Deuteronomo 11 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 11:1-32

Kukonda ndi Kumvera Yehova

1Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake. 2Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka; 3zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse; 4zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero. 5Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu, 6ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo. 7Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.

8Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani, 9ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi. 10Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba. 11Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba. 12Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.

13Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, 14pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta. 15Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.

16Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira. 17Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani. 18Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu. 19Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka. 20Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu, 21kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.

22Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye 23Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu. 24Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo. 25Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.

26Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu, 27dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero. 28Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe. 29Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala. 30Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala. 31Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo, 32mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 11:1-32

Love and Obey the Lord

1Love the Lord your God. Do what he requires. Always obey his rules, laws and commands. 2Remember today that your children weren’t the ones the Lord your God guided and corrected. They didn’t see his majesty. They weren’t in Egypt when he reached out his mighty hand and powerful arm. 3They didn’t see the signs and the other things he did in Egypt. They didn’t see what he did to Pharaoh, the king of Egypt, and to his whole country. 4They weren’t there when the Lord destroyed the army of Egypt and its horses and chariots. He swept the waters of the Red Sea over the Egyptians while they were chasing you. He wiped them out forever. 5Your children didn’t see what he did for you in the desert before you arrived here. 6They didn’t see what he did to Dathan and Abiram, the sons of Eliab. Eliab was from the tribe of Reuben. The earth opened its mouth right in the middle of the Israelite camp. It swallowed up Dathan and Abiram. It swallowed them up together with their families, tents and every living thing that belonged to them. 7But with your own eyes you saw all the great things the Lord has done.

8So obey all the commands I’m giving you today. Then you will be strong enough to go in and take over the land. You will go across the Jordan River and take the land as your own. 9You will live there for a long time. It’s the land the Lord promised to give to Abraham, Isaac and Jacob and their children after them. He gave his word when he made that promise. The land has plenty of milk and honey. 10You will enter it and take it over. It isn’t like the land of Egypt. That’s where you came from. You planted your seeds there. You had to water them, just as you have to water a vegetable garden. 11But you will soon go across the Jordan River. The land you are going to take over has mountains and valleys in it. It drinks rain from heaven. 12It’s a land the Lord your God takes care of. His eyes always look on it with favor. He watches over it from the beginning of the year to its end.

13So be faithful. Obey the commands the Lord your God is giving you today. Love him. Serve him with all your heart and with all your soul. 14Then the Lord will send rain on your land at the right time. He’ll send rain in the fall and in the spring. You will be able to gather your grain. You will also be able to make olive oil and fresh wine. 15He’ll provide grass in the fields for your cattle. You will have plenty to eat.

16But be careful. Don’t let anyone tempt you to do something wrong. Don’t turn away and worship other gods. Don’t bow down to them. 17If you do, the Lord will be very angry with you. He’ll close up the sky. It won’t rain. The ground won’t produce its crops. Soon you will die. You won’t live to enjoy the good land the Lord is giving you. 18So keep my words in your hearts and minds. Write them down and tie them on your hands as a reminder. Also tie them on your foreheads. 19Teach them to your children. Talk about them when you are at home. Talk about them when you walk along the road. Speak about them when you go to bed. And speak about them when you get up. 20Write them on the doorframes of your houses. Also write them on your gates. 21Then you and your children will live for a long time in the land. The Lord promised to give the land to Abraham, Isaac and Jacob. Your family line will continue as long as the heavens remain above the earth.

22So be careful. Obey all the commands I’m giving you to follow. Love the Lord your God. Live exactly as he wants you to live. Remain true to him. 23Then the Lord will drive out all the nations to make room for you. They are larger and stronger than you are. But you will take their land. 24Every place you walk on will belong to you. Your territory will go all the way from the desert to Lebanon. It will go from the Euphrates River to the Mediterranean Sea. 25No one will be able to stand up against you. The Lord your God will throw the whole land into a panic because of you. He’ll do it everywhere you go, just as he promised you.

26Listen to me. I’m setting a blessing and a curse in front of you today. 27I’m giving you the commands of the Lord your God today. You will be blessed if you obey them. 28But you will be cursed if you don’t obey them. So don’t turn away from the path I’m now commanding you to take. Don’t turn away by worshiping other gods you didn’t know before. 29The Lord your God will bring you into the land to take it over. When he does, you must announce the blessings from Mount Gerizim. You must announce the curses from Mount Ebal. 30As you know, those mountains are across the Jordan River. They are on the west side of the Jordan toward the setting sun. They are near the large trees of Moreh. The mountains are in the territory of the Canaanites, who live in the Arabah Valley near Gilgal. 31You are about to go across the Jordan River. You will enter the land and take it over. The Lord your God is giving it to you. You will take it over and live there. 32When you do, make sure you obey all the rules and laws I’m giving you today.