัลลังก์ในอิสราเอลยาวนานสืบไป